< Micheasza 2 >

1 Biada tym, którzy wymyślają nieprawość, i knują złe na łożach swoich, a na świtaniu rano do skutku je przywodzą, gdyż to jest w mocy rąk ich.
Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
2 Pożądają pól, i wydzierają; także i domów, i odejmują; a tak przewodzą gwałt nad mężem i domem jego, nad każdym mężem i nad dziedzictwem jego.
Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
3 Dlatego tak mówi Pan: Oto Ja złe myślę przeciwko rodzajowi temu, z którego nie wyjmiecie szyj waszych, ani będziecie chodzić pysznie; bo czas zły będzie.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
4 W on dzień urośnie o was przypowieść, i narzekać będą nad wami płaczem żałośnym, mówiąc: Spustoszeniśmy do szczętu, Pan odmienił dział ludu mojego; o jakoć mi go odjął! jakoć wziąwszy pole nasze rozdzielił!
Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
5 Dlatego nie będziesz miał, ktoby rzucił sznurem na los w zgromadzeniu Pańskiem.
Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
6 Mówią: Nie prorokujcie, niech nam inni prorokują; bo nie prorokują tak jako ci; żaden z nich nie przestaje mów zelżywych.
Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
7 O ty ludu, który słyniesz domem Jakóbowym! izali ukrócony ma być duch Pański? Izali takowe są sprawy jego? Azaż słowa moje nie są dobre temu, który chodzi w uprzejmości?
Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
8 Wczoraj był ludem moim, a dziś jako nieprzyjaciel powstaje; mając odzienie, zdzieracie płaszcz z tych, którzy chodzą bezpiecznie, którzy się wracają z wojny;
Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
9 Żony ludu mego wyganiacie z domu rozkoszy ich, od dziatek ich ustawicznie odejmujecie sławę moję.
Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
10 Wstańcie, a odejdźcie, bo tu nie masz odpocznienia; pogubi was dla nieczystości, a to pogubieniem srogiem.
Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
11 Gdy się kto za proroka udaje, a kłamstwo opowiadając mówi: Będęć prorokował o winie albo o napoju mocnym: takowyć bywa miłym prorokiem ludu tego.
Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
12 Zgromadzając cale cię zgromadzę, Jakóbie! zgromadzając zgromadzę ostatki Izraela, a spędzę je w gromadę jako owce Bocra, jako trzodę w pośród obory jego, i wyjdzie huk od ludu.
“Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
13 Zstąpi ten, który przełamywać będzie przed nimi; przełamie, a przejdą bramą, i wnijdą przez nią; nawet i król ich pójdzie przed nimi, a Pan na czele ich.
Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”

< Micheasza 2 >