< Иов 18 >

1 И отвечал Вилдад Савхеянин и сказал:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 когда же положите вы конец таким речам? обдумайте, и потом будем говорить.
“Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
3 Зачем считаться нам за животных и быть униженными в собственных глазах ваших?
Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
4 О ты, раздирающий душу твою в гневе твоем! Неужели для тебя опустеть земле, и скале сдвинуться с места своего?
Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
5 Да, свет у беззаконного потухнет, и не останется искры от огня его.
“Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
6 Померкнет свет в шатре его, и светильник его угаснет над ним.
Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
7 Сократятся шаги могущества его, и низложит его собственный замысел его,
Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
8 ибо он попадет в сеть своими ногами и по тенетам ходить будет.
Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
9 Петля зацепит за ногу его, и грабитель уловит его.
Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
10 Скрытно разложены по земле силки для него и западни на дороге.
Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
11 Со всех сторон будут страшить его ужасы и заставят его бросаться туда и сюда.
Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
12 Истощится от голода сила его, и гибель готова, сбоку у него.
Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
13 Съест члены тела его, съест члены его первенец смерти.
Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
14 Изгнана будет из шатра его надежда его, и это низведет его к царю ужасов.
Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
15 Поселятся в шатре его, потому что он уже не его; жилище его посыпано будет серою.
Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
16 Снизу подсохнут корни его, и сверху увянут ветви его.
Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
17 Память о нем исчезнет с земли, и имени его не будет на площади.
Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
18 Изгонят его из света во тьму и сотрут его с лица земли.
Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
19 Ни сына его, ни внука не будет в народе его, и никого не останется в жилищах его.
Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
20 О дне его ужаснутся потомки, и современники будут объяты трепетом.
Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
21 Таковы жилища беззаконного, и таково место того, кто не знает Бога.
Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”

< Иов 18 >