< Иов 11 >

1 И отвечал Софар Наамитянин и сказал:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
2 разве на множество слов нельзя дать ответа, и разве человек многоречивый прав?
“Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
3 Пустословие твое заставит ли молчать мужей, чтобы ты глумился, и некому было постыдить тебя?
Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
4 Ты сказал: суждение мое верно, и чист я в очах Твоих.
Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
5 Но если бы Бог возглаголал и отверз уста Свои к тебе
Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
6 и открыл тебе тайны премудрости, что тебе вдвое больше следовало бы понести! Итак знай, что Бог для тебя некоторые из беззаконий твоих предал забвению.
ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
7 Можешь ли ты исследованием найти Бога? Можешь ли совершенно постигнуть Вседержителя?
“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
8 Он превыше небес, - что можешь сделать? глубже преисподней, - что можешь узнать? (Sheol h7585)
Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
9 Длиннее земли мера Его и шире моря.
Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
10 Если Он пройдет и заключит кого в оковы и представит на суд, то кто отклонит Его?
“Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
11 Ибо Он знает людей лживых и видит беззаконие, и оставит ли его без внимания?
Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
12 Но пустой человек мудрствует, хотя человек рождается подобно дикому осленку.
Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
13 Если ты управишь сердце твое и прострешь к Нему руки твои,
“Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
14 и если есть порок в руке твоей, а ты удалишь его и не дашь беззаконию обитать в шатрах твоих,
ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
15 то поднимешь незапятнанное лице твое и будешь тверд и не будешь бояться.
udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
16 Тогда забудешь горе: как о воде протекшей, будешь вспоминать о нем.
Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
17 И яснее полдня пойдет жизнь твоя; просветлеешь, как утро.
Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
18 И будешь спокоен, ибо есть надежда; ты огражден, и можешь спать безопасно.
Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
19 Будешь лежать, и не будет устрашающего, и многие будут заискивать у тебя.
Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
20 А глаза беззаконных истают, и убежище пропадет у них, и надежда их исчезнет.
Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”

< Иов 11 >