< Izajasza 36 >

1 W czternastym roku królowania Ezechiasza Sennacheryb, król Asyrii, wyruszył przeciwko wszystkim warownym miastom Judy i zdobył je.
Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
2 I król Asyrii posłał Rabszaka z Lakisz do Jerozolimy, do króla Ezechiasza, z wielkim wojskiem. Ten stanął przy kanale górnej sadzawki przy drodze pola folusznika.
Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
3 Wtedy wyszli do niego Eliakim, syn Chilkiasza, przełożony domu, i Szebna, pisarz, oraz Joach, syn Asafa, kronikarz.
Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
4 Wtedy Rabszak powiedział do nich: Proszę, powiedzcie Ezechiaszowi: Tak mówi wielki król, król Asyrii: Co to za ufność, na której polegasz?
Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
5 [Mówisz] – ale to słowa daremne – mam dość dużo rad i siły do wojny. Teraz więc w kim pokładasz ufność, że zbuntowałeś się przeciwko mnie?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
6 Oto opierasz się na tej nadłamanej lasce trzcinowej – na Egipcie – która, gdy ktoś się oprze na niej, wbija mu się w dłoń i przebija ją. Taki jest faraon, król Egiptu, dla wszystkich, którzy mu ufają.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
7 A jeśli mi powiesz: Ufamy PANU, naszemu Bogu, czy on nie jest tym, którego wyżyny i ołtarze zniósł Ezechiasz i nakazał Judzie i Jerozolimie: Przed tym ołtarzem będziecie oddawać pokłon?
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
8 Dlatego teraz proszę, daj zastaw memu panu, królowi Asyrii, a ja dam ci dwa tysiące koni, jeśli zdołasz posadzić na nich jeźdźców.
“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
9 Jakże więc stawisz opór jednemu dowódcy z najmniejszych sług mego pana, a pokładasz nadzieję w Egipcie, że [otrzymasz] rydwany i jeźdźców?
Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
10 Poza tym czy bez woli PANA wyruszyłem przeciw tej ziemi, aby ją zniszczyć? PAN powiedział do mnie: Wyrusz przeciwko tej ziemi i spustosz ją.
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
11 Wtedy Eliakim, Szebna i Joach powiedzieli do Rabszaka: Proszę, mów do swoich sług po syryjsku, bo rozumiemy, a nie mów do nas po hebrajsku wobec ludu, który jest na murze.
Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
12 Lecz Rabszak odpowiedział: Czy do twego pana i do ciebie posłał mnie mój pan, abym mówił te słowa? Czyż nie do tych mężczyzn siedzących na murze, aby jedli swój kał i pili swój mocz razem z wami?
Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
13 Stał więc Rabszak i zawołał donośnym głosem po hebrajsku tymi słowami: Słuchajcie słów wielkiego króla, króla Asyrii.
Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
14 Tak mówi król: Niech was nie zwodzi Ezechiasz, bo nie będzie mógł was wybawić.
Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
15 A nie dajcie się przekonać Ezechiaszowi, by zaufać PANU, gdy mówi: Na pewno PAN nas wybawi i to miasto nie będzie wydane w ręce króla Asyrii.
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
16 Nie słuchajcie Ezechiasza. Tak bowiem powiedział król Asyrii: Zawrzyjcie ze mną przymierze i wyjdźcie do mnie, a każdy będzie jeść ze swojej winorośli i ze swego drzewa figowego i każdy będzie pić wodę ze swojej studni;
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
17 Aż przyjdę i zabiorę was do ziemi podobnej do waszej ziemi, do ziemi zboża i wina, do ziemi chleba i winnic.
mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
18 Niech Ezechiasz nie zwodzi was, mówiąc: PAN nas wybawi. Czy bogowie [innych] narodów mogli wybawić swoją ziemię z ręki króla Asyrii?
“Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
19 Gdzie są bogowie Chamatu i Arpadu? Gdzie są bogowie Sefarwaim? Czy wybawili Samarię z mojej ręki?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
20 Którzy spośród wszystkich bogów tych ziem wybawili swoją ziemię z mojej ręki, żeby PAN miał wybawić Jerozolimę z mojej ręki?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
21 Lecz lud milczał i nie odpowiedział mu ani słowa, bo taki był rozkaz króla: Nie odpowiadajcie mu.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
22 Wtedy przełożony domu Eliakim, syn Chilkiasza, pisarz Szebna i kronikarz Joach, syn Asafa, przyszli do Ezechiasza z rozdartymi szatami i oznajmili mu słowa Rabszaka.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.

< Izajasza 36 >