< Micheasza 6 >

1 Słuchajcie tego, co mówi PAN: Wstań, spieraj się z górami i niech pagórki słuchają twego głosu.
Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
2 Słuchajcie, góry, sporu PANA, i najmocniejsze fundamenty ziemi, bo PAN [wiedzie] spór ze swoim ludem i rozprawia się z Jerozolimą.
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
3 Mój ludu, cóż ci uczyniłem? W czym ci się uprzykrzyłem? Zeznaj przeciwko mnie.
“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
4 Wyprowadziłem cię bowiem z ziemi Egiptu, odkupiłem cię z domu niewolników i posłałem przed tobą Mojżesza, Aarona i Miriam.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
5 Mój ludu! Wspomnij teraz, co zamierzał Balak, król Moabu, a co mu odpowiedział Balaam, syn Beora; [wspomnij też, co się działo] od Szittim aż do Gilgal, abyś poznał sprawiedliwość PANA.
Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
6 Z czym [mam] się stawić przed PANEM i pokłonić się Bogu najwyższemu? Czy [mam] stawić się przed nim z ofiarami całopalnymi i jednorocznymi cielcami?
Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
7 Czy PAN ma upodobanie w tysiącach baranów [i] w dziesiątkach tysięcy strumieni oliwy? Czy [mam] mu dać swego pierworodnego za mój występek, owoc mego łona za grzech mojej duszy?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
8 On ci oznajmił, człowieku, co jest dobre i czego PAN żąda od ciebie: jedynie [tego], byś czynił sprawiedliwie, kochał miłosierdzie i pokornie chodził z twoim Bogiem.
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
9 Głos PANA woła do miasta (ale roztropny [sam] ujrzy twoje imię): Słuchajcie rózgi i tego, kto ją ustanowił.
Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Czy jeszcze [są] w domu bezbożnego skarby niesprawiedliwe [i] miara niesprawiedliwa i obrzydliwa?
Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Czy mam usprawiedliwić oszukańczą wagę i worek fałszywych odważników?
Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 Jego bogacze są pełni zdzierstwa, jego mieszkańcy mówią kłamstwo i ich język w ich ustach [jest] kłamliwy.
Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 Dlatego też dotknę cię chorobą, uderzę cię i zniszczę z powodu twoich grzechów.
Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Będziesz jeść, ale się nie nasycisz; twoje poniżenie [będzie] w środku ciebie. Pochwycisz, ale nie ocalisz, a co ocalisz, wydam pod miecz.
Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Będziesz siał, ale nie będziesz żął; będziesz tłoczył oliwki, ale nie namaścisz się oliwą; [będziesz wyciskał] moszcz, ale nie napijesz się wina.
Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 Przestrzegacie bowiem ustaw Omriego i wszystkich czynów domu Achaba i postępujecie według ich rad. Dlatego cię wydam na spustoszenie i jego mieszkańców na pośmiewisko. Będziecie więc nosić hańbę mego ludu.
Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

< Micheasza 6 >