< Kaznodziei 9 >

1 Zaprawdę, wszystko to rozważałem w swoim sercu po to, aby to wszystko wyjaśnić – że sprawiedliwi i mądrzy oraz ich dzieła [są] w rękach Boga. Człowiek nie zna ani miłości, ani nienawiści ze wszystkich rzeczy, które są przed nim.
Ndinalingalira zonse ndanenazi ndipo ndinapeza kuti anthu olungama ndi anthu anzeru ali mʼmanja mwa Mulungu pamodzi ndi zimene amachita, koma palibe amene amadziwa zimene zikumudikira mʼtsogolo mwake, kaya chikondi kapena chidani.
2 Wszystkich [spotyka] to samo: ten sam los spotyka sprawiedliwego i niegodziwego, dobrego i czystego, i nieczystego, składającego ofiary i tego, który nie składa ofiar, zarówno dobrego, jak i grzesznika, przysięgającego i tego, kto boi się przysięgi.
Onsewa mathero awo ndi amodzi, anthu olungama ndi anthu oyipa, abwino ndi oyipa, oyera ndi odetsedwa, amene amapereka nsembe ndi amene sapereka nsembe. Zomwe zimachitikira munthu wabwino, zimachitikiranso munthu wochimwa, zomwe zimachitikira amene amalumbira, zimachitikiranso amene amaopa kulumbira.
3 Jest takie zło we wszystkim, co się dzieje pod słońcem: jeden los spotyka wszystkich. A przy tym serce synów ludzkich jest pełne zła, a głupota [znajduje się] w ich sercach, póki żyją, a potem [idą] do zmarłych.
Choyipa chimene chili mʼzonse zochitika pansi ndi ichi: Mathero a zonse ndi amodzi. Ndithu, mitima ya anthu ndi yodzaza ndi zoyipa, ndipo mʼmitima mwawo muli zamisala pamene ali ndi moyo, potsiriza pake iwo amakakhala pamodzi ndi anthu akufa.
4 Ktokolwiek bowiem jest złączony ze wszystkimi żyjącymi, ma nadzieję, gdyż lepszy jest żywy pies niż zdechły lew.
Aliyense amene ali ndi moyo amakhala ndi chiyembekezo, pajatu galu wamoyo aposa mkango wakufa!
5 Żyjący bowiem wiedzą, że umrą, ale umarli o niczym nie wiedzą i nie mają już żadnej zapłaty, gdyż pamięć o nich uległa zapomnieniu.
Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa, koma akufa sadziwa kanthu; alibe mphotho ina yowonjezera, ndipo palibe amene amawakumbukira.
6 Tak samo ich miłość, nienawiść i zazdrość już zginęły. I już nigdy więcej nie będą mieć działu we wszystkim, co się dzieje pod słońcem.
Chikondi chawo, chidani chawo ndiponso nsanje yawo, zonse zinatha kalekale; sadzakhalanso ndi gawo pa zonse zochitika pansi pano.
7 Idź więc, jedz z radością swój chleb i pij z wesołym sercem swe wino, gdyż Bóg już przyjął twoje dzieła.
Pita, kadye chakudya chako mokondwera ndi kumwa vinyo wako ndi mtima wosangalala, pakuti tsopano Mulungu akukondwera ndi zochita zako.
8 Niech twoje szaty będą zawsze białe i niech nie zabraknie olejku na twoją głowę.
Uzivala zovala zoyera nthawi zonse, uzidzola mafuta mʼmutu mwako nthawi zonse.
9 Ciesz się życiem z żoną, którą ukochałeś po wszystkie dni swego marnego życia, jakie dał ci [Bóg] pod słońcem, po wszystkie dni swojej marności. To jest bowiem twój dział w życiu i w trudzie, który podejmujesz pod słońcem.
Uzikondwerera moyo pamodzi ndi mkazi wako amene umamukonda, masiku onse a moyo uno wopanda phindu, amene Mulungu wakupatsa pansi pano. Pakuti mkaziyo ndiye gawo la moyo wako pa ntchito yako yolemetsa pansi pano.
10 Wszystko, cokolwiek twoja ręka postanowi czynić, czyń z całej swojej siły; [nie ma] bowiem żadnej pracy ani zamysłu, ani wiedzy, ani mądrości w grobie, do którego zmierzasz. (Sheol h7585)
Ntchito iliyonse imene ukuyigwira, uyigwire ndi mphamvu zako zonse, pakuti ku manda kumene ukupita kulibe kugwira ntchito, kulibe malingaliro, chidziwitso ndiponso nzeru. (Sheol h7585)
11 Potem obróciłem się i widziałem pod słońcem, że bieg nie [należy] do szybkich ani wojna do dzielnych, ani żywność do mądrych, ani bogactwo do roztropnych, ani łaska do zdolnych, lecz czas i przypadek spotyka wszystkich.
Ine ndinaonanso chinthu china pansi pano: opambana pa kuthamanga si aliwiro, kapena opambana pa nkhondo si amphamvu, ndiponso okhala ndi chakudya si anzeru, kapena okhala ndi chuma si odziwa zambiri, kapena okomeredwa mtima si ophunzira; koma mwayi umangowagwera onsewa pa nthawi yake.
12 Człowiek bowiem nie zna swojego czasu, ale jak ryby, które się łowi szkodliwą siecią, i jak ptaki chwytane w sidła, tak synowie ludzcy są uwikłani w złej chwili, gdy ta nagle na nich spadnie.
Kungoti palibe munthu amene amadziwa kuti nthawi yake idzafika liti: monga momwe nsomba zimagwidwira mu ukonde, kapena mmene mbalame zimakodwera mu msampha, chimodzimodzinso anthu amakodwa mu msampha pa nthawi yoyipa, pamene tsoka limawagwera mosayembekezera.
13 Widziałem również tę mądrość pod słońcem, która wydała mi się wielka:
Ine ndinaonanso pansi pano chitsanzo ichi cha nzeru chimene chinandikhudza kwambiri:
14 Było małe miasto, a w nim niewielu ludzi. I wyruszył przeciw niemu potężny król, obległ je i zbudował przeciwko niemu wielkie wały.
Panali mzinda waungʼono umene unali ndi anthu owerengeka. Ndipo mfumu yamphamvu inabwera kudzawuthira nkhondo, inawuzungulira ndi kumanga mitumbira yankhondo.
15 I znalazł się w nim człowiek ubogi i mądry, który wybawił to miasto przez swoją mądrość. Nikt jednak nie pamiętał tego ubogiego człowieka.
Tsono mu mzindamo munali munthu wosauka koma wanzeru, ndipo anapulumutsa mzindawo ndi nzeru zakezo. Koma palibe amene anakumbukira munthu wosaukayo.
16 I powiedziałem: Lepsza jest mądrość niż siła. Lecz mądrość ubogiego bywa wzgardzona i jego słów nikt nie słucha.
Choncho ine ndinati, “Nzeru ndi yopambana mphamvu.” Koma nzeru ya munthu wosauka imanyozedwa, ndipo palibe amene amalabadirako za mawu ake.
17 Spokojnych słów ludzi mądrych należy słuchać bardziej niż krzyku tego, który panuje wśród głupców.
Mawu oyankhula mofatsa a munthu wanzeru, anthu amawasamalira kwambiri kupambana kufuwula kwa mfumu ya zitsiru.
18 Lepsza jest mądrość niż oręż wojenny, ale jeden grzesznik niszczy wiele dobrego.
Nzeru ndi yabwino kupambana zida zankhondo, koma wochimwa mmodzi amawononga zinthu zambiri zabwino.

< Kaznodziei 9 >