< 2-я Паралипоменон 17 >

1 И воцарился Иосафат, сын его, вместо него; и укрепился он против Израильтян.
Yehosafati mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake ndipo anadzilimbitsa pofuna kulimbana ndi Israeli.
2 И поставил он войско во все укрепленные города Иудеи и расставил охранное войско по земле Иудейской и по городам Ефремовым, которыми овладел Аса, отец его.
Iye anayika magulu a asilikali mʼmizinda yonse yotetezedwa ya Yuda, ndipo anamanga maboma mu Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Efereimu imene Asa abambo ake analanda.
3 И был Господь с Иосафатом, потому что он ходил первыми путями Давида, отца своего, и не взыскал Ваалов,
Yehova anali ndi Yehosafati chifukwa mʼzaka zoyambirira anatsatira makhalidwe a Davide abambo ake. Iye sanafunsire kwa Abaala.
4 но взыскал он Бога отца своего и поступал по заповедям Его, а не по деяниям Израильтян.
Koma anafunafuna Mulungu wa abambo ake ndipo anatsatira malamulo ake osati zochita za Israeli.
5 И утвердил Господь царство в руке его, и давали все Иудеи дары Иосафату, и было у него много богатства и славы.
Yehova anakhazikitsa kolimba ufumuwo mʼmanja mwake ndipo Ayuda onse anabweretsa mphatso kwa Yehosafati, kotero kuti anali ndi chuma ndi ulemu wambiri.
6 И возвысилось сердце его на путях Господних; притом и высоты отменил он и дубравы в Иудее.
Mtima wake anawupereka kutsatira Yehova, kuwonjezera apo, anachotsa malo onse achipembedzo ndi mafano a Asera mu Yuda.
7 И в третий год царствования своего он послал князей своих Бенхаила и Овадию, и Захарию и Нафанаила и Михея, чтоб учили по городам Иудиным народ,
Mʼchaka chachitatu cha ufumu wake, iye anatuma akuluakulu ake Beni-Haili, Obadiya, Zekariya, Netaneli ndi Mikaya kukaphunzitsa mʼmizinda ya Yuda.
8 и с ними левитов: Шемаию и Нефанию, и Зевадию и Азаила, и Шемирамофа и Ионафана, и Адонию и Товию и Тов-Адонию, и с ними Елишаму и Иорама, священников.
Pamodzi ndi iwo panali Alevi ena: Semaya, Netaniya, Zebadiya, Asaheli, Semiramoti, Yonatani, Adoniya, Tobiya ndi Tobu-Adoniya ndiponso ansembe Elisama ndi Yehoramu.
9 И они учили в Иудее, имея с собою книгу закона Господня; и обходили все города Иудеи и учили народ.
Iwo anaphunzitsa mu Yuda monse atatenga Buku la Malamulo a Yehova iwo anayenda mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndipo anaphunzitsa anthu.
10 И был страх Господень на всех царствах земель, которые вокруг Иудеи, и не воевали с Иосафатом.
Kuopsa kwa Yehova kunali pa maufumu onse a mayiko oyandikana ndi Yuda, kotero kuti sanachite nkhondo ndi Yehosafati.
11 А от Филистимлян приносили Иосафату дары и в дань серебро; также Аравитяне пригоняли к нему мелкий скот: овнов семь тысяч семьсот и козлов семь тысяч семьсот.
Afilisti ena anabweretsa kwa Yehosafati mphatso ndi siliva ngati msonkho, ndipo Aarabu anabweretsa ziweto: nkhosa zazimuna 7,700 ndi mbuzi 7,700.
12 И возвышался Иосафат все более и более и построил в Иудее крепости и города для запасов.
Mphamvu za Yehosafati zinkakulirakulira. Iye anamanga malo otetezedwa ndi mizinda yosungiramo chuma mu Yuda
13 Много было у него запасов в городах Иудейских, а в Иерусалиме людей военных, храбрых.
ndipo anali ndi katundu wambiri mʼmizinda ya Yuda. Iye anayikanso asilikali odziwa bwino nkhondo mu Yerusalemu.
14 И вот список их по поколениям их: у Иуды начальники тысяч: Адна начальник, и у него отличных воинов триста тысяч;
Chiwerengero chawo potsata mabanja awo chinali chotere: kuchokera ku Yuda, atsogoleri a magulu 1,000; mtsogoleri Adina, anali ndi anthu 300,000 odziwa nkhondo;
15 за ним Иоханан начальник, и у него двести восемьдесят тысяч;
otsatana naye, mtsogoleri Yehohanani, anali ndi anthu 280,000;
16 за ним Амасия, сын Зихри, посвятивший себя Господу, и у него двести тысяч воинов отличных.
otsatana naye, Amasiya mwana wa Zikiri amene anadzipereka yekha kutumikira Yehova, anali ndi anthu 200,000.
17 У Вениамина: отличный воин Елиада, и у него вооруженных луком и щитом двести тысяч;
Kuchokera ku Benjamini: Eliada, msilikali wolimba mtima, anali ndi anthu 200,000 amene anali ndi mauta ndi zishango;
18 за ним Иегозавад, и у него сто восемьдесят тысяч вооруженных воинов.
otsatana naye, Yehozabadi, anali ndi anthu 180,000 okonzekera nkhondo.
19 Вот служившие царю, сверх тех, которых расставил царь в укрепленных городах по всей Иудее.
Awa ndi anthu amene ankatumikira mfumu osawerengera amene anawayika mʼmizinda yotetezedwa mʼdziko lonse la Yuda.

< 2-я Паралипоменон 17 >