< Иезекииль 23 >

1 И было ко мне слово Господне:
Yehova anandiyankhula nati:
2 сын человеческий! были две женщины, дочери одной матери,
“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
3 и блудили они в Египте, блудили в своей молодости; там измяты груди их, и там растлили девственные сосцы их.
Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
4 Имена им: большой - Огола, а сестре ее - Оголива. И были они Моими, и рождали сыновей и дочерей; и именовались - Огола Самариею, а Оголива Иерусалимом.
Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 И стала Огола блудить от Меня и пристрастилась к своим любовникам, к Ассириянам, к соседям своим,
“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
6 к одевавшимся в ткани яхонтового цвета, к областеначальникам и градоправителям, ко всем красивым юношам, всадникам, ездящим на конях;
Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
7 и расточала блудодеяния свои со всеми отборными из сынов Ассура, и оскверняла себя всеми идолами тех, к кому ни пристращалась;
Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
8 не переставала блудить и с Египтянами, потому что они с нею спали в молодости ее и растлевали девственные сосцы ее, и изливали на нее похоть свою.
Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
9 За то Я и отдал ее в руки любовников ее, в руки сынов Ассура, к которым она пристрастилась.
“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
10 Они открыли наготу ее, взяли сыновей ее и дочерей ее, а ее убили мечом. И она сделалась позором между женщинами, когда совершили над нею казнь.
Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
11 Сестра ее, Оголива, видела это, и еще развращеннее была в любви своей, и блужение ее превзошло блужение сестры ее.
“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
12 Она пристрастилась к сынам Ассуровым, к областеначальникам и градоправителям, соседям ее, пышно одетым, к всадникам, ездящим на конях, ко всем отборным юношам.
Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
13 И Я видел, что она осквернила себя, и что у обеих их одна дорога.
Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
14 Но эта еще умножила блудодеяния свои, потому что, увидев вырезанных на стене мужчин, красками нарисованные изображения Халдеев,
“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
15 опоясанных по чреслам своим поясом, с роскошными на голове их повязками, имеющих вид военачальников, похожих на сынов Вавилона, которых родина земля Халдейская,
atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
16 она влюбилась в них по одному взгляду очей своих и послала к ним в Халдею послов.
Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
17 И пришли к ней сыны Вавилона на любовное ложе, и осквернили ее блудодейством своим, и она осквернила себя ими; и отвратилась от них душа ее.
Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
18 Когда же она явно предалась блудодеяниям своим и открыла наготу свою, тогда и от нее отвратилась душа Моя, как отвратилась душа Моя от сестры ее.
Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
19 И она умножала блудодеяния свои, вспоминая дни молодости своей, когда блудила в земле Египетской;
Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
20 и пристрастилась к любовникам своим, у которых плоть - плоть ослиная, и похоть, как у жеребцов.
Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
21 Так ты вспомнила распутство молодости твоей, когда Египтяне жали сосцы твои из-за девственных грудей твоих.
Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
22 Посему, Оголива, так говорит Господь Бог: вот, Я возбужу против тебя любовников твоих, от которых отвратилась душа твоя, и приведу их против тебя со всех сторон:
“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
23 сынов Вавилона и всех Халдеев, из Пехода, из Шоа и Коа, и с ними всех сынов Ассура, красивых юношей, областе-начальников и градоправителей, сановных и именитых, всех искусных наездников.
Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
24 И придут на тебя с оружием, с конями и колесницами и с множеством народа, и обступят тебя кругом в латах, со щитами и в шлемах, и отдам им тебя на суд, и будут судить тебя своим судом.
Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
25 И обращу ревность Мою против тебя, и поступят с тобою яростно: отрежут у тебя нос и уши, а остальное твое от меча падет; возьмут сыновей твоих и дочерей твоих, а остальное твое огнем будет пожрано;
Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
26 и снимут с тебя одежды твои, возьмут наряды твои.
Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
27 И положу конец распутству твоему и блужению твоему, принесенному из земли Египетской, и не будешь обращать к ним глаз твоих, и о Египте уже не вспомнишь.
Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
28 Ибо так говорит Господь Бог: вот, Я предаю тебя в руки тех, которых ты возненавидела, в руки тех, от которых отвратилась душа твоя.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
29 И поступят с тобою жестоко, и возьмут у тебя все, нажитое трудами, и оставят тебя нагою и непокрытою, и открыта будет срамная нагота твоя, и распутство твое, и блудодейство твое.
Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
30 Это будет сделано с тобою за блудодейство твое с народами, которых идолами ты осквернила себя.
zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
31 Ты ходила дорогою сестры твоей; за то и дам в руку тебе чашу ее.
Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
32 Так говорит Господь Бог: ты будешь пить чашу сестры твоей, глубокую и широкую, и подвергнешься посмеянию и позору, по огромной вместительности ее.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
33 Опьянения и горести будешь исполнена: чаша ужаса и опустошения - чаша сестры твоей, Самарии!
Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
34 И выпьешь ее, и осушишь, и черепки ее оближешь, и груди твои истерзаешь: ибо Я сказал это, говорит Господь Бог.
Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
35 Посему так говорит Господь Бог: так как ты забыла Меня и отвратилась от Меня, то и терпи за беззаконие твое и за блудодейство твое.
“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
36 И сказал мне Господь: сын человеческий! хочешь ли судить Оголу и Оголиву? выскажи им мерзости их;
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
37 ибо они прелюбо-действовали, и кровь на руках их, и с идолами своими прелюбодействовали, и сыновей своих, которых родили Мне, через огонь проводили в пищу им.
Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
38 Еще вот что они делали Мне: оскверняли святилище Мое в тот же день, и нарушали субботы Мои;
Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
39 потому что, когда они заколали детей своих для идолов своих, в тот же день приходили в святилище Мое, чтобы осквернять его: вот как поступали они в доме Моем!
Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
40 Кроме сего посылали за людьми, приходившими издалека; к ним отправляли послов, и вот, они приходили, и ты для них умывалась, сурьмила глаза твои и украшалась нарядами,
“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
41 и садились на великолепное ложе, перед которым приготовляем был стол и на котором предлагала ты благовонные курения Мои и елей Мой.
Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
42 И раздавался голос народа, ликовавшего у нее, и к людям из толпы народной вводимы были пьяницы из пустыни; и они возлагали на руки их запястья и на головы их красивые венки.
“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
43 Тогда сказал Я об одряхлевшей в прелюбодействе: теперь кончатся блудодеяния ее вместе с нею.
Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
44 Но приходили к ней, как приходят к жене блуднице, так приходили к Оголе и Оголиве, к распутным женам.
Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
45 Но мужи праведные будут судить их; они будут судить их судом прелюбодейц и судом проливающих кровь, потому что они прелюбодейки, и у них кровь на руках.
Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
46 Ибо так сказал Господь Бог: созвать на них собрание и предать их озлоблению и грабежу.
“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
47 И собрание побьет их камнями, и изрубит их мечами своими, и убьет сыновей их и дочерей их, и домы их сожжет огнем.
Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
48 Так положу конец распутству на сей земле, и все женщины примут урок, и не будут делать срамных дел подобно вам;
“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
49 и возложат на вас ваше распутство, и понесете наказание за грехи с идолами вашими, и узнаете, что Я Господь Бог.
Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”

< Иезекииль 23 >