< Hioba 8 >

1 Wtedy Bildad z Szuach odpowiedział:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Jak długo będziesz mówił takie rzeczy? [Jak długo] słowa z twoich ust [będą jak] gwałtowny wiatr?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Czy Bóg wypacza sąd? Czy Wszechmocny wypacza sprawiedliwość?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Jeśli twoi synowie zgrzeszyli przeciwko niemu, a on ich odrzucił za ich nieprawość;
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Jeśli zwrócisz się pilnie do Boga i będziesz błagać Wszechmocnego;
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Jeśli jesteś czysty i prawy, wtedy na pewno obudzi się dla ciebie i poszczęści mieszkaniu twojej sprawiedliwości.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 A [choćby] twój początek był niewielki, jednak twój koniec bardzo się rozmnoży.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Bo zapytaj, proszę, dawnych pokoleń i rozważ doświadczenie ich ojców;
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (My bowiem jesteśmy wczorajsi i nic nie wiemy, ponieważ nasze dni na ziemi są [jak] cień).
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Czy oni nie pouczą cię i nie powiedzą ci, i czy z ich serc nie wypłyną słowa?
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Czy sitowie urośnie bez wilgoci? Czy trzcina urośnie bez wody?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Chociaż jeszcze jest świeża i nieskoszona, prędzej usycha niż inna trawa.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Takie [są] drogi wszystkich, którzy zapominają Boga, i [tak] zginie nadzieja obłudnika.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Jego nadzieja zostanie podcięta, a jego ufność [będzie] jak pajęczyna.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Oprze się o swój dom, ale się nie ostoi; uchwyci się go, ale nie przetrwa.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Zieleni się na słońcu i w ogrodzie jego świeża latorośl wyrasta.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Jego korzenie są splątane wśród kamieni i wyrastają spośród nich.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Ale gdy go wyrwą z jego miejsca, wtedy miejsce to wyprze się go, [mówiąc]: Nie widziałem cię.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Takie oto [jest] szczęście jego drogi, a z ziemi wyrosną inni.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Oto Bóg nie odrzuci [człowieka] prawego, ale złoczyńcom nie poda ręki;
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Aż się napełnią twoje usta uśmiechem, a twoje wargi radością.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Gdyż ci, którzy cię nienawidzą, okryją się hańbą, a namiotu niegodziwych [już] nie będzie.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Hioba 8 >