< Исход 26 >

1 Скинию же сделай из десяти покрывал крученого виссона и из голубой, пурпуровой и червленой шерсти, и херувимов сделай на них искусною работою;
“Panga chihema pogwiritsa ntchito nsalu khumi zofewa, zosalala ndi zolukidwa bwino, zobiriwira, zapepo ndi zofiira. Ndipo anthu aluso apete pa nsaluzo Akerubi.
2 длина каждого покрывала двадцать восемь локтей, а ширина каждого покрывала четыре локтя: мера одна всем покрывалам.
Nsalu zonse zikhale zofanana. Mulitali mwake zikhale mamita khumi ndi atatu, mulifupi mamita awiri.
3 Пять покрывал пусть будут соединены одно с другим, и другие пять покрывал соединены одно с другим.
Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi. Uchite chimodzimodzi ndi nsalu zisanu zinazo.
4 Сделай к ним петли голубого цвета на краю первого покрывала, в конце соединяющего обе половины; так сделай и на краю последнего покрывала, соединяющего обе половины;
Panga zokolowekamo za nsalu yobiriwira mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsiriza ya mbali ina. Uchitenso chimodzimodzi ndi nsalu yotsiriza ya mbali inayo.
5 пятьдесят петлей сделай у одного покрывала и пятьдесят петлей сделай на краю покрывала, которое соединяется с другим; петли должны соответствовать одна другой;
Upange zokolowekamo 50 pa nsalu yoyamba ndi zokolowekamo makumi asanu zinanso pa nsalu inayo. Upange motero kuti zokolowekamozo ziziyangʼanana.
6 и сделай пятьдесят крючков золотых и крючками соедини покрывала одно с другим, и будет скиния одно целое.
Kenaka upange ngowe zagolide makumi asanu zolumikizira nsalu ziwirizo kuti zipange chihema chimodzi.
7 И сделай покрывала на козьей шерсти, чтобы покрывать скинию; одиннадцать покрывал сделай таких;
“Upange nsalu za ubweya wambuzi zophimba pamwamba pa chihemacho. Nsalu zonse pamodzi zikhale khumi ndi imodzi.
8 длина одного покрывала тридцать локтей, а ширина четыре локтя; это одно покрывало: одиннадцати покрывалам одна мера.
Nsalu zonse khumi ndi imodzi zikhale zofanana. Mulitali mwake mukhale mamita khumi ndi anayi ndipo mulifupi mwake mukhale mamita awiri.
9 И соедини пять покрывал особо и шесть покрывал особо; шестое покрывало сделай двойное с передней стороны скинии.
Ulumikize nsalu zisanu kuti ikhale nsalu imodzi ndipo zina zisanu ndi imodzi uzilumikizenso kuti ikhale nsalu imodzinso. Nsalu yachisanu ndi chimodzi imene ili kutsogolo kwa tenti uyipinde pawiri.
10 Сделай пятьдесят петлей на краю крайнего покрывала, для соединения его с другим, и пятьдесят петлей сделай на краю другого покрывала, для соединения с ним;
Upange zokolowekamo 50 mʼmphepete mwa nsalu imodzi yotsirizira ya nsalu yoyamba yolumikiza ija. Upangenso zokolowekamo zina 50 mʼmphepete mwa nsalu yotsirizira ya nsalu inanso yolumikiza ija.
11 сделай пятьдесят крючков медных, и вложи крючки в петли, и соедини покров, чтобы он составлял одно.
Kenaka upange ngowe 50 zamkuwa ndipo uzilowetse mu zokolowekazo. Ndiye uphatikize nsalu ziwirizo kuti tentiyo ikhale imodzi.
12 А излишек, остающийся от покрывал скиний, - половина излишнего покрывала пусть будет свешена на задней стороне скинии;
Theka lotsalira la nsaluyo lidzalendewera kumbuyo kwa chihemacho.
13 а излишек от длины покрывал скинии, на локоть с одной и на локоть с другой стороны, пусть будет свешен по бокам скинии с той и с другой стороны, для покрытия ее.
Nsalu yotsalira ya masentimita 46 mulitali mwake mʼmbali zonse ziwiri idzalendewere kuphimba mbali ziwirizo.
14 И сделай покрышку для покрова из кож бараньих красных и еще покров верхний из кож синих.
Upange chikopa cha nkhosa zazimuna cha utoto wofiira chophimbira tentiyo ndipo pamwamba pake upangireponso chophimbira china cha zikopa za akatumbu.
15 И сделай брусья для скинии из дерева ситтим, чтобы они стояли:
“Upange maferemu amatabwa amtengo wa mkesha oyimikira chihemacho.
16 длиною в десять локтей сделай брус, и полтора локтя каждому брусу ширина;
Feremu iliyonse ikhale yotalika mamita anayi ndipo mulifupi mwake mukhale masentimita 69.
17 у каждого бруса по два шипа на концах, один против другого: так сделай у всех брусьев скинии.
Thabwa lililonse likhale ndi zolumikizira ziwiri. Upange maferemu onse a chihemacho ndi matabwa otere.
18 Так сделай брусья для скинии: двадцать брусьев для полуденной стороны к югу,
Upange maferemu makumi awiri a mbali yakummwera kwa chihemacho.
