< Psalmów 90 >

1 Modlitwa Mojżesza, męża Bożego. Panie! tyś bywał ucieczką naszą od narodu do narodu.
Pemphero la Mose munthu wa Mulungu. Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo pa mibado yonse.
2 Pierwej niżli góry stanęły i niżliś wykształtował ziemię, i okrąg świata, oto zaraz od wieku aż na wieki tyś jest Bogiem.
Mapiri asanabadwe, musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse, kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.
3 Ty znowu człowieka w proch obracasz, a mówisz: Nawróćcie się synowie ludzcy.
Inu mumabwezera anthu ku fumbi, mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
4 Albowiem tysiąc lat przed oczyma twemi są jako dzień wczorajszy, który przeminął, i jako straż nocna.
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu zili ngati tsiku limene lapita kapena ngati kamphindi ka usiku.
5 Powodzią porywasz ich; są jako sen, i jako trawa, która z poranku rośnie.
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa, iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
6 Z poranku kwitnie i rośnie; ale w wieczór bywa pokoszona, i usycha.
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano, pofika madzulo wauma ndi kufota.
7 Albowiem od gniewu twego giniemy, a popędliwością twoją jesteśmy przestraszeni.
Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu; ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
8 Położyłeś nieprawości nasze przed sobą, tajne występki nasze przed jasnością oblicza twego.
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu, machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
9 Skąd wszystkie dni nasze nagle przemijają dla gniewu twego; jako słowa niszczeją lata nasze.
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu; timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
10 Dni wieku naszego jest lat siedmdziesiąt, a jeźli kto duższy, lat ośmdziesiąt, a to, co najlepszego w nich, tylko kłopot i nędza, a gdy to pominie, tedy prędko odlatujemy.
Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70, kapena 80 ngati tili ndi mphamvu; komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa, zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.
11 Ale któż zna srogość gniewu twego? albo kto bojąc się ciebie zna zapalczywość twoję?
Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu? Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
12 Nauczże nas obliczać dni naszych, abyśmy przywiedli serce do mądrości.
Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola, kuti tikhale ndi mtima wanzeru.
13 Nawróćże się, Panie! dokądże odwłaczasz? zlitujże się nad sługami twymi.
Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti? Achitireni chifundo atumiki anu.
14 Nasyćże nas z poranku miłosierdziem twojem; tak, abyśmy wesoło śpiewać i radować się mogli po wszystkie dni nasze.
Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha, kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 Rozweselże nas według dni, którycheś nas utrapił, według lat, którycheśmy doznali złego.
Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa, kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Niech będzie znaczna przy sługach twoich sprawa twoja, a chwała twoja przy synach ich.
Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu, kukongola kwanu kwa ana awo.
17 Niech będzie przyjemność Pana, Boga naszego, przy nas, a sprawę rąk naszych utwierdź między nami, sprawę rąk naszych utwierdź, Panie!
Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife; tikhazikitsireni ntchito ya manja athu; inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

< Psalmów 90 >