< К Евреям 3 >

1 Итак, братия святые, участники в небесном звании, уразумейте Посланника и Первосвященника исповедания нашего, Иисуса Христа,
Nʼchifukwa chake abale oyera mtima, amenenso munayitanidwa ndi kumwamba, lingalirani za Yesu amene ndi Mtumwi ndi Mkulu wa ansembe wa chikhulupiriro chimene timavomereza.
2 Который верен Поставившему Его, как и Моисей во всем доме Его.
Iye anali wokhulupirika kwa Mulungu amene anamupatsa udindowo, monga momwe Mose anali wokhulupirika mʼnyumba yonse ya Mulungu.
3 Ибо Он достоин тем большей славы пред Моисеем, чем большую честь имеет в сравнении с домом тот, кто устроил его;
Yesu anapezeka woyenera kulandira ulemu waukulu kuposa Mose, monga momwemonso womanga nyumba amalandira ulemu waukulu kuposa nyumbayo.
4 Ибо всякий дом устрояется кем - либо; а устроивший все есть Бог.
Pakuti nyumba iliyonse imamangidwa ndi munthu wina, koma amene anapanga zonse ndi Mulungu.
5 И Моисей верен во всем доме Его, как служитель для засвидетельствования того, что надлежало возвестить.
Mose anali wokhulupirika monga mtumiki mʼnyumba yonse ya Mulungu, kuchitira umboni zimene zidzayankhulidwe mʼtsogolo.
6 А Христос - как Сын в доме его; дом же Его - мы, если только дерзновение и упование, которым хвалимся, твердо сохраним до конца.
Koma Khristu ndi wokhulupirika monga mwana pa nyumba ya Mulungu. Ndipo ndife nyumba yake ngati tipitirire kulimbika mtima ndi kunyadira zomwe tikuyembekerazo.
7 Почему как говорит Дух Святый, “ныне, когда услышите глас Его,
Tsono monga Mzimu Woyera akuti, “Lero mukamva mawu ake,
8 Не ожесточите сердец ваших как во время ропота в день искушения в пустыне,
musawumitse mitima yanu ngati munachitira pamene munawukira, pa nthawi yoyesedwa mʼchipululu.
9 Где искушали меня отцы ваши, испытывали Меня и видели дела мои сорок лет,
Pamene makolo anu anandiputa ndi kundiyesa, ndipo kwa zaka makumi anayi anaona zimene Ine ndinachita.
10 Посему Я вознегодовал на оный род и сказал: непрестанно заблуждают сердцем, не познали они путей Моих;
Nʼchifukwa chake ndinawukwiyira mʼbadowo, ndipo Ine ndinati, ‘Nthawi zonse mitima yawo imasochera, ndipo iwo sadziwa njira zanga.’
11 Посему Я поклялся во гневе Моем, что они не войдут в покой мой”.
Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti, ‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’”
12 Смотрите, братия чтобы не было в ком из вас сердца лукавого и неверного, дабы вам не отступить от Бога живого.
Abale samalani, kuti pasapezeke wina aliyense mwa inu wokhala ndi mtima woyipa ndi wosakhulupirira, womulekanitsa ndi Mulungu wamoyo.
13 Но наставляйте друг друга каждый день доколе можно говорить “ныне”, чтобы кто из вас не ожесточился, обольстившись грехом.
Koma muzilimbikitsana tsiku ndi tsiku, ikanalipo nthawi imene imatchedwa kuti “Lero” kuti aliyense wa inu mtima wake usawumitsidwe ndi chinyengo cha tchimo.
14 Ибо мы сделались причастниками Христу, если только начатую жизнь сохраним до конца,
Pakuti timakhala anzake a Khristu, ngati tigwiritsitsa mpaka potsiriza chitsimikizo chimene tinali nacho pachiyambi.
15 Доколе говорится: “ныне, когда услышите глас Его, не ожесточите сердец ваших, как во время ропота”.
Monga kunanenedwa kuti, “Lero ngati mumva mawu ake, musawumitse mitima yanu ngati momwe munachitira pamene munawukira.”
16 Ибо некоторые из слышавших возроптали, но не все вышедшие из Египта с Моисеем.
Nanga amene anamva ndi kuwukira anali ndani? Kodi si onse amene Mose anawatulutsa mu Igupto?
17 На кого же негодовал он сорок лет? Не на согревших ли, которых кости пали в пустыне?
Nanga amene Mulungu anawakwiyira zaka makumi anayi anali ndani? Kodi si anthu amene anachimwa, amene mitembo yawo inatsala mʼchipululu muja?
18 Против кого же клялся, что не войдут в покой Его, как не против непокорных?
Nanga Mulungu ankanena za ndani kuti sadzalowa mu mpumulo wake? Pajatu ankanena za anthu amene sanamvere aja.
19 И так видим, что они не могли войти за неверие.
Tsono ife tikuona kuti sanalowe chifukwa cha kusakhulupirika kwawo.

< К Евреям 3 >