< Иов 17 >

1 Дыхание мое ослабело; дни мои угасают; гробы предо мною.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 Если бы не насмешки их, то и среди споров их око мое пребывало бы спокойно.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 Заступись, поручись Сам за меня пред Собою! иначе кто поручится за меня?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 Ибо Ты закрыл сердце их от разумения, и потому не дашь восторжествовать им.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 Кто обрекает друзей своих в добычу, у детей того глаза истают.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 Он поставил меня притчею для народа и посмешищем для него.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 Помутилось от горести око мое, и все члены мои, как тень.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Изумятся о сем праведные, и невинный вознегодует на лицемера.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 Но праведник будет крепко держаться пути своего, и чистый руками будет больше и больше утверждаться.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 Выступайте, все вы, и подойдите; не найду я мудрого между вами.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 Дни мои прошли; думы мои - достояние сердца моего - разбиты.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 А они ночь хотят превратить в день, свет приблизить к лицу тьмы.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 Если бы я и ожидать стал, то преисподняя - дом мой; во тьме постелю я постель мою; (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 гробу скажу: ты отец мой, червю: ты мать моя и сестра моя.
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 Где же после этого надежда моя? и ожидаемое мною кто увидит?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 В преисподнюю сойдет она и будет покоиться со мною в прахе. (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Иов 17 >