< К Евреям 2 >

1 Посему, мы должны быть особенно внимательны к слышанному, чтобы не отпасть.
Nʼchifukwa chake, ife tiyenera kusamalira kwambiri zimene tinamva, kuopa kuti pangʼono ndi pangʼono tingazitaye.
2 Ибо, если чрез Ангелов возвещенное слово было твердо, и всякое преступление и непослушание получало праведное воздаяние,
Popeza uthenga umene unayankhulidwa kudzera mwa angelo unali okhazikika ndithu, choncho aliyense amene ananyozera ndi kusamvera analandira chilango choyenera.
3 то как мы избежим, вознерадевши о толиком спасении, которое, быв сначала проповедано Господом, в нас утвердилось слышавшими от Него,
Nanga ife tidzapulumuka bwanji tikapanda kusamala chipulumutso chachikulu chotere? Ambuye ndiye anayamba kuyankhula za chipulumutsochi, kenaka amenenso anamvawo anatitsimikizira.
4 при засвидетельствовании от Бога знамениями и чудесами, различными силами, и раздаянием Духа Святого по Его воле!
Mulungu anachitiranso umboni pochita zizindikiro, zinthu zodabwitsa ndi zamphamvu zamitundumitundu ndi powapatsa mphatso za Mzimu Woyera monga mwachifuniro chake.
5 Ибо не Ангелам Бог покорил будущую вселенную, о которой говорил;
Mulungu sanapereke kwa angelo ulamuliro wa dziko limene likubwerali, limene ife tikulinena.
6 Напротив, некто негде засвидетельствовал, говоря: “Что значит человек, что Ты помнишь его? или сын человеческий, что Ты посещаешь его?
Koma palipo pena pamene wina anachitira umboni kuti, “Kodi munthu ndani kuti muzimukumbukira, kapena mwana wa munthu kuti muzimusamalira?
7 Немного Ты унизил его пред Ангелами; славою и честью увенчал его и поставил его над делами рук Твоих;
Munamuchepetsa pangʼono kusiyana ndi angelo; munamupatsa ulemerero ndi ulemu.
8 Все покорил под ноги его”. Когда же покорил ему все, то не оставил ничего не покоренным ему. Ныне же еще не видим, чтобы все было ему покорено;
Munamupatsa ulamuliro pa zinthu zonse.” Poyika zinthu zonse pansi pa ulamuliro wake, Mulungu sanasiye kanthu kamene sikali mu ulamuliro wake. Koma nthawi ino sitikuona zinthu pansi pa ulamuliro wake.
9 Но видим, что за претерпение смерти увенчан славою и честью Иисус, который немного был унижен пред Ангелами, дабы Ему по благодати Божией, вкусить смерть за всех.
Koma tikuona Yesu, amene kwa kanthawi kochepa anamuchepetsa pangʼono kwa angelo, koma tsopano wavala ulemerero ndi ulemu chifukwa anamva zowawa za imfa, kuti mwachisomo cha Mulungu, Iye afere anthu onse.
10 Ибо надлежало, чтобы Тот, для Которого все и от Которого все, приводящего многих сынов в славу, Вождя спасения их совершил через страдания.
Mulungu amene analenga zinthu zonse ndipo zinthu zonse zilipo chifukwa cha Iye ndi mwa Iye, anachiona choyenera kubweretsa ana ake ambiri mu ulemerero. Kunali koyenera kudzera mʼnjira ya zowawa, kumusandutsa Yesu mtsogoleri wangwiro, woyenera kubweretsa chipulumutso chawo.
11 Ибо Освящающий и освящаемые, все - от Единого; поэтому Он не стыдится называть их братиями, говоря:
Popeza iye amene ayeretsa ndi oyeresedwa onse ndi abanja limodzi. Nʼchifukwa chake Yesu sachita manyazi kuwatcha iwo abale ake.
12 “Возвещу имя Твое братиям Моим, посреди церкви воспою Тебя”.
Iye akuti, “Ine ndidzawuza abale anga za dzina lanu. Ndidzakuyimbirani nyimbo zamatamando pamaso pa mpingo.”
13 И еще: “Я буду уповать на Него”. И еще: “Вот Я и дети, которых дал Мне Бог”.
Ndiponso, “Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.” Ndiponso Iye akuti, “Ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Mulungu wandipatsa.”
14 А как дети причастны плоти и крови, то и Он также воспринял оные, дабы смертью лишить силы имеющего державу смерти, то есть, диавола,
Tsono popeza kuti anawo ndi anthu, okhala ndi mnofu ndi magazi, Yesu nayenso anakhala munthu ngati iwowo kuti kudzera mu imfa yake awononge Satana amene ali ndi mphamvu yodzetsa imfa.
15 и избавить тех, которые от страха смерти всю жизнь были подвержены рабству.
Pakuti ndi njira yokhayi imene Iye angamasule amene pa moyo wawo wonse anali ngati akapolo chifukwa choopa imfa.
16 Ибо не Ангелов восприемлет Он, но восприемлет семя Авраамово.
Pakuti tikudziwanso kuti sathandiza angelo, koma zidzukulu za Abrahamu.
17 Посему Он должен был во всем уподобиться братиям, чтоб быть милостивым и верным Первосвященником пред Богом, для умилостивления за грехи народа,
Chifukwa cha zimenezi, Iye anayenera kukhala wofanana ndi abale ake pa zonse, kuti akhale mkulu wa ansembe wachifundo ndi wokhulupirika potumikira Mulungu, kuti potero achotse machimo a anthu.
18 Ибо, как Сам Он претерпел, быв искушен, то может и искушаемым помочь.
Popeza Iye mwini anamva zowawa pamene anayesedwa, Iyeyo angathe kuthandiza amene akuyesedwanso.

< К Евреям 2 >