< Kapłańska 9 >

1 I stało się dnia ósmego, wezwał Mojżesz Aarona i synów jego, i starszych Izraelskich.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Mose anayitana Aaroni, ana ake ndi akuluakulu a Aisraeli.
2 I rzekł do Aarona: Weźmij sobie cielca młodego na ofiarę za grzech, i barana na ofiarę całopalenia, oboje zupełne, i ofiaruj je przed obliczem Pańskiem.
Ndipo anawuza Aaroni kuti, “Tenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yako yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza. Zonsezi zikhale zopanda chilema ndipo uzipereke pamaso pa Yehova.
3 Do synów zaś Izraelskich rzeczesz, mówiąc: Weźmijcie kozła z kóz na ofiarę za grzech, i cielca, i barana, roczniaki zupełne, zdrowe, na ofiarę całopalenia;
Kenaka uwawuze Aisraeli kuti, ‘Tengani mbuzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo. Mutengenso mwana wangʼombe ndi mwana wankhosa. Zonsezi zikhale za chaka chimodzi ndi zopanda chilema kuti zikhale nsembe yopsereza.
4 Także wołu, i barana na ofiary spokojne ku ofiarowaniu przed Panem, i ofiarę śniedną nagniecioną z oliwą; albowiem się wam dziś Pan ukaże.
Mutengenso ngʼombe yayimuna ndi nkhosa yayimuna kuti zikhale nsembe yachiyanjano zoti ziperekedwe pamaso pa Yehova. Pamodzi ndi izi mubwerenso ndi nsembe yachakudya yosakaniza ndi mafuta pakuti lero Yehova akuonekerani.’”
5 I przynieśli, co rozkazał Mojżesz, przed namiot zgromadzenia; a przystąpiwszy wszystek lud, stanął przed Panem.
Anthu anatenga zonse zimene Mose analamula nabwera nazo pa khomo la tenti ya msonkhano. Gululo linasendera pafupi ndi kuyima pamaso pa Yehova.
6 Zatem rzekł Mojżesz: Tać jest rzecz, którą wam Pan rozkazał; czyńcież ją, a ukaże się wam chwała Pańska.
Tsono Mose anati, “Izi ndi zimene Yehova walamula kuti muchite kuti ulemerero wa Yehova ukuonekereni.”
7 Rzekł zaś Mojżesz do Aarona: Przystąp do ołtarza, a uczyń ofiarę za grzech swój, i ofiarę paloną twoję, a wykonaj oczyszczenie za się i za lud; uczyń też ofiarę od ludu, i uczyń oczyszczenie za lud, jako rozkazał Pan.
Pambuyo pake Mose anawuza Aaroni kuti, “Sendera pafupi ndi guwa ndipo upereka nsembe yako yopepesera machimo ndi nsembe yako yopsereza ndikuchita mwambo wopepesera machimo ako ndi machimo a anthu. Anthuwa apereke nsembe zawo zopepesera machimo monga momwe Yehova walamulira.”
8 Tedy przystąpił Aaron do ołtarza, i zabił cielca na ofiarę za grzech swój.
Choncho Aaroni anasendera pafupi ndi guwa, napha mwana wangʼombe uja kukhala nsembe yake yopepesera machimo.
9 I podali mu synowie Aaronowi krew, który omoczywszy palec swój we krwi pomazał rogi ołtarza, a ostatek krwi wylał u spodku ołtarza;
Ana a Aaroni anabwera ndi magazi kwa Aaroni ndipo iye anaviyika chala chake mʼmagaziwo, nawapaka pa nyanga za guwa. Magazi wotsalawo anawathira pa tsinde la guwalo.
10 Ale tłustość z nerkami, i odzieczkę z wątrobą z ofiary za grzech spalił na ołtarzu, jako był rozkazał Pan Mojżeszowi;
Kenaka anatentha paguwapo, mafuta, impsyo pamodzi ndi mafuta amene amakuta chiwindi ngati nsembe yopepesera machimoyo, monga momwe Yehova analamulira Mose.
11 Mięso zaś i skórę spalił ogniem precz za obozem.
Koma nyama ndi chikopa anazitenthera kunja kwa msasa.
