< Исаия 15 >

1 Пророчество о Моаве. - Так! ночью будет разорен Ар-Моав и уничтожен; так! ночью будет разорен Кир-Моав и уничтожен!
Uthenga wonena za Mowabu: Popeza kuti mu usiku umodzi wokha mzinda wa Ari wa ku Mowabu wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha. Mzinda wa Kiri wawonongedwa, wawonongedwa pa usiku umodzi wokha.
2 Он восходит к Баиту и Дивону, восходит на высоты, чтобы плакать; Моав рыдает над Нево и Медевою; у всех их острижены головы, у всех обриты бороды.
Anthu a ku Diboni akupita ku nyumba ya milungu yawo, akupita ku malo awo achipembedzo kukalira; anthu a ku Mowabu akulirira mofuwula mzinda wa Nebo ndi wa Medeba. Mutu uliwonse wametedwa mpala, ndipo ndevu zonse zametedwa.
3 На улицах его препоясываются вретищем; на кровлях его и площадях его все рыдает, утопает в слезах.
Mʼmisewu akuvala ziguduli; pa madenga ndi mʼmabwalo aliyense akulira mofuwula, misozi ili pupupu.
4 И вопит Есевон и Елеала; голос их слышится до самой Иаацы; за ними и воины Моава рыдают; душа его возмущена в нем.
Anthu a ku Hesiboni ndi Eleali akulira mofuwula, mawu awo akumveka mpaka ku Yahazi. Kotero asilikali a ku Mowabu akulira mofuwula, ndipo ataya mtima.
5 Рыдает сердце мое о Моаве; бегут из него к Сигору, до третьей Эглы; восходят на Лухит с плачем; по дороге Хоронаимской поднимают страшный крик;
Inenso ndikulirira Mowabu; chifukwa othawa nkhondo ake akupita akulira ku chikweza cha Luluti mpaka ku Zowari ndi Egilati-Selisiya akupita akulira ku chikweza cha Luhiti, Akulira mosweka mtima pa njira yopita ku Horonaimu; akulira mosweka mtima chifukwa cha chiwonongeko chawo.
6 потому что воды Нимрима иссякли, луга засохли, трава выгорела, не стало зелени.
Madzi a ku Nimurimu aphwa ndipo udzu wauma; zomera zawonongeka ndipo palibe chomera chobiriwira chatsala.
7 Поэтому они остатки стяжания и, что сбережено ими, переносят за реку Аравийскую.
Kotero kuti chuma chomwe anachipeza ndi kuchisunga, achitenga kuti awoloke nacho chigwembe cha Misondozi.
8 Ибо вопль по всем пределам Моава, до Эглаима плач его и до Беэр-Елима плач его;
Kulira kwawo kukumveka mʼdziko lonse la Mowabu; kulira kwawo kosweka mtima kukumveka mpaka ku Egilaimu ndi Beeri-Elimu.
9 потому что воды Димона наполнились кровью, и Я наведу на Димон еще новое - львов на убежавших из Моава и на оставшихся в стране.
Madzi a ku Dimoni afiira ndi magazi, komabe ndidzabweretsa zina zambiri pa Dimoni, mkango woti udzagwire aliyense othawa mu Mowabu ndi aliyense wotsala mʼdzikomo.

< Исаия 15 >