< К Ефесянам 6 >

1 Дети, повинуйтесь своим родителям в Господе, ибо сего требует справедливость.
Inu ana, mverani makolo anu mwa Ambuye, pakuti zimenezi ndi zoyenera.
2 Почитай отца твоего и мать, это первая заповедь с обетованием:
“Lemekeza abambo ndi amayi ako.” Limeneli ndi lamulo loyamba lokhala ndi lonjezo.
3 да будет тебе благо, и будешь долголетен на земле.
Ngati ulemekeza abambo ako ndi amayi ako, “zinthu zidzakuyendera bwino ndipo udzasangalala ndi moyo wautali pa dziko lapansi.”
4 И вы, отцы, не раздражайте детей ваших, но воспитывайте их в учении и наставлении Господнем.
Abambo musakwiyitse ana anu; mʼmalo mwake, muwalere mʼchiphunzitso ndi mʼchilangizo cha Ambuye.
5 Рабы, повинуйтесь господам своим по плоти со страхом и трепетом, в простоте сердца вашего, как Христу,
Inu antchito, mverani mabwana anu mwaulemu ndi mwamantha ndi moona mtima, monga momwe mungamvere Khristu.
6 не с видимою только услужливостью, как человекоугодники, но как рабы Христовы, исполняя волю Божию от души,
Musawamvere pamene akukuonani kuti akukomereni mtima, koma ngati akapolo a Khristu ochita chifuniro cha Mulungu kuchokera mu mtima mwanu.
7 служа с усердием, как Господу, а не как человекам,
Tumikirani ndi mtima wonse, ngati kuti mukutumikira Ambuye, osati anthu.
8 зная, что каждый получит от Господа по мере добра, которое он сделал, раб ли или свободный.
Inu mukudziwa kuti Ambuye adzamupatsa munthu aliyense mphotho chifukwa cha ntchito yake yabwino imene anagwira, kaya munthuyo ndi kapolo kapena mfulu.
9 И вы, господа, поступайте с ними так же, умеряя строгость, зная, что и над вами самими и над ними есть на небесах Господь, у Которого нет лицеприятия.
Ndipo inu mabwana, muziwachitiranso chimodzimodzi antchito anu. Musamawaopseze, popeza mukudziwa kuti Mbuye wawo ndi wanunso, nonse Mbuye wanu ali kumwamba, ndipo Iyeyo alibe tsankho.
10 Наконец, братия мои, укрепляйтесь Господом и могуществом силы Его.
Potsiriza ndikuti, dzilimbitseni mwa Ambuye ndi mwa mphamvu zake zazikulu.
11 Облекитесь во всеоружие Божие, чтобы вам можно было стать против козней диавольских,
Valani zida zonse za Mulungu kuti muthe kuyima ndi kukana machenjerero a Satana.
12 потому что наша брань не против крови и плоти, но против начальств, против властей, против мироправителей тьмы века сего, против духов злобы поднебесных. (aiōn g165)
Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. (aiōn g165)
13 Для сего приимите всеоружие Божие, дабы вы могли противостать в день злый и, все преодолев, устоять.
Choncho valani zida zonse za Mulungu, kuti pamene tsiku loyipa kwambiri lifika, mudzathe kuyima chilili, ndipo mutatha kuchita zonse, mudzayimabe mwamphamvu.
14 Итак станьте, препоясав чресла ваши истиною, и облекшись в броню праведности,
Tsono imani mwamphamvu, mutamangira choonadi ngati lamba mʼchiwuno mwanu, mutavala chilungamo ngati chitsulo chotchinjiriza pa chifuwa.
15 и обув ноги в готовность благовествовать мир;
Valani Uthenga Wabwino wamtendere ku mapazi anu ngati nsapato.
16 а паче всего возьмите щит веры, которым возможете угасить все раскаленные стрелы лукавого;
Kuwonjezera pa zonsezi, nyamulani chishango cha chikhulupiriro, ndipo ndi chimenechi mudzatha kuzimitsa mivi yonse yoyaka moto ya oyipayo.
17 и шлем спасения возьмите, и меч духовный, который есть Слово Божие.
Valani chipewa cha chipulumutso ndi kutenga lupanga la mzimu, limene ndi Mawu a Mulungu.
18 Всякою молитвою и прошением молитесь во всякое время духом и старайтесь о сем самом со всяким постоянством и молением о всех святых
Ndipo mupemphere mwa Mzimu nthawi zonse, mʼmitundu yonse ya mapemphero ndi zopempha. Ndipo pozindikira izi, khalani achangu kupempherera oyera mtima nthawi zonse.
19 и о мне, дабы мне дано было слово - устами моими открыто с дерзновением возвещать тайну благовествования,
Mundipempherere inenso, kuti nthawi iliyonse pamene nditsekula pakamwa panga, andipatse mawu kuti ndiwulule zinsinsi za Uthenga Wabwino mopanda mantha.
20 для которого я исполняю посольство в узах, дабы я смело проповедывал, как мне должно.
Ndine kazembe wa Uthenga Wabwinowu ngakhale ndili womangidwa mʼndende. Pempherani kuti ndilalikire mopanda mantha, monga ndiyenera.
21 А дабы и вы знали о моих обстоятельствах и делах, обо всем известит вас Тихик, возлюбленный брат и верный в Господе служитель,
Tukiko, mʼbale wanga wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye, adzakuwuzani zonse kuti inunso mudziwe mmene ndilili ndi zimene ndikuchita.
22 которого я и послал к вам для того самого, чтобы вы узнали о нас и чтобы он утешил сердца ваши.
Ine ndikumutumiza kwa inu, kuti mudziwe za moyo wathu, ndi kuti akulimbikitseni.
23 Мир братиям и любовь с верою от Бога Отца и Господа Иисуса Христа.
Mtendere, chikondi pamodzi ndi chikhulupiriro kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi abale onse.
24 Благодать со всеми, неизменно любящими Господа нашего Иисуса Христа. Аминь
Chisomo kwa onse amene amakonda Ambuye athu Yesu Khristu ndi chikondi chosatha.

< К Ефесянам 6 >