< Иов 16 >

1 И отвечал Иов и сказал:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 слышал я много такого; жалкие утешители все вы!
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Будет ли конец ветреным словам? и что побудило тебя так отвечать?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 И я мог бы так же говорить, как вы, если бы душа ваша была на месте души моей; ополчался бы на вас словами и кивал бы на вас головою моею;
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 подкреплял бы вас языком моим и движением губ утешал бы.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 Говорю ли я, не утоляется скорбь моя; перестаю ли, что отходит от меня?
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 Но ныне Он изнурил меня. Ты разрушил всю семью мою.
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 Ты покрыл меня морщинами во свидетельство против меня; восстает на меня изможденность моя, в лицо укоряет меня.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 Гнев Его терзает и враждует против меня, скрежещет на меня зубами своими; неприятель мой острит на меня глаза свои.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 Разинули на меня пасть свою; ругаясь бьют меня по щекам; все сговорились против меня.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 Предал меня Бог беззаконнику и в руки нечестивым бросил меня.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 Я был спокоен, но Он потряс меня; взял меня за шею и избил меня и поставил меня целью для Себя.
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 Окружили меня стрельцы Его; Он рассекает внутренности мои и не щадит, пролил на землю желчь мою,
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 пробивает во мне пролом за проломом, бежит на меня, как ратоборец.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 Вретище сшил я на кожу мою и в прах положил голову мою.
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 Лицо мое побагровело от плача, и на веждах моих тень смерти,
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 при всем том, что нет хищения в руках моих, и молитва моя чиста.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 Земля! не закрой моей крови, и да не будет места воплю моему.
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 И ныне вот на небесах Свидетель мой, и Заступник мой в вышних!
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 Многоречивые друзья мои! К Богу слезит око мое.
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 О, если бы человек мог иметь состязание с Богом, как сын человеческий с ближним своим!
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 Ибо летам моим приходит конец, и я отхожу в путь невозвратный.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”

< Иов 16 >