< Kapłańska 27 >

1 Potem rzekł Pan do Mojżesza, mówiąc:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Mów do synów Izraelskich, a powiedz im: Gdyby człowiek ślubem poślubił duszę Panu, według szacunku twego da okup.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole,
3 A będzie tak szacunek twój: Za mężczyznę od dwudziestu lat aż do sześćdziesiąt lat, będzie szacunek twój pięćdziesiąt syklów srebra według wagi świątnicy.
mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60.
4 A jeźli jest biała głowa szacunek twój będzie trzydzieści syklów,
Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu.
5 A jeźli od piątego roku aż do dwudziestego roku, tedy będzie szacunek twój za mężczyznę dwadzieścia syklów a za białą głowę dziesięć syklów.
Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi.
6 A jeźli za dziecię od jednego miesiąca aż do pięciu lat, tedy będzie szacunek twój za mężczyznę pięć syklów srebra, a za dzieweczkę szacunek twój trzy sykle srebra.
Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva.
7 A jeźli od sześćdziesiąt lat i wyżej będzieli mężczyzna tedy będzie szacunek twój piętnaście syklów a za białą głowę dziesięć syklów.
Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi.
8 Lecz jeźliby był tak ubogi, żeby nie mógł oddać szacunku twego, tedy go stawią przed kapłana, i oszacuje go kapłan, według przemożenia tego który ślubował, oszacuje go kapłan.
Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.
9 Jeźliby też bydlę z tych, które się ofiarują na ofiarę Panu, poślubił, każde, które odda Panu będzie święte.
“‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika.
10 Nie odmieni go, ani da innego za nie, lepszego za gorsze, albo gorszego za lepsze; jeźliby też jakokolwiek odmienił bydlę za bydlę, tedy i ono, i to, które za nie dano będzie święte.
Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika.
11 A jeźliby które nie czyste bydlę poślubił z tych, co nie bywają ofiarowane Panu, tedy stawi to bydlę przed kapłana,
Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe,
12 I oszacuje kapłan bądź dobre, bądź złe, a jako je oszacuje kapłan, tak będzie.
ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
13 A jeźliby je kto odkupić chciał, przyda piątą część nad szacunek twój.
Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.
14 Jeźliby też kto poświęcił dom swój, żeby był święty Panu, tedy go oszacuje kapłan bądź dobry, bądź zły; jako go oszacuje kapłan, tak zostanie.
“‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
15 A gdyby ten, który poświęcił, chciał odkupić dom swój, przyda piątą część pieniędzy na szacunek twój, i będzie jego.
Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.
16 Jeźli też kto część roli z dziedzictwa swego poświęcił Panu tedy będzie szacunek twój według zasiewku jej; gdzie się wysieje chomer jęczmienia, za pięćdziesiąt syklów srebra szacowane będzie.
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu.
17 Jeźli do miłościwego lata poświęcił rolę swoję, według szacunku twego zostanie.
Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa.
18 Ale jeźliżby po miłościwem lecie poświęcił rolę twoję tedy kapłan obrachuje mu pieniądze według lat zostawających do miłościwego lata i umniejszy mu się z szacunku twego.
Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo.
19 A chciałliby odkupić rolą, ten, który ją poświęcił, przyda piątą część pieniędzy do szacunku twego i zostanie przy niej.
Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake.
20 Ale gdzie by nie odkupił roli onej, a sprzedana by była rola komu inszemu, nie może być odkupiona.
Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso.
21 I będzie ona rola, gdy wynijdzie miłościwe lato święta Panu, jako rola poświęcona a przyjdzie w osiadłość kapłanowi.
Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.
22 A jeźliby kto rolą kupioną, która nie była z ról dziedzictwa jego poślubił Panu.
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake,
23 Tedy porachuje mu kapłan sumę szacunku twego aż do roku miłościwego, i da szacunek ten dnia onego za rzecz poświęconą Panu.
wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova.
24 A w miłościwe lato wróci się rola od tego, od kogo ją kupiono, do tego, który dziedzicznie trzymał rolą onę.
Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake.
25 A każdy szacunek twój będzie wedle sykla świątnicy, a dwadzieścia pieniędzy sykiel waży.
Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.
26 Wszakże pierworodnego, a które prawem pierworodztwa bywa ofiarowane Panu z bydła, nikt go nie poświęci, bądź wół bądź owca, ponieważ Pańskie są.
“‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova.
27 A jeźliby z bydląt nieczystych było, odkupi je według szacunku twego, i przyda piątą część nad to; a jeźliby go nie odkupiono, niechże sprzedane będzie według szacunku twego.
Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.
28 Każda jednak rzecz poślubiona, którą by kto poślubił Panu ze wszystkiego, co ma z ludzi, i z bydła, i z ról osiadłości swojej, nie będzie sprzedawana, ani odkupowana; bo wszelka rzecz poślubiona najświętsza jest Panu.
“‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.
29 Wszelkie bydlę poślubione, które się pod ślubem oddawa, od człowieka nie będzie odkupione, ale śmiercią umrze.
“‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.
30 Wszystkie także dziesięciny ziemi z nasienia ziemi, z owocu drzewa, Pańskie są; bo poświęcone są Panu.
“‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova.
31 Ale kto by chciał odkupić co z dziesięcin swoich, piątą część ceny przyda do nich.
Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo.
32 Także wszystkie dziesięciny z rogatego bydła, i z drobnego bydła, wszystkiego, co przechodzi pod laską pasterską, każde dziesiąte będzie poświęcone Panu.
Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova.
33 Nie będzie przebierał między dobrem albo złem, ani go odmieniać będzie; a jeźliby je jakokolwiek odmienił, będzie to i ono odmienione poświęcone, nie ma być odkupione.
Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’”
34 Teć są przykazania, które rozkazał Pan Mojżeszowi do synów Izraelskich na górze Synaj.
Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.

< Kapłańska 27 >