< Liczb 15 >

1 I rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Powiedz synom Izraelskim, a mów do nich: Gdy przyjdziecie do ziemi mieszkania waszego, którą Ja wam dam,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo,
3 A będziecie chcieli czynić ofiarę ognistą Panu na całopalenie, albo ofiarę, bądź poślubioną bądź dobrowolną, albo też na uroczyste święta wasze, czyniąc wdzięczną wonność Panu z wołów albo z owiec:
ndipo mukamadzapereka kwa Yehova, nsembe yotentha pa moto ya ngʼombe kapena nkhosa monga fungo lokoma kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena nsembe zina, nsembe yapadera chifukwa cha lumbiro kapena nsembe yoperekedwa mwaufulu kapenanso yoperekedwa pa chikondwerero,
4 Tedy, ktobykolwiek ofiarował ofiarę swoję Panu, niechże ofiaruje ofiarę śniedną, pszennej mąki dziesiątą część, zagniecionej z oliwą, której będzie czwarta część hynu.
munthu amene akubweretsa zopereka zake, azikapereka kwa Yehova chopereka chachakudya cholemera kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta wokwana lita imodzi.
5 Przytem wina na ofiarę mokrą czwartą część hynu ofiarować będziesz przy całopaleniu, albo przy ofierze innej do każdego baranka.
Pamodzi ndi mwana wankhosa aliyense wa nsembe yopsereza kapena nsembe ina, muzikakonzanso lita imodzi la vinyo ngati chopereka cha chakumwa.’”
6 Przy baranie też ofiarować będziesz ofiarę śniedną, mąki pszennej dwie dziesiąte części, zaczynionej z oliwą z trzecią częścią hynu.
“Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, muzikakonzanso chopereka cha chakudya cholemera makilogalamu awiri a ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta okwanira lita imodzi ndi theka,
7 Wina także na ofiarę mokrą trzecią część hynu ofiarować będziesz na wdzięczną wonność Panu.
ndi vinyo wokwanira lita imodzi ndi theka ngati chopereka cha chakumwa. Muzikapereka monga nsembe yopereka fungo lokoma kwa Yehova.
8 Jeźli zaś cielca ofiarować będziesz na ofiarę całopalenia, albo na ofiarę wypełnienia ślubu, albo na ofiarę spokojną Panu,
“‘Pamene mukukonza mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse: ya lumbiro lapadera kapena nsembe yachiyanjano kwa Yehova,
9 Tedy będziesz ofiarował społem z cielcem ofiarę śniedną, pszennej mąki trzy dziesiąte części, zagniecionej z oliwą z połową hynu.
pamodzi ndi mwana wangʼombe wamwamunayo muzibweretsa nsembe yachakudya yolemera makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta okwana malita awiri.
10 Wina także będziesz ofiarował na ofiarę mokrą połowę hynu, na ofiarę ognistą ku wdzięcznej wonności Panu.
Komanso muzibweretsa vinyo wokwanira malita awiri monga chopereka chachakumwa. Imeneyi idzakhala chopereka chotentha pa moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
11 Także uczynisz przy każdym wole, i przy każdym baranie i baranku, bądź z owiec bądź z kóz.
Ngʼombe yayimuna iliyonse kapena nkhosa yayimuna iliyonse, mwana wankhosa aliyense kapena mbuzi yayingʼono, zizikonzedwa motere.
12 Według liczby, którą ofiarować będziecie, tak uczynicie przy każdym z nich według liczby ich.
Ngakhale zingachuluke chotani, chitani izi kwa iliyonse ya nyamazo.
13 Każdy w domu zrodzony tak też będzie czynił, gdy będzie oddawał ofiarę ognistą na wdzięczną wonność Panu.
“‘Mbadwa iliyonse ya mu Israeli izichita zimenezi pamene ibweretsa nsembe yotentha pa moto kuti ikhale fungo lokoma kwa Yehova.
14 A gdyby, gościem będąc między wami przychodzień, albo mieszkający między wami w narodziech waszych, ofiarował ognistą ofiarę ku wdzięcznej wonności Panu, jako wy czynicie, tak i on uczyni.
Ku mibado yanu yonse ya mʼtsogolo, pamene mlendo kapena wina aliyense wokhala pakati panu apereka chopereka chotentha pa moto kuti chikhale fungo lokoma kwa Yehova, azichita mofanana ndi momwe inu mumachitira.
15 O ludu mój! Ustawa jedna niechaj będzie tak wam, jako i przychodniowi, mieszkającemu z wami; ustawa to jest wieczna w narodziech waszych; jako wy, tak przychodzień będzie przed Panem.
Gulu lonse likhale ndi malamulo ofanana a inu kapena mlendo wokhala pakati panu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya kwa mibado imene ikubwera. Inuyo ndi mlendo mudzakhala wofanana pamaso pa Yehova.
16 Prawo jedno, i jeden sąd będzie wam i przychodniowi mieszkającemu z wami.
Mudzakhale ndi malamulo ndi miyambo yofanana, inuyo ndi mlendo wokhala pakati panu.’”
17 I rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anawuza Mose kuti,
18 Powiedz synom Izraelskim, a rzecz do nich: Gdy wnijdziecie do ziemi, do której Ja was wprowadzę:
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo unene kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukutengeraniko
19 A jeść będziecie chleb onej ziemi, ofiarować będziecie ofiarę podnoszenia Panu.
ndipo mukakadya chakudya cha mʼdzikolo, mukapereke gawo lina kwa Yehova monga chopereka.
20 Z pierwszych ciast waszych placek ofiarować będziecie na ofiarę podnoszenia; jako ofiarę z bojewiska, tak go ofiarować będziecie.
Pa buledi wanu woyamba, mukapereke mmodzi monga nsembe, ngati chopereka chochokera ku malo wopunthira tirigu.
21 Z pierwszych ciast waszych ofiarować będziecie Panu ofiarę podnoszenia w narodziech waszych.
Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.
22 A gdybyście pobłądzili, i nie uczynilibyście wszystkich przykazań tych, które rozkazał Pan przez Mojżesza;
“‘Ndipo ngati muchimwa mosadziwa posasunga ena mwa malamulo awa amene Yehova wapereka kwa Mose,
23 Wszystkiego, co wam Pan rozkazał przez Mojżesza, od onego dnia, którego wydał Pan przykazanie, i potem w narodziech waszych:
lina lililonse mwa malamulo a Yehova amene wapereka kwa inu kudzera mwa Mose, kuyambira tsiku limene Yehova anawapereka mpaka mibado ya mʼtsogolo,
24 Tedy jeźliby z niewiadomości zgromadzenia stało się to pobłądzenie, wszystko zgromadzenie ofiarować będzie cielca młodego jednego na całopalenie, na wdzięczną wonność Panu, także śniedną ofiarę jego, i mokrą ofiarę jego według zwyczaju, i kozła jednego z stada za grzech.
ndipo ngati zimenezi zachitika osati mwadala ndipo gulu lonse silinadziwe, zikatero gulu lonselo lipereke mwana wangʼombe wamwamuna monga nsembe yopsereza kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova pamodzinso ndi chopereka chachakudya ndi chopereka cha chakumwa ndi mbuzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo potsata zimene zinalamulidwa.
25 Tak oczyści kapłan wszystko zgromadzenie synów Izraelskich, i będzie im odpuszczona, gdyż się z niewiadomości stało. A oni ofiarować będą ofiarę swoję na ofiarę ognistą Panu, i na ofiarę za grzech swój przed Panem za obłądzenie swoje.
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimo a gulu lonse la Aisraeli, ndipo adzakhululukidwa, pakuti linali tchimo lochita mosadziwa. Ndipo chifukwa cha tchimo lawolo, abweretse kwa Yehova nsembe yotentha pa moto ndi nsembe yopepesera machimo.
26 I będzie odpuszczono wszystkiemu zgromadzeniu synów Izraelskich, i przychodniowi, który mieszka między nimi, ponieważ wszystkiego ludu pobłądzenie jest.
Gulu lonse la Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo adzakhululukidwa chifukwa anthu onsewo anachimwa mosadziwa.
27 A jeźliby kto sam tylko zgrzeszył z niewiadomości, tedy przyniesie Panu kozę roczną na ofiarę za grzech;
“‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
28 I oczyści kapłan człowieka obłądzonego, któryby zgrzeszył z niewiadomości; przed Panem oczyści go, i będzie mu odpuszczono.
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimowo pamaso pa Yehova chifukwa cha munthu yemwe anachimwa mosadziwayo. Nsembe yopepesera tchimo lakelo ikaperekedwa, munthuyo adzakhululukidwa.
29 Tak zrodzonemu między synami Izraelskimi, jako przychodniowi, który mieszka między nimi, zakon jeden będzie wam, gdyby kto zgrzeszył z niewiadomości.
Lamulo lomweli ligwiritsidwe ntchito kwa aliyense wochimwa mosadziwa, kaya ndi mbadwa ya mu Israeli kapena mlendo.
30 Ale człowiek, któryby z hardości swawolnie zgrzeszył, tak urodzony w domu, jako i przychodzień, takowy Pana zelżył; przetoż wykorzeniony będzie on człowiek z pośrodku ludu swego.
“‘Koma aliyense amene achimwa mwadala, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, nachitira chipongwe Yehova, ameneyo achotsedwe ndithu pakati pa anthu ake.
31 Albowiem słowem Pańskiem pogardził, i przykazanie jego zgwałcił; koniecznie wytracony będzie takowy człowiek; nieprawość jego na nim zostanie.
Popeza wanyoza mawu a Yehova ndi kuphwanya malamulo ake. Munthu ameneyo achotsedwe ndithu, kuchimwa kwake kudzakhala pa iyeyo.’”
32 I stało się, gdy byli synowie Izraelscy na puszczy, że znaleźli człowieka zbierającego drwa w dzień sabatu.
Aisraeli ali mʼchipululu, munthu wina anapezeka akutola nkhuni tsiku la Sabata.
33 I przywiedli go, którzy go znaleźli zbierającego drwa, przed Mojżesza, i przed Aarona, i przed wszystko zgromadzenie.
Amene anamupeza akutola nkhunizo anabwera naye kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa gulu lonse
34 I dali go do więzienia; bo jeszcze im nie było oznajmiono, coby miano czynić z takowym.
ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa sankadziwa choti achite naye.
35 Tedy rzekł Pan do Mojżesza: śmiercią niech umrze człowiek ten; bez litości niechaj go ukamionuje wszystko zgromadzenie za obozem.
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Munthu ameneyu ayenera kuphedwa. Gulu lonse liyenera kumugenda ndi miyala kunja kwa msasa.”
36 I wywiedli go wszystko zgromadzenie za obóz, i ciskali nań kamieniem, aż umarł, jako rozkazał Pan Mojżeszowi.
Choncho gululo linamutengera kunja kwa msasa ndi kumupha pomugenda ndi miyala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
37 Zatem rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anawuza Mose kuti,
38 Mów do synów Izraelskich, a powiedz im, aby sobie poczynili bramy na krajach szat swoich w narodziech swych, a niech przyprawią do bram sznurek hijacyntowy.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira.
39 I będziecie mieli te bramy, żebyście poglądając na nie, wspominali sobie na wszystkie przykazania Pańskie, abyście je czynili, i abyście się nie unosili za sercem waszem, i za oczyma waszemi, za któremi wy idąc cudzołożylibyście.
Mudzakhala ndi mphonje zimenezi kuti mukaziona muzikakumbukira malamulo onse a Yehova ndi kuwamvera kuti musamatsatenso zilakolako za mʼmitima mwanu ndi za maso anu.
40 Ale żebyście pamiętali i czynili wszystkie przykazania moje, a byli świętymi Bogu waszemu.
Motero mudzakumbukira kumvera malamulo anga ndipo mudzakhala opatulikira a Mulungu wanu.
41 Ja Pan, Bóg wasz, którym was wywiódł z ziemi Egipskiej, abym wam był za Boga; Jam Pan, Bóg wasz.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”

< Liczb 15 >