< 1-я Паралипоменон 27 >

1 Вот сыны Израилевы по числу их, главы семейств, тысяченачальники и стоначальники и управители, которые по отделениям служили царю во всех делах, приходя и отходя каждый месяц, во все месяцы года. В каждом отделении было их по двадцать четыре тысячи.
Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.
2 Над первым отделением, для первого месяца, начальствовал Иашовам, сын Завдиила; в его отделении было двадцать четыре тысячи;
Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
3 он был из сынов Фареса, главный над всеми военачальниками в первый месяц.
Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.
4 Над отделением второго месяца был Додай Ахохиянин; в отделении его был и князь Миклоф, и в его отделении было двадцать четыре тысячи.
Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
5 Третий главный военачальник, для третьего месяца, Ванея, сын Иодая, священника, и в его отделении было двадцать четыре тысячи:
Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000.
6 этот Ванея - один из тридцати храбрых и начальник над ними, и в его отделе находился Аммизавад, сын его.
Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.
7 Четвертый, для четвертого месяца, был Асаил, брат Иоава, и по нем Завадия, сын его, и в его отделении двадцать четыре тысячи.
Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
8 Пятый, для пятого месяца, князь Шамгуф Израхитянин, и в его отделении двадцать четыре тысячи.
Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
9 Шестой, для шестого месяца, Ира, сын Иккеша, Фекоянин, и в его отделении двадцать четыре тысячи.
Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
10 Седьмой, для седьмого месяца, Хелец Пелонитянин, из сынов Ефремовых, и в его отделении двадцать четыре тысячи.
Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
11 Восьмой, для восьмого месяца, Совохай Хушатянин, из племени Зары, и в его отделении двадцать четыре тысячи.
Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000
12 Девятый, для девятого месяца, Авиезер Анафофянин, из сыновей Вениаминовых, и в его отделении двадцать четыре тысячи.
Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
13 Десятый, для десятого месяца, Магарай Нетофафянин, из племени Зары, и в его отделении двадцать четыре тысячи.
Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
14 Одиннадцатый, для одиннадцатого месяца, Ванея Пирафонянин, из сынов Ефремовых, и в его отделении двадцать четыре тысячи.
Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
15 Двенадцатый, для двенадцатого месяца, Хелдай Нетофафянин, из потомков Гофониила, и в его отделении двадцать четыре тысячи.
Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.
16 А над коленами Израилевыми, - у Рувимлян главным начальником был Елиезер, сын Зихри; у Симеона - Сафатия, сын Маахи;
Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa: Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri; mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;
17 у Левия - Хашавия, сын Кемуила; у Аарона - Садок;
mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli, mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;
18 у Иуды - Елиав, из братьев Давида; у Иссахара - Омри, сын Михаила;
mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide; mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;
19 у Завулона - Ишмаия, сын Овадии; у Неффалима - Иеримоф, сын Азриила;
mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya; mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;
20 у сыновей Ефремовых - Осия, сын Азазии; у полуколена Манассиина - Иоиль, сын Федаии;
mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya; mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;
21 у полуколена Манассии в Галааде - Иддо, сын Захарии; у Вениамина - Иаасиил, сын Авенира;
mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya; mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;
22 у Дана - Азариил, сын Иерохама. Вот вожди колен Израилевых.
mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu. Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.
23 Давид не делал счисления тех, которые были от двадцати лет и ниже, потому что Господь сказал, что Он умножит Израиля, как звезды небесные.
Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga.
24 Иоав, сын Саруи, начал делать счисление, но не кончил. И был за это гнев Божий на Израиля, и не вошло то счисление в летопись царя Давида.
Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.
25 Над сокровищами царскими был Азмавеф, сын Адиилов, а над запасами в поле, в городах, и в селах и в башнях - Ионафан, сын Уззии;
Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu. Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.
26 над занимающимися полевыми работами, земледелием - Езрий, сын Хелува;
Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.
27 над виноградниками - Шимей из Рамы, а над запасами вина в виноградниках Завдий из Шефама;
Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa. Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.
28 над маслинами и смоковницами в долине - Баал-Ханан Гедеритянин, а над запасами деревянного масла - Иоас;
Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela. Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.
29 над крупным скотом, пасущимся в Шароне - Шитрай Шаронянин, а над скотом в долинах - Шафат, сын Адлая;
Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni. Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.
30 над верблюдами - Овил Исмаильтянин; над ослицами - Иехдия Меронифянин;
Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira. Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.
31 над мелким скотом - Иазиз Агаритянин. Все эти были начальниками над имением, которое было у царя Давида.
Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi. Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.
32 Ионафан, дядя Давидов, был советником, человек умный и писец; Иехиил, сын Хахмониев, был при сыновьях царя;
Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.
33 Ахитофел был советником царя; Хусий Архитянин - другом царя;
Ahitofele anali phungu wa mfumu. Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu.
34 после же Ахитофела Иодай, сын Ванеи, и Авиафар, а Иоав был военачальником у царя.
Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara. Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.

< 1-я Паралипоменон 27 >