< I Koryntian 13 >

1 Choćbym mówił językami ludzi i aniołów, a miłości bym nie miał, stałbym się [jak] miedź brzęcząca albo cymbał brzmiący.
Ngakhale nditamayankhula mʼmalilime a anthu ndi a angelo, koma ngati ndilibe chikondi, ndili ngati chinganga chaphokoso kapena ngati chitsulo chosokosera.
2 I choćbym miał [dar] prorokowania, i znał wszystkie tajemnice, i [posiadał] wszelką wiedzę, i choćbym miał pełnię wiary, tak, żebym góry przenosił, a miłości bym nie miał, byłbym niczym.
Ngati ndili ndi mphatso ya uneneri, nʼkumazindikira zinsinsi ndi kudziwa zonse, ndipo ngati ndili ndi chikhulupiriro chosuntha mapiri, koma wopanda chikondi, ine sindili kanthu.
3 I choćbym rozdał na żywność dla [ubogich] cały swój majątek, i choćbym wydał swoje ciało na spalenie, a miłości bym nie miał, nic nie zyskam.
Ngati ndipereka zanga zonse kwa osauka ndi kupereka thupi langa kuti alitenthe, koma ngati ndilibe chikondi, ine sindipindula kanthu.
4 Miłość jest cierpliwa, jest życzliwa. Miłość nie zazdrości, nie przechwala się, nie unosi się pychą;
Chikondi nʼcholeza mtima, chikondi nʼchokoma mtima, chilibe nsanje, sichidzikuza, sichidzitamandira.
5 Nie postępuje nieprzyzwoicie, nie szuka swego, nie jest porywcza, nie myśli [nic] złego;
Chikondi chilibe mwano, sichodzikonda, sichipsa mtima msanga, sichisunga mangawa.
6 Nie raduje się z niesprawiedliwości, ale raduje się z prawdy;
Chikondi sichikondwera ndi zoyipa koma chimakondwera ndi choonadi.
7 Wszystko znosi, wszystkiemu wierzy, wszystkiego się spodziewa, wszystko przetrzyma.
Chimatchinjiriza nthawi zonse, chimakhulupirika nthawi zonse, chimakhala ndi chiyembekezo nthawi zonse, chimapirira nthawi zonse.
8 Miłość nigdy nie ustaje. Bo choć są proroctwa, przeminą; choć języki, ustaną; choć wiedza, obróci się wniwecz.
Chikondi ndi chosatha. Koma mphatso ya uneneri idzatha, pamene pali kuyankhula malilime adzatha, pamene pali chidziwitso chidzatha.
9 Po części bowiem poznajemy i po części prorokujemy.
Pakuti timadziwa zinthu pangʼono chabe ndipo timanenera pangʼono chabe.
10 Ale gdy przyjdzie to, co doskonałe, wtedy przeminie to, co jest cząstkowe.
Koma changwiro chikadzaoneka ndipo chopereweracho chidzatha.
11 Dopóki byłem dzieckiem, mówiłem jak dziecko, rozumiałem jak dziecko, myślałem jak dziecko. Lecz gdy stałem się mężczyzną, zaniechałem tego, co dziecięce.
Pamene ndinali mwana ndinkayankhula ngati mwana, ndinkaganiza ngati mwana, ndinkalingalira ngati mwana. Koma nditakula, zonse zachibwana ndinazisiya.
12 Teraz bowiem widzimy w zwierciadle, niewyraźnie, ale wówczas twarzą w twarz. Teraz poznaję cząstkowo, ale wtedy poznam tak, jak jestem poznany.
Pakuti tsopano tiona zinthu mosaoneka bwino ngati mʼgalasi loonera; kenaka tidzaziona maso ndi maso. Tsopano ndidziwa mosakwanira koma kenaka ndidzadziwa mokwanira, monga mmene Mulungu akundidziwira ine.
13 A teraz trwają wiara, nadzieja, miłość, te trzy. Z nich zaś największa jest miłość.
Ndipo tsopano zatsala zinthu zitatu: chikhulupiriro, chiyembekezo ndi chikondi. Koma chachikulu pa zonsezi ndi chikondi.

< I Koryntian 13 >