< Lamentacje 5 >

1 Wspomnij, Panie! na to, co się nam przydało; wejrzyj a obacz pohańbienie nasze.
Inu Yehova, kumbukirani zimene zinatichitikira; yangʼanani ndipo muone kunyozeka kwathu.
2 Dziedzictwo nasze obrócone jest do obcych, a domy nasze do cudzoziemców.
Apereka cholowa chathu kwa obwera, nyumba zathu kwa alendo.
3 Sierotamiśmy a bez ojca; matki nasze są jako wdowy.
Takhala amasiye ndi wopanda abambo, amayi athu ali ngati akazi amasiye.
4 Wody nasze za pieniądze pijemy, drwa nasze za pieniądze kupujemy.
Tiyenera kugula madzi amene timamwa, nkhuni zathunso nʼzogula.
5 Na szyi swej prześladowanie cierