< Micheasza 5 >

1 Zbierzże się teraz w hufy, o walecznico! oblęż nas; niech laską biją w lice sędziego Izraelskiego.
Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
2 Ale ty, Betlehemie Efrata! acześ najmniejszy między tysiącami Judzkimi, z ciebie mi jednak wyjdzie ten, który będzie panującym w Izraelu, a wyjścia jego są z dawna, ode dni wiecznych.
“Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
3 Przetoż choć ich wyda w rozproszenie aż do czasu, któregoby rodząca porodziła, wszakże ostatek braci jego nawrócą się z synami Izraelskimi.
Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
4 I stanie się a paść ich będzie w sile Pańskiej, i w sławie imienia Pana, Boga swego; i będą mieszkać, bo już wielmożnym będzie aż do granic ziemi.
Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
5 I będzie taki pokój, że gdy Assyryjczyk wtargnie w ziemię naszę, i gdy podepcze pałace nasze, tedy wystawimy przeciw niemu siedmiu pasterzy, i ośmiu książąt z ludu.
Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
6 Ci wypasą ziemię Assyryjską mieczem, i ziemię Nimrodową w granicach ich; a tak wyrwie nas Assyryjczykowi, gdy przyciągnie do ziemi naszej, i gdy będzie deptał granicę nasze.
Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
7 Przetoż ostatki Jakóbowe w pośrodku wielu narodów będą jako rosa od Pana, jako ciche deszcze skrapiające trawę, których się nie spodziewa od człowieka, ani ich czeka od synów ludzkich.
Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
8 Będą też ostatki Jakóbowe między poganami w pośrodku wielu narodów jako lew między zwierzętami leśnemi, a jako szczenię lwie między trzodą owiec, które gdy idzie, a depcze i łapie, niemasz nikogo, ktoby wydarł.
Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
9 Wywyższy się ręka twoja nad nieprzyjaciołmi twoimi, a wszyscy przeciwnicy twoi wykorzenieni będą.
Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
10 I stanie się dnia onego, mówi Pan, że wytracę konie twoje z pośrodku ciebie, a wozy twoje popsuję,
Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
11 I wygubię miasta ziemi twojej, a poburzę wszystkie twierdze twoje.
Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
12 Wygubię też gusła z ciebie, a wieszczków nie będzie w tobie.
Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
13 Wygubię też ryte bałwany twoje i obrazy twoje z pośrodku ciebie, a nie będziesz się więcej kłaniał robocie rąk twoich.
Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
14 Wykorzenię i gaje twoje z pośrodku ciebie, a wygładzę nieprzyjaciół twoich.
Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
15 A tak w gniewie i w zapalczywości wykonam pomstę nad narodami, które nie były posłuszne.
Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”

< Micheasza 5 >