< Psalmów 44 >

1 Przedniejszemu śpiewakowi z synów Korego psalm nauczający. Boże! uszami naszemi słyszeliśmy; ojcowie nasi powiadali nam o sprawach, któreś czynił za dni ich, za dni starodawnych.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
2 Tyś ręką swą wypędził pogan, a onycheś wszczepił; wytraciłeś narody, a onycheś rozkrzewił.
Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
3 Bo nie przez miecz swój posiedli ziemię, i ramię ich nie wybawiło ich, ale prawica twoja i ramię twoje, a światłość oblicza twego, przeto, żeś ich upodobał sobie.
Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
4 Tyś sam król mój, o Boże! sprawże wielkie wybawienie Jakóbowi.
Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
5 Przez cię nieprzyjaciół naszych porażaliśmy; w imieniu twojem deptaliśmy powstawających przeciwko nam.
Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
6 Bom w łuku moim nie ufał, ani miecz mój obronił mię;
Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
7 Aleś nas ty wybawiał od nieprzyjaciół naszych, a nienawidzących nas zawstydzałeś.
koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
8 Przetoż chlubimy się w tobie, Boże! na każdy dzień, a imię twoje na wieki wysławiamy. (Sela)
Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
9 Ale teraz odrzuciłeś i zawstydziłeś nas, a nie wychodzisz z wojskami naszemi.
Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
10 Sprawiłeś, żeśmy tył podali nieprzyjacielowi, a ci, którzy nas mają w nienawiści, rozchwycili między się dobra nasze.
Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
11 Podałeś nas jako owce na żer, a między pogan rozproszyłeś nas.
Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
12 Sprzedałeś lud twój za nic, a nie podniosłeś ceny ich.
Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
13 Podałeś nas na wzgardę sąsiadom naszym, na szyderstwo i na pośmiech tym, którzy są około nas.
Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
14 Wystawiłeś nas na przypowieść między poganami, tak, że nad nami narody głową kiwają.
Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
15 Na każdy dzień wstyd mój jest przedemną, a hańba twarzy mojej okrywa mię.
Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
16 Dla głosu tego, który mię sromoci i potwarza, dla nieprzyjaciela, i tego, który się mści.
chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
17 To wszystko przyszło na nas; a wżdyśmy cię nie zapomnieli, aniśmy wzruszyli przymierza twego.
Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
18 Nie cofnęło się nazad serce nasze, ani się uchyliły kroki nasze od ścieżki twojej,
Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
19 Chociażeś nas był potarł, wrzuciwszy nas na miejsce smoków, i okryłeś nas cieniem śmierci.
Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
20 Byśmyć byli zapomnieli imienia Boga naszego, a podnieśli ręce nasze do Boga cudzego,
Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
21 Iazliby się był Bóg o tem nie pytał? gdyż on wie skrytości serca.
kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
22 Aleć nas dla ciebie zabijają na każdy dzień; poczytają nas jako owce na rzeź zgotowane.
Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
23 Ocuć się; przeczże śpisz, Panie! Przebudź się, nie odrzucaj nas na wieki.
Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
24 Przeczże oblicze twoje ukrywasz, a zapominasz utrapienia naszego i ucisku naszego?
Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
25 Albowiem potłoczona jest aż do prochu dusza nasza, a przylgnął do ziemi żywot nasz.
Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
26 Powstańże na ratunek nasz, a odkup nas dla miłosierdzia twego.
Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.

< Psalmów 44 >