12 Zabił też ofiarę całopalenia; i podali mu synowie Aaronowi krew, którą pokropił wierzch ołtarza w około.
Kenaka anapha nsembe yopsereza. Ana a Aaroni atabwera ndi magazi kwa iye, Aaroniyo anawawaza mbali zonse za guwa.
13 Przynieśli mu też ofiarę całopalenia, i sztuki jej i głowę jej; a spalił ją na ołtarzu;
Ana akewo anamupatsa nyama yoduladula ya nsembe yopsereza ija pamodzi ndi mutu ndipo anazitentha pa guwa.
14 Omył też wnętrzności, i nogi, i spalił je z ofiarą całopalenia na ołtarzu.
Aaroni anatsuka matumbo ndi miyendo nazitentha pa guwa pamodzi ndi nsembe yopsereza ija.
15 Potem sprawował ofiarę wszystkiego ludu, i wziął kozła na ofiarę za grzech ludu, którego zabił, i ofiarował go, jako i pierwszego.
Kenaka Aaroni anapereka zopereka za anthuwo. Anatenga mbuzi yopepesera machimo a anthuwo, yopereka chifukwa cha tchimo, nayipha ndi kuyipereka kuti ikhale yopepesera machimo monga anachitira ndi nsembe yoyamba ija.
16 Ofiarował też ofiarę całopalenia, i uczynił jej według zwyczaju.
Anabwera ndi nsembe yopsereza, nayipereka potsata mwambo wake.
17 Ofiarował też ofiarę śniedną, a wziąwszy z niej pełną garść swoję, spalił na ołtarzu oprócz ofiary całopalenia porannej.
Anabweranso ndi chopereka cha chakudya. Anatapa ufa dzanja limodzi ndi kutentha pa guwa, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa ija.
18 Zabił też wołu, i barana na ofiarę spokojną, która była za lud; i podali mu synowie Aaronowi krew, którą pokropił ołtarz z wierzchu około.
Tsono Aaroni anapha ngʼombe ndi nkhosa yayimuna monga nsembe yachiyanjano ya anthu. Ana ake anamupatsira magazi ndipo anawawaza mbali zonse za guwa.
19 Podali mu także tłustość z wołu, i z barana ogon, i tłustość okrywającą wnętrzności i nerki, i odzieczkę z wątroby.
Anamupatsiranso mafuta a ngʼombeyo ndi nkhosa yayimunayo: mchira wamafuta, mafuta wokuta matumbo, impsyo ndi mafuta wokuta chiwindi.
20 Włożyli też tłustości na mostek, i spalili też tłustość na ołtarzu;
Ana a Aaroni anayika mafutawo pa zidale. Pambuyo pake Aaroni anatentha mafutawo pa guwa lansembe.
21 Ale mostek i łopatkę prawą obracał Aaron tam i sam na ofiarę obracania przed obliczem Pańskiem, jako był Pan rozkazał Mojżeszowi.
Koma zidale ndi ntchafu ya kumanja Aaroni anaziweyula ngati chopereka choweyula pamaso pa Yehova.
22 Tedy podniósłszy Aaron ręce swe do ludu błogosławił im, a zstąpił od ofiarowania ofiary za grzech, i ofiary całopalenia, i ofiary spokojnej.
Kenaka Aaroni anakweza manja ake pa anthuwo nawadalitsa. Ndipo atatha kupereka nsembe yopepesera machimo, nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano, anatsika pa guwapo.
23 I wszedł Mojżesz i Aaron do namiotu zgromadzenia, a wszedłszy błogosławili ludowi; i okazała się chwała Pańska wszystkiemu ludowi;
Ndipo Mose pamodzi ndi Aaroni analowa mu tenti ya msonkhano. Atatulukamo anadalitsa anthuwo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa anthu onse.
24 Bo zstąpiwszy ogień od obliczności Pańskiej spalił na ołtarzu ofiarę całopalenia i tłustości; co gdy widział wszystek lud, wykrzykali a padali na twarzy swoje.
Pomwepo moto unatuluka pamaso pa Yehova niwutentha nsembe zopsereza ndi mafuta zimene zinali pa guwa. Anthu onse ataona zimenezi anafuwula mwachimwemwe ndipo anaweramitsa nkhope zawo pansi.

< Kapłańska 9 >