< 2-я Паралипоменон 31 >

1 И по окончании всего этого, пошли все Израильтяне, там находившиеся, в города Иудейские и разбили статуи, срубили посвященные дерева, и разрушили высоты и жертвенники во всей Иудее и в земле Вениаминовой, Ефремовой и Манассииной, до конца. И потом возвратились все сыны Израилевы, каждый во владение свое, в города свои.
Zonse zitatha, Aisraeli onse amene anali kumeneko anapita ku mizinda ya ku Yuda, nakaphwanya miyala yachipembedzo ndi kudula mitengo ya mafano a Asera. Iwo anakawononga malo achipembedzo ndi maguwa ansembe amene anali mʼdziko lonse la Yuda, Benjamini, Efereimu ndi Manase. Atawononga zonsezi, Aisraeli anabwerera ku mizinda yawo ndi ku malo awo.
2 И поставил Езекия череды священников и левитов, по их распределению, каждого при деле своем, священническом или левитском, при всесожжении и при жертвах мирных, для службы, для хваления и славословия, у ворот дома Господня.
Hezekiya anakhazikitsa magulu a ansembe ndi Alevi, gulu lililonse monga mwa ntchito zawo ngati ansembe kapena Alevi, kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, kutumikira, kuyamikira ndi kuyimba matamando pa zipata za ku malo okhala Yehova.
3 И определил царь часть из имущества своего на всесожжения: на всесожжения утренние и вечерние, и на всесожжения в субботы и в новомесячия, и в праздники, как написано в законе Господнем.
Kuchokera pa chuma chake, mfumu inapereka nsembe zopsereza za mmawa ndi madzulo ndiponso nsembe zopsereza za pa Chikondwerero cha Masabata, Chikondwerero cha Mwezi Watsopano ndipo inakhazikitsa zikondwerero monga zinalembedwera mʼmalamulo a Yehova.
4 И повелел он народу, живущему в Иерусалиме, давать определенное содержание священникам и левитам, чтоб они были ревностны в законе Господнем.
Iyo inalamula anthu amene amakhala mu Yerusalemu kupereka gawo lawo kwa ansembe ndi Alevi kuti iwowo adzipereke ku malamulo a Yehova.
5 Когда обнародовано было это повеление, тогда нанесли сыны Израилевы множество начатков хлеба, вина, и масла, и меду, и всяких произведений полевых; и десятин из всего нанесли множество.
Lamuloli atangolilengeza, Aisraeli anapereka mowolowamanja zipatso zoyamba kucha za tirigu, vinyo watsopano, mafuta ndi uchi ndi zonse zomwe nthaka yawo inabereka. Anabweretsa zochuluka kwambiri, chakhumi cha chilichonse.
6 И Израильтяне и Иудеи, живущие по городам Иудейским, также представили десятины из крупного и мелкого скота и десятины из пожертвований, посвященных Господу Богу их; и наложили груды, груды.
Aisraeli ndi Ayuda amene amakhala mʼmizinda ya Yuda anabweretsanso chakhumi cha ngʼombe zawo ndi nkhosa ndi chakhumi cha zinthu zoyera zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wawo, ndipo anaziyika mʼmilumilu.
7 В третий месяц начали класть груды, и в седьмой месяц кончили.
Anayamba kuchita izi mwezi wachitatu ndipo anatsiriza mwezi wachisanu ndi chiwiri.
8 И пришли Езекия и вельможи, и увидели груды, и благодарили Господа и народ Его Израиля.
Hezekiya ndi akuluakulu ake atabwera ndi kuona miluyo, anatamanda Yehova ndi kudalitsa anthu ake, Aisraeli.
9 И спросил Езекия священников и левитов об этих грудах.
Hezekiya anafunsa ansembe ndi Alevi za miluyi;
10 И отвечал ему Азария первосвященник из дома Садокова и сказал: с того времени, как начали носить приношения в дом Господень, мы ели досыта, и многое осталось, потому что Господь благословил народ Свой. Из оставшегося составилось такое множество.
ndipo Azariya, mkulu wa ansembe, ochokera ku banja la Zadoki anayankha kuti, “Kuyambira pamene anthu anayamba kubweretsa zopereka zawo ku Nyumba ya Yehova ife takhala ndi zokwanira kudya ndi zina zambiri zosunga, chifukwa Yehova wadalitsa anthu ake, ndipo mulu umenewu ndiye zotsala.”
11 И приказал Езекия приготовить комнаты при доме Господнем. И приготовили.
Hezekiya analamula kuti akonze zipinda zosungiramo za mʼNyumba ya Yehova, ndipo izi zinachitika.
