< 1-я Паралипоменон 15 >

1 И построил он себе домы в городе Давидовом, и приготовил место для ковчега Божия, и устроил для него скинию.
Davide atadzimangira nyumba zina mu Mzinda wa Davide, iye anakonza malo a Bokosi la Mulungu ndipo analimangira tenti.
2 Тогда сказал Давид: никто не должен носить ковчега Божия, кроме левитов, потому что их избрал Господь на то, чтобы носить ковчег Божий и служить Ему во веки.
Pamenepo Davide anati, “Palibe wina ati anyamule Bokosi la Mulungu koma Alevi chifukwa Yehova anawasankha kuti azinyamula Bokosi la Yehova ndi kumatumikira pamaso pake nthawi zonse.”
3 И собрал Давид всех Израильтян в Иерусалим, чтобы внести ковчег Господень на место его, которое он для него приготовил.
Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse mu Yerusalemu kuti abweretse Bokosi la Yehova ku malo amene analikonzera.
4 И созвал Давид сыновей Аароновых и левитов:
Iye anayitanitsa pamodzi zidzukulu za Aaroni ndi Alevi:
5 из сыновей Каафовых, Уриила начальника и братьев его - сто двадцать человек;
kuchokera ku banja la Kohati, mtsogoleri Urieli ndi abale ake 120.
6 из сыновей Мерариных, Асаию начальника и братьев его - двести двадцать человек;
Kuchokera ku banja la Merari, mtsogoleri Asaya ndi abale ake 220;
7 из сыновей Гирсоновых, Иоиля начальника и братьев его - сто тридцать человек;
kuchokera ku banja la Geresomu, mtsogoleri Yoweli ndi abale ake 130;
8 из сыновей Елисафановых, Шемаию начальника и братьев его - двести;
kuchokera ku banja la Elizafani, mtsogoleri Semaya ndi abale ake 200;
9 из сыновей Хевроновых, Елиела начальника и братьев его - восемьдесят;
kuchokera ku banja la Hebroni, mtsogoleri Elieli ndi abale ake 80;
10 из сыновей Уззииловых, Аминадава начальника и братьев его - сто двенадцать.
kuchokera ku banja la Uzieli, mtsogoleri Aminadabu ndi abale ake 112.
11 И призвал Давид священников: Садока и Авиафара, и левитов: Уриила, Асаию, Иоиля, Шемаию, Елиела и Аминадава,
Kenaka Davide anayitanitsa ansembe Zadoki ndi Abiatara, ndi Alevi awa, Urieli, Asaya, Yoweli, Semaya, Elieli ndi Aminadabu.
12 и сказал им: вы, начальники родов левитских, освятитесь сами и братья ваши, и принесите ковчег Господа Бога Израилева на место, которое я приготовил для него;
Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu atsogoleri a mabanja a Alevi ndipo inu ndi abale anu Alevi mudziyeretse nokha ndi kubweretsa Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli ku malo amene ine ndalikonzera.
13 ибо как прежде не вы это делали, то Господь Бог наш поразил нас за то, что мы не взыскали Его, как должно.
Popeza kuti inu Alevi simunalinyamule poyamba paja, Yehova Mulungu wathu anatikantha. Sitinafunse momwe tikanachitira monga mmene Iyeyo anafotokozera.”
14 И освятились священники и левиты для того, чтобы нести ковчег Господа, Бога Израилева.
Kotero ansembe ndi Alevi anadziyeretsa ndi cholinga chakuti akatenge Bokosi la Yehova Mulungu wa Israeli.
15 И понесли сыновья левитов ковчег Божий, как заповедал Моисей по слову Господа, на плечах, на шестах.
Ndipo Alevi ananyamula Bokosi la Mulungu pa mapewa awo pa mitengo yake yonyamulira monga momwe Mose analamulira molingana ndi mawu a Yehova.
16 И приказал Давид начальникам левитов поставить братьев своих певцов с музыкальными орудиями, с псалтирями и цитрами и кимвалами, чтобы они громко возвещали глас радования.
Davide anawuza atsogoleri a Alevi kuti asankhe abale awo kuti akhale oyimba nyimbo zachisangalalo, zoyimba ndi zida: azeze, apangwe ndi ziwaya za malipenga.