19 и под двадцать брусьев сделай сорок серебряных подножий: два подножия под один брус для двух шипов его, и два подножия под другой брус для двух шипов его;
Ndipo upange matsinde 40 asiliva ndipo uwayike pansi pa maferemuwo. Pansi pa feremu iliyonse pakhale matsinde awiri ogwiriziza zolumikizira ziwiri zija.
20 и двадцать брусьев для другой стороны скинии к северу,
Ndipo mbali yakumpoto ya chihemacho upangenso maferemu makumi awiri.
21 и для них сорок подножий серебряных: два подножия для двух шипов его под один брус, и два подножия под другой брус для двух шипов его;
Upangenso matsinde 40 asiliva, awiri pansi pa feremu iliyonse.
22 для задней же стороны скинии к западу сделай шесть брусьев
Upange maferemu asanu ndi imodzi a kumbuyo kwa tenti, kumbali yakumadzulo.
23 и два бруса сделай для углов скинии на заднюю сторону;
Ndipo upangenso maferemu awiri a pa ngodya yakumbuyo kwenikweni kwa tenti.
24 они должны быть соединены внизу и соединены вверху к одному кольцу: так должно быть с ними обоими; для обоих углов пусть они будут;
Pa ngodya ziwirizi pakhale maferemu awiri, kuyambira pansi mpaka pamwamba ndipo alumikizidwe pa ngowe imodzi. Maferemu onse akhale ofanana.
25 и так будет восемь брусьев, и для них серебряных подножий шестнадцать: два подножия под один брус, и два подножия под другой брус для двух шипов его.
Choncho pakhale maferemu asanu ndi atatu ndiponso matsinde 16 asiliva, awiri akhale pansi pa feremu iliyonse.
26 И сделай шесты из дерева ситтим, пять шестов для брусьев одной стороны скинии,
“Upange mitanda ya matabwa amtengo wa mkesha: mitanda isanu ikhale ya maferemu a mbali imodzi ya chihema,
27 и пять шестов для брусьев другой стороны скинии, и пять шестов для брусьев задней стороны сзади скинии, к западу;
mitanda isanu inanso ikhale ya maferemu a mbali inayo. Pakhalenso mitanda ina isanu ya mbali yakumadzulo, kumapeto kwenikweni kwa chihema.
28 а внутренний шест будет проходить по средине брусьев от одного конца до другого;
Mtanda wapakati pa maferemuwo uchokere pa maferemu a mbali ina mpaka mbali inanso.
29 брусья же обложи золотом, и кольца, для вкладывания шестов, сделай из золота, и шесты обложи золотом.
Maferemuwo uwakute ndi golide ndiponso upange mphete zagolide zogwiriziza mitandayo. Ndipo mitandayonso uyikute ndi golide.
30 И поставь скинию по образцу, который показан тебе на горе.
“Upange chihema mofanana ndi momwe ndinakuonetsera pa phiri paja.
31 И сделай завесу из голубой, пурпуровой и червленой шерсти и крученого виссона; искусною работою должны быть сделаны на ней херувимы;
“Upange nsalu yokhala ndi mtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira ndipo nsaluyo ikhale yolukidwa bwino, yofewa ndi yosalala. Ndipo anthu aluso apetepo zithunzi za Akerubi.
32 и повесь ее на четырех столбах из ситтим, обложенных золотом, с золотыми крючками, на четырех подножиях серебряных;
Nsaluyo uyikoloweke pa nsanamira zinayi zamtengo wa mkesha zokutidwa ndi golide zomwe zili ndi ngowe zagolide, zomwe zayima pa matsinde asiliva anayi.
33 и повесь завесу на крючках и внеси туда за завесу ковчег откровения; и будет завеса отделять вам святилище от Святаго-святых.
Ukoloweke kataniyo ku ngowe ndipo uyike Bokosi la Chipangano mʼkatimo. Kataniyo idzalekanitse malo wopatulika ndi malo wopatulika kwambiri.
34 И положи крышку на ковчег откровения во Святом-святых.
Uyike chivundikiro pa bokosi laumboni ku malo wopatulika kwambiri.
35 И поставь стол вне завесы и светильник против стола на стороне скинии к югу; стол же поставь на северной стороне скинии.
Uyike tebulo kunja kwa katani yotchinga cha kumpoto kwa chihema ndipo uyike choyikapo nyale chija kummwera moyangʼanana ndi tebulolo.
36 И сделай завесу для входа в скинию из голубой и пурпуровой и червленой шерсти и из крученого виссона узорчатой работы;
“Pa chipata cholowera mu chihema, uyikepo nsalu yamtundu wamtambo, wapepo ndi ofiira, yomwe ndi yofewa ndi yosalala, yopetedwa bwino ndi amisiri aluso.
37 и сделай для завесы пять столбов из ситтим и обложи их золотом; крючки к ним золотые; и вылей для них пять подножий медных.
Upange ngowe zagolide za nsaluyo ndi nsanamira zisanu zamtengo wa mkesha ndipo uzikute ndi golide. Upangenso matsinde asanu amkuwa a nsanamirazo.”

< Исход 26 >