< Salmos 147 >

1 Louvai ao SENHOR, porque é bom cantar louvores ao nosso Deus; porque agradável e merecido [é] o louvor.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 O SENHOR edifica a Jerusalém; [e] ajunta os dispersos de Israel.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 Ele sara aos de coração partido, e os cura de suas dores.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 Ele conta o número das estrelas; chama todas elas pelos seus nomes.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 O nosso Senhor é grande e muito poderoso; seu entendimento é incomensurável.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 O SENHOR levanta aos mansos; [e] abate aos perversos até a terra.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Cantai ao SENHOR em agradecimento; cantai louvores ao nosso Deus com harpa.
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Ele que cobre o céu com nuvens, que prepara chuva para a terra, que faz os montes produzirem erva;
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Que dá ao gado seu pasto; e [também] aos filhos dos corvos, quando clamam.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 Ele não se agrada da força do cavalo, nem se contenta com as pernas do homem.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 O SENHOR se agrada dos que o temem, daqueles que esperam por sua bondade.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Louva, Jerusalém, ao SENHOR; celebra ao teu Deus, ó Sião.
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 Porque ele fortifica os ferrolhos de tuas portas; ele abençoa a teus filhos dentro de ti.
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 [Ele é] o que dá paz às tuas fronteiras; e te farta com o melhor trigo;
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 Que envia sua ordem à terra; sua palavra corre velozmente.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 Que dá a neve como a lã; espalha a geada como a cinza.
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 Que lança seu gelo [em] pedaços; quem pode subsistir ao seu frio?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 Ele manda sua palavra, e os faz derreter; faz soprar seu vento, [e] escorrem-se as águas.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 Ele declara suas palavras a Jacó; e seus estatutos e seus juízos a Israel.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 Ele não fez assim a nenhuma [outra] nação; [e] não conhecem os juízos [dele]. Louvai ao SENHOR.
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Salmos 147 >