< К Колоссянам 4 >

1 Господа, оказывайте рабам должное и справедливое, зная, что и вы имеете Господа на небесах.
Mabwana, antchito anu muzikhala nawo mwachilungamo ndi moyenera, podziwa kuti nanunso muli nawo Ambuye anu mmwamba.
2 Будьте постоянны в молитве, бодрствуя в ней с благодарением.
Pempherani modzipereka, mukhale atcheru ndiponso oyamika.
3 Молитесь также и о нас, чтобы Бог отверз нам дверь для слова, возвещать тайну Христову, за которую я и в узах,
Ndipo muzitipemphereranso ife kuti Mulungu atitsekulire khomo la uthenga wathu, kuti tilalikire chinsinsi cha Khristu, chimene ndine womangidwa nacho mʼndende.
4 дабы я открыл ее, как должно мне возвещать.
Pempherani kuti ndilalikire momveka bwino, monga ndikuyenera.
5 Со внешними обходитесь благоразумно, пользуясь временем.
Mayendedwe anu pakati pa akunja, akhale anzeru ndipo mugwiritse ntchito mpata uliwonse umene muli nawo.
6 Слово ваше да будет всегда с благодатию, приправлено солью, дабы вы знали, как отвечать каждому.
Mayankhulidwe anu nthawi zonse akhale odzaza ndi chisomo ndi okoma, kuti mudziwe kuyankha aliyense.
7 О мне все скажет вам Тихик, возлюбленный брат и верный служитель и сотрудник в Господе,
Tukiko adzakuwuzani zonse za ine. Iye ndi mʼbale wokondedwa, mtumiki wokhulupirika ndiponso wantchito mnzanga mwa Ambuye.
8 которого я для того послал к вам, чтобы он узнал о ваших обстоятельствах и утешил сердца ваши,
Ine ndikumutumiza kwa inu ndi cholinga choti mudziwe zimene tikukumana nazo ndiponso kuti alimbikitse mitima yanu.
9 с Онисимом, верным и возлюбленным братом нашим, который от вас. Они расскажут вам о всем здешнем.
Iye akubwera ndi Onesimo, mʼbale wathu wokhulupirika ndi wokondedwa, amene ndi mmodzi mwa inu. Iwo adzakuwuzani zonse zimene zikuchitika kuno.
10 Приветствует вас Аристарх, заключенный вместе со мною, и Марк, племянник Варнавы о котором вы получили приказания: если придет к вам, примите его,
Aristariko, wamʼndende mnzanga akupereka moni, Marko akuperekanso moni, msuweni wa Barnaba. (Inu munawuzidwa kale za Iye. Iye akabwera kwanuko, mulandireni).
11 также Иисус, прозываемый Иустом, оба из обрезанных. Они единственные сотрудники для Царствия Божия, бывшие мне отрадою.
Yesu wotchedwa Yusto, akuperekanso moni. Amenewa ndi Ayuda okhawo pakati pa atumiki anzanga mu ufumu wa Mulungu, ndipo aonetsa kuti ndi chitonthozo kwa ine.
12 Приветствует вас Епафрас ваш, раб Иисуса Христа, всегда подвизающийся за вас в молитвах, чтобы вы пребыли совершенны и исполнены всем, что угодно Богу.
Epafra ndi mmodzi mwa inu ndiponso mtumiki wa Khristu Yesu, akupereka moni. Iyeyu nthawi zonse amakupemphererani mwamphamvu, kuti mukhazikike pa chifuniro chonse cha Mulungu, mukhale okhwima ndi otsimikiza kwathunthu.
13 Свидетельствую о нем, что он имеет великую ревность и заботу о вас и о находящихся в Лаодикии и Иераполе.
Ine ndikumuchitira umboni kuti amagwira ntchito mwamphamvu chifukwa cha inu ndiponso kwa amene ali ku Laodikaya ndi Herapoli.
14 Приветствует вас Лука, врач возлюбленный, и Димас.
Luka, dotolo wathu wokondedwa ndi Dema, akupereka moni.
15 Приветствуйте братьев в Лаодикии, и Нимфана, и домашнюю церковь его.
Perekani moni kwa abale a ku Laodikaya, ndiponso kwa Numfa ndi mpingo wa mʼnyumba mwake.
16 Когда это послание прочитано будет у вас, то распорядитесь, чтобы оно было прочитано и в Лаодикийской церкви; а то, которое из Лаодикии, прочитайте и вы.
Kalata iyi ikawerengedwa pakati panu, muonetsetse kuti ikawerengedwenso ku mpingo wa ku Laodikaya ndipo inunso muwerenge kalata yochokera ku Laodikaya.
17 Скажите Архиппу: смотри, чтобы тебе исполнить служение, которое ты принял в Господе.
Uzani Arkipo kuti, “Wonetsetsa kuti wamaliza ntchito imene unayilandira mwa Ambuye.”
18 Приветствие моею рукою Павловою. Помните мои узы. Благодать со всеми вами. Аминь.
Ine Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa moni uwu. Kumbukirani kuti ndili mu unyolo. Chisomo chikhale ndi inu.

< К Колоссянам 4 >