17 И поставили левиты Емана, сына Иоилева, и из братьев его, Асафа, сына Верехиина, а из сыновей Мерариных, братьев их, Ефана, сына Кушаии;
Kotero Alevi anasankha Hemani mwana wa Yoweli; ndipo mwa abale ake anasankha Asafu mwana wa Berekiya; ndipo mwa ana a Merari, abale awo, anasankha Etani mwana wa Kusaya;
18 и с ними братьев их второстепенных: Захарию, Бена, Иаазиила, Шемирамофа, Иехиила, Унния, Елиава, Ванею, Маасея, Маттафию, Елифлеуя, Микнея и Овед-Едома и Иеиела, привратников.
ndipo pamodzi ndi iwowa abale awo otsatana nawo: Zekariya, Yaazieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Benaya, Maaseya, Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli, alonda a pa chipata.
19 Еман, Асаф и Ефан играли громко на медных кимвалах,
Anthu oyimba aja Hemani, Asafu ndi Etani ndiwo ankayimba ziwaya za malipenga zamkuwa;
20 а Захария, Азиил, Шемирамоф, Иехиил, Унний, Елиав, Маасей и Ванея - на псалтирях, тонким голосом.
Zekariya, Azieli, Semiramoti, Yehieli, Uni, Eliabu, Maaseya ndi Benaya ankayimba azeze a liwu lokwera;
21 Маттафия же, Елифлеуй, Микней, Овед-Едом, Иеиел и Азазия - на цитрах, чтобы делать начало.
ndipo Matitiya, Elifelehu, Mikineya, Obedi-Edomu, Yeiyeli ndi Azaziya ankayimba apangwe a liwu lotsika.
22 А Хенания, начальник левитов, был учитель пения, потому что был искусен в нем.
Kenaniya, mtsogoleri wa Alevi anali woyangʼanira mayimbidwe; uwu ndiye unali udindo wake pakuti anali waluso pa zimenezi.
23 Верехия и Елкана были придверниками у ковчега.
Berekiya ndi Elikana anali olondera pa khomo la bokosilo.
24 Шевания, Иосафат, Нафанаил, Амасай, Захария, Ванея и Елиезер, священники, трубили трубами пред ковчегом Божиим. Овед-Едом и Иехия были придверниками у ковчега.
Ansembe awa; Sebaniya, Yehosafati, Netaneli, Amasai, Zekariya, Benaya ndi Eliezara ndiwo ankayimba malipenga patsogolo pa Bokosi la Mulungu. Obedi-Edomu ndi Yehiya analinso alonda a pa khomo la bokosilo.
25 Так Давид и старейшины Израилевы и тысяченачальники пошли перенести ковчег завета Господня из дома Овед-Едомова с веселием.
Choncho Davide pamodzi ndi akuluakulu a Israeli ndiponso asilikali olamulira magulu a anthu 1,000, anapita kukatenga Bokosi la Chipangano la Yehova ku nyumba ya Obedi-Edomu akukondwera.
26 И когда Бог помог левитам, несшим ковчег завета Господня, тогда закололи в жертву семь тельцов и семь овнов.
Popeza Mulungu anathandiza Alevi amene ananyamula Bokosi la Chipangano la Yehova, anapereka nsembe ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndiponso nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.
27 Давид был одет в виссонную одежду, а также и все левиты, несшие ковчег, и певцы, и Хенания начальник музыкантов и певцов. На Давиде же был еще льняной ефод.
Ndipo Davide anali atavala mkanjo wa nsalu yofewa yosalala, monga anavalira Alevi onse amene ananyamula bokosi pamodzi anthu oyimba, ndiponso Kenaniya, amene anali woyangʼanira magulu oyimba. Davide anavalanso efodi ya nsalu yofewa yosalala.
28 Так весь Израиль вносил ковчег завета Господня с восклицанием, при звуке рога и труб и кимвалов, играя на псалтирях и цитрах.
Kotero Aisraeli onse anabweretsa Bokosi la Chipangano la Yehova ndi mfuwu, ndiponso akuyimba zitoliro zanyanga zankhosa zazimuna, malipenga ndi maseche ndiponso akuyimba azeze ndi apangwe.
29 Когда ковчег завета Господня входил в город Давидов, Мелхола, дочь Саулова, смотрела в окно и, увидев царя Давида, скачущего и веселящегося, уничижила его в сердце своем.
Bokosi la Chipangano la Yehova likulowa mu Mzinda wa Davide, Mikala mwana wamkazi wa Sauli ankaona ali pa zenera. Ndipo ataona Mfumu Davide ikuvina ndi kukondwera, iye ananyoza Davideyo mu mtima mwake.

< 1-я Паралипоменон 15 >