< Исход 37 >

1 И сделал Веселеил ковчег из дерева ситтим; длина его два локтя с половиною, ширина его полтора локтя и высота его полтора локтя;
Bezaleli anapanga Bokosi la Chipangano lamatabwa amtengo wa mkesha. Kutalika kwake kunali masentimita 114, mulifupi mwake munali masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69.
2 и обложил его чистым золотом внутри и снаружи и сделал вокруг него золотой венец;
Iye analikuta bokosilo ndi golide wabwino kwambiri mʼkati mwake ndi kunja komwe. Anapanganso mkombero wagolide kuzungulira bokosilo.
3 и вылил для него четыре кольца золотых, на четырех нижних углах его: два кольца на одной стороне его и два кольца на другой стороне его.
Iye anapanga mphete zinayi zagolide ndi kuzimangirira ku miyendo yake inayi ija, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri.
4 И сделал шесты из дерева ситтим и обложил их золотом;
Kenaka anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide.
5 и вложил шесты в кольца, по сторонам ковчега, чтобы носить ковчег.
Ndipo analowetsa nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira.
6 И сделал крышку из чистого золота: длина ее два локтя с половиною, а ширина полтора локтя.
Iye anapanga chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69.
7 И сделал двух херувимов из золота: чеканной работы сделал их на обоих концах крышки,
Ndipo anapanga Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo ndi kuwayika mbali ziwiri za chivundikirocho.
8 одного херувима с одного конца, а другого херувима с другого конца: выдавшимися из крышки сделал херувимов с обоих концов ее;
Iye anapanga kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa anawapangira limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo.
9 и были херувимы с распростертыми вверх крыльями и покрывали крыльями своими крышку, а лицами своими были обращены друг к другу; к крышке были лица херувимов.
Mapiko a Akerubiwo anatambasukira pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo anakhala choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho.
10 И сделал стол из дерева ситтим длиною в два локтя, шириною в локоть и вышиною в полтора локтя,
Iwo anapanga tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69.
11 и обложил его золотом чистым, и сделал вокруг него золотой венец;
Kenaka analikuta ndi golide wabwino kwambiri, ndipo anapanga mkombero wagolide mʼmbali mwake.
12 и сделал вокруг него стенки в ладонь и сделал золотой венец у стенок его;
Iwo anapanga feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo anayika mkombero wagolide kuzungulira feremuyo.
13 и вылил для него четыре кольца золотых и утвердил кольца на четырех углах, у четырех ножек его;
Iwo anapanga mphete zinayi zagolide ndipo anazilumikiza ku ngodya zake zinayi, kumene kunali miyendo yake inayi.
14 при стенках были кольца, чтобы влагать шесты для ношения стола;
Mphetezo anaziyika kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo.
15 и сделал шесты из дерева ситтим и обложил их золотом для ношения стола.
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo.
16 Потом сделал сосуды, принадлежавшие к столу: блюда, кадильницы, кружки и чаши, чтобы возливать ими, из чистого золота.
Ndipo anapanga ziwiya za pa tebulolo zagolide wabwino, mbale ndi zipande, mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe za chakumwa.
17 И сделал светильник из золота чистого, чеканный сделал светильник; стебель его, ветви его, чашечки его, яблоки его и цветы его выходили из него;
Iwo anapanga choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zinasulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zinapangidwa kumodzi.
18 шесть ветвей выходило из боков его: три ветви светильника из одного бока его и три ветви светильника из другого бока его;
Mʼmbali mwake munali mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse.
19 три чашечки были наподобие миндального цветка, яблоко и цветы на одной ветви, и три чашечки наподобие миндального цветка, яблоко и цветы на другой ветви: так на всех шести ветвях, выходящих из светильника;
Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zinali pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri panalinso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zinali chimodzimodzi ndipo zinatuluka mʼchoyikapo nyalecho.
20 а на стебле светильника было четыре чашечки наподобие миндального цветка с яблоками и цветами;
Pa choyikapo nyalecho panali zikho zinayi zokhala ngati maluwa amtowo, mphukira ndi maluwa ake.
21 у шести ветвей, выходящих из него, яблоко под первыми двумя ветвями, и яблоко под вторыми двумя ветвями, и яблоко под третьими двумя ветвями;
Mphukira yoyamba inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Mphukira yachitatu inali mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zinali nthambi zisanu ndi imodzi
22 яблоки и ветви их выходили из него; весь он был чеканный, цельный, из чистого золота.
Mphukira ndi nthambi zonse zinasulidwa kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.
23 И сделал к нему семь лампад, и щипцы к нему и лотки к нему, из чистого золота;
Iwo anapanga nyale zisanu ndi ziwiri, mbaniro ndi zowolera phulusa, zonse zinali zagolide wabwino kwambiri.
24 из таланта чистого золота сделал его со всеми принадлежностями его.
Iwo anapanga choyikapo nyale ndi zipangizo zake zonse zagolide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34.
25 И сделал жертвенник курения из дерева ситтим: длина его локоть и ширина его локоть, четырехугольный, вышина его два локтя; из него выходили роги его;
Iwo anapanga guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Linali lofanana mbali zonse, mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91, ndipo nyanga zake zinapangidwa kumodzi ndi guwalo.
26 и обложил его чистым золотом, верх его и стороны его кругом, и роги его, и сделал к нему золотой венец вокруг;
Iwo anakuta guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse ndi nyanga zake, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira guwalo.
27 под венцом его на двух углах его сделал два кольца золотых; с двух сторон его сделал их, чтобы вкладывать в них шесты для ношения его;
Anapanga mphete ziwiri pansi pa mkomberowo ndi kulumikiza ku mbali zonse ziwiri kuti apisemo nsichi zonyamulira.
28 шесты сделал из дерева ситтим и обложил их золотом.
Anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndipo anayikuta ndi golide.
29 И сделал миро для священного помазания и курение благовонное, чистое, искусством составляющего масти.
Iwo anapanganso mafuta opatulika odzozera ndi zofukiza za fungo lokoma kwambiri. Iyi inali ntchito ya mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa.

< Исход 37 >