< Psalmów 42 >

1 Przedniejszemu śpiewakowi z synów Korego pieśń ćwicząca. Jako jeleń krzyczy do strumieni wód, tak dusza moja woła do ciebie, o Boże!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Monga mbawala ipuma wefuwefu kufunafuna mitsinje yamadzi, kotero moyo wanga upuma wefuwefu kufunafuna Inu Mulungu.
2 Pragnie dusza moja do Boga, do Boga żywego, mówiąc: Kiedyż przyjdę, a okażę się przed obliczem Bożem?
Moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Mulungu, lofuna Mulungu wamoyo. Kodi ndipite liti kukakumana ndi Mulungu?
3 Łzy moje są mi miasto chleba we dnie i w nocy, gdy mi mówią co dzień: Kędyż jest Bóg twój?
Misozi yanga yakhala chakudya changa usana ndi usiku, pamene anthu akunena kwa ine tsiku lonse kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
4 Na to wspominając wylewam sam sobie duszę moję, żem bywał w poczcie innych, i chadzałem z nimi do domu Bożego, z wesołym głosem, i z chwałą, w mnóstwie weselących się.
Zinthu izi ndimazikumbukira pamene ndikukhuthula moyo wanga: momwe ndinkapitira ndi gulu lalikulu, kutsogolera mayendedwe a ku Nyumba ya Mulungu ndi mfuwu yachimwemwe ndi mayamiko pakati pa anthu a pa chikondwerero.
5 Przeczże się smucisz, duszo moja! a przecz sobą trwożysz we mnie? Czekaj na Boga; albowiem go jeszcze będę wysławiał za wielkie wybawienie twarzy jego.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni, iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Yembekezera Mulungu, pakuti ndidzamulambirabe, Mpulumutsi wanga ndi
6 Boże mój! dusza moja tęskni sobie we mnie; przetoż na cię wspominam w ziemi Jordańskiej i Hermońskiej, na górze Mizar.
Mulungu wanga. Moyo wanga uli ndi chisoni mʼkati mwanga kotero ndidzakumbukira Inu kuchokera ku dziko la Yorodani, ku mitunda ya Herimoni kuchokera ku phiri la Mizara.
7 Przepaść przepaści przyzywa, na szum upustów twoich: wszystkie powodzi twoje i nawałności twoje na mię się zwaliły.
Madzi akuya akuyitana madzi akuya mu mkokomo wa mathithi anu; mafunde anu onse obwera mwamphamvu andimiza.
8 Wszakże we dnie udzieli mi Pan miłosierdzia swego, a w nocy piosnka jego będzie ze mną, i modlitwa do Boga żywota mego.
Koma usana Yehova amalamulira chikondi chake, nthawi ya usiku nyimbo yake ili nane; pemphero kwa Mulungu wa moyo wanga.
9 Rzekę Bogu, skale mojej: Przeczżeś mię zapomniał? I czemu smutno chodzę dla uciśnienia od nieprzyjaciela?
Ine ndikuti kwa Mulungu Thanthwe langa, “Nʼchifukwa chiyani mwandiyiwala? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?”
10 Jest jako rana w kościach moich, gdy mi urągają nieprzyjaciele moi, mówiąc do mnie na każdy dzień: Kędy jest Bóg twój?
Mafupa anga ali ndi ululu wakufa nawo pamene adani anga akundinyoza, tsiku lonse akunena kuti, “Mulungu wako ali kuti?”
11 Przeczże się smucisz, duszo moja? a przecz sobą trwożysz we mnie? Czekaj na Boga; albowiem go jeszcze będę wysławiał, gdyż on jest wielkiem zbawieniem twarzy mojej, i Bogiem moim.
Bwanji ukumva chisoni, iwe mtima wanga? Chifukwa chiyani ukuvutika chonchi mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandanso, Iye amene ali thandizo langa ndi Mulungu wanga.

< Psalmów 42 >