12 И перенесли туда приношения, и десятины, и пожертвования, со всею точностью. И был начальником при них Хонания левит, и Симей, брат его, вторым.
Ndipo iwo mokhulupirika anabweretsa zopereka, chakhumi ndi mphatso zopatulika. Konaniya Mlevi ndiye amayangʼanira zinthu zimenezi ndipo mʼbale wake Simei ndiye anali wachiwiri wake.
13 А Иехиил и Азазия, и Нахаф и Асаил, и Иеримоф и Иозавад, и Елиел и Исмахия, и Махаф и Бенания были смотрителями под рукою Хонании и Симея, брата его, по распоряжению царя Езекии и Азарии, начальника при доме Божием.
Yehieli, Azaziya, Nahati, Asaheli, Yerimoti, Yozabadi, Elieli, Isimakiya, Mahati ndi Benaya anali oyangʼanira motsogozedwa ndi Konaniya ndi Simei, mʼbale wake. Iwowa anasankhidwa ndi mfumu Hezekiya ndi Azariya mkulu woyangʼanira Nyumba ya Mulungu.
14 Коре, сын Имны, левит, привратник на восточной стороне, был при добровольных приношениях Богу, для выдачи принесенного Господу и важнейших из вещей посвященных.
Kore mwana wa Imuna Mlevi, mlonda wa Chipata Chakummawa, amayangʼanira zopereka zaufulu kwa Mulungu, ankagawa zopereka za kwa Yehova ndiponso mphatso zopatulika.
15 И под его ведением находились Еден, и Миниамин, и Иешуа, и Шемаия, и Амария и Шехания в городах священнических, чтобы верно раздавать братьям своим части, как большому, так и малому,
Edeni, Miniyamini, Yesuwa, Semaya, Amariya, Sekaniya amamuthandiza mokhulupirika mʼmizinda yonse a ansembe kugawira kwa ansembe anzawo monga mwa magulu awo, aakulu ndi aangʼono omwe.
16 сверх списка их, всем мужеского пола от трех лет и выше, всем ходящим в дом Господа для дел ежедневных, для служения их, по должностям их и по отделам их,
Kuwonjezera apa, amagawira ana aamuna a zaka zitatu kapena kupitirira amene mayina awo anali mʼmbiri ya mibado yawo, amene adzalowe mʼNyumba ya Yehova kugwira ntchito za tsiku ndi tsiku za magulu awo, molingana ndi udindo ndi magulu awo.
17 и внесенным в список священникам, по поколениям их, и левитам от двадцати лет и выше, по должностям их, по отделам их,
Ndipo anazigawa kwa ansembe amene analembetsa mayina awo mwa mbiri ya mabanja awo, chimodzimodzinso Alevi amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirira molingana ndi udindo wawo ndi magulu awo.
18 и внесенным в список, со всеми малолетними их, с женами их и с сыновьями их и с дочерями их, - всему обществу, ибо они со всею верностью посвятили себя на священную службу.
Iwo anaphatikizanso ana onse aangʼono, akazi ndiponso ana aamuna ndi ana aakazi a gulu lonse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado yawo iyi, pakuti anakhulupirika pa kudzipatula okha.
19 И для сынов Аароновых, священников в селениях вокруг городов их, при каждом городе поставлены были мужи поименованные, чтобы раздавать участки всем мужеского пола у священников и всем внесенным в список у левитов.
Kunena za ansembe, zidzukulu za Aaroni, amene amakhala mʼminda yozungulira mizinda yawo kapena mzinda wina uliwonse, anthu anasankhidwa mowatchula mayina kuti azipereka magawo kwa munthu wamwamuna aliyense pakati pawo ndiponso kwa onse amene analembedwa mʼmbiri ya mibado ya Alevi.
20 Вот что сделал Езекия во всей Иудее, - и он делал доброе, и справедливое, и истинное пред лицем Господа Бога своего.
Izi ndi zimene Hezekiya anachita mu Yuda monse, kuchita zabwino, zolungama ndi zokhulupirika pamaso pa Yehova Mulungu wake.
21 И во всем, что он предпринимал на служение дому Божию и для соблюдения закона и заповедей, помышляя о Боге своем, он действовал от всего сердца своего и имел успех.
Pa chilichonse chimene anachita pa ntchito ya Nyumba ya Mulungu ndi pa kumvera malangizo ndi malamulo, iye anafunafuna Mulungu wake ndipo anagwira ntchito ndi mtima wake wonse. Ndipo zinthu zimamuyendera bwino.

< 2-я Паралипоменон 31 >