< 8 >

1 Então Bildade, o suíta, respondeu, dizendo:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Até quando falarás tais coisas, e as palavras de tua boca serão como um vento impetuoso?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Por acaso Deus perverteria o direito, ou o Todo-Poderoso perverteria a justiça?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Se teus filhos pecaram contra ele, ele também os entregou ao castigo por sua transgressão.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Se tu buscares a Deus com empenho, e pedires misericórdia ao Todo-Poderoso;
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Se fores puro e correto, certamente logo ele se levantará em teu favor, e restaurará a morada de tua justiça.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 Ainda que teu princípio seja pequeno, o teu fim será muito grandioso.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Pois pergunta agora à geração passada, e considera o que seus pais descobriram.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 Pois nós somos de ontem e nada sabemos, pois nossos dias sobre a terra são como a sombra.
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Por acaso eles não te ensinarão, e te dirão, e falarão palavras de seu coração?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Pode o papiro crescer sem lodo? Ou pode o junco ficar maior sem água?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Estando ele ainda verde, sem ter sido cortado, ainda assim se seca antes de toda erva.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Assim são os caminhos de todos os que esquecem de Deus; e a esperança do corrupto perecerá;
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Sua esperança será frustrada, e sua confiança será como a teia de aranha.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Ele se apoiará em sua casa, mas ela não ficará firme; ele se apegará a ela, mas ela não ficará de pé.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Ele está bem regado diante do sol, e seus ramos brotam por cima de sua horta;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Suas raízes se entrelaçam junto à fonte, olhando para o pedregal.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Se lhe arrancarem de seu lugar, este o negará, [dizendo]: Nunca te vi.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Eis que este é o prazer de seu caminho; e do solo outros brotarão.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Eis que Deus não rejeita ao íntegro, nem segura pela mão aos malfeitores.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Ainda ele encherá tua boca de riso, e teus lábios de júbilo.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Os que te odeiam se vestirão de vergonha, e nunca mais haverá tenda de perversos.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< 8 >