< 1-я Паралипоменон 24 >

1 И вот распределения сыновей Аароновых: сыновья Аарона: Надав, Авиуд, Елеазар и Ифамар.
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 Надав и Авиуд умерли прежде отца своего, сыновей же не было у них, и потому священствовали Елеазар и Ифамар.
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 И распределил их Давид - Садока из сыновей Елеазара, и Ахимелеха из сыновей Ифамара, поочередно на службу их.
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 И нашлось, что между сынами Елеазара глав поколений более, нежели между сынами Ифамара. И он распределил их так: из сынов Елеазара шестнадцать глав семейств, а из сынов Ифамара восемь.
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 Распределял же их по жребиям, потому что главными во святилище и главными пред Богом были из сынов Елеазара и из сынов Ифамара,
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 и записывал их Шемаия, сын Нафанаила, писец из левитов, пред лицем царя и князей и пред священником Садоком и Ахимелехом, сыном Авиафара, и пред главами семейств священнических и левитских: брали при бросании жребия одно семейство из рода Елеазарова, потом брали из рода Ифамарова.
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 И вышел первый жребий Иегоиариву, второй Иедаии,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 третий Хариму, четвертый Сеориму,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 пятый Малхию, шестой Миямину,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 седьмой Гаккоцу, восьмой Авии,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 девятый Иешую, десятый Шехании,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 одиннадцатый Елиашиву, двенадцатый Иакиму,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 тринадцатый Хушаю, четырнадцатый Иешеваву,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 пятнадцатый Вилге, шестнадцатый Имеру,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 семьнадцатый Хезиру, восемнадцатый Гапицецу,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 девятнадцатый Петахии, двадцатый Иезекиилю,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 двадцать первый Иахину, двадцать второй Гамулу, у
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 двадцать третий Делаии, двадцать четвертый Маазии.
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 Вот порядок их при служении их, как им приходить в дом Господень, по уставу их чрез Аарона, отца их, как заповедал ему Господь Бог Израилев.
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 У прочих сыновей Левия - распределение: из сынов Амрама: Шуваил; из сынов Шуваила: Иедия;
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 от Рехавии: из сынов Рехавии Ишшия был первый;
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 от Ицгара: Шеломоф; из сыновей Шеломофа: Иахав;
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 из сыновей Хеврона: первый Иерия, второй Амария, третий Иахазиил, четвертый Иекамам.
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 Из сыновей Озиила: Миха; из сыновей Михи: Шамир.
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 Брат Михи Ишшия; из сыновей Ишшии: Захария.
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 Сыновья Мерари: Махли и Муши; из сыновей Иаазии: Бено.
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 Из сыновей Мерари у Иаазии: Бено и Шогам, и Заккур и Иври.
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 У Махлия - Елеазар; у него сыновей не было.
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 У Киса: из сыновей Киса: Иерахмиил;
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 сыновья Мушия: Махли, Едер и Иеримоф. Вот сыновья левитов по поколениям их.
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 Бросали и они жребий, наравне с братьями своими, сыновьями Аароновыми, пред лицем царя Давида и Садока и Ахимелеха, и глав семейств священнических и левитских: Глава семейства наравне с меньшим братом своим.
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 1-я Паралипоменон 24 >