< Йов 8 >

1 Билдад дин Шуах а луат кувынтул ши а зис:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 „Пынэ кынд врей сэ ворбешть астфел ши пынэ кынд вор фи кувинтеле гурий тале ка ун вынт путерник?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Оаре ва рэстурна Думнезеу дрептул? Сау ва рэстурна Чел Атотпутерник дрептатя?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Дакэ фиий тэй ау пэкэтуит ымпотрива Луй, й-а дат пе мына пэкатулуй.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Дар ту, дакэ алерӂь ла Думнезеу, дакэ роӂь пе Чел Атотпутерник,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 дакэ ешть курат ши фэрэ приханэ, атунч, негрешит, Ел ва вегя асупра та ши ва да ынапой феричиря локуинцей тале невиновате.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Векя та пропэшире ва фи микэ фацэ де чя де май тырзиу.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Ынтрябэ пе чей дин нямуриле трекуте ши я аминте ла пэцания пэринцилор лор.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Кэч ной сунтем де ерь ши ну штим нимик, зилеле ноастре пе пэмынт ну сунт декыт о умбрэ.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Ей те вор ынвэца, ыць вор ворби ши вор скоате дин инима лор ачесте кувинте:
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 ‘Креште папура фэрэ балтэ? Креште трестия фэрэ умезялэ?’
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Фиинд ынкэ верде ши фэрэ сэ се тае, еа се усукэ май репеде декыт тоате ербуриле.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Аша се ынтымплэ тутурор челор че уйтэ пе Думнезеу, ши нэдеждя челуй нелеӂюит ва пери.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Ынкредеря луй есте здробитэ, ши сприжинул луй есте о пынзэ де пэянжен.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Се бизуеште пе каса луй, дар ну есте таре; се принде де еа, дар ну цине.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Кум дэ соареле, ынверзеште, ышь ынтинде рамуриле песте грэдина са,
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 ышь ымплетеште рэдэчиниле принтре петре, пэтрунде пынэ ын зидурь.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Дар, дакэ-л смулӂь дин локул ын каре стэ, локул ачеста се ляпэдэ де ел ши зиче: ‘Ну штиу сэ те фи куноскут вреодатэ!’
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Ятэ, аша сунт десфэтэриле пе каре и ле адук кэиле веций луй; апой дин ачелашь пэмынт рэсар алций дупэ ел.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Ну, Думнезеу ну ляпэдэ пе омул фэрэ приханэ ши ну окротеште пе чей рэй.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Ба ынкэ, Ел ыць умпле гура ку стригэте де букурие, ши бузеле ку кынтэрь де веселие.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Врэжмаший тэй вор фи акопериць де рушине, яр кортул челор рэй ва пери.”
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Йов 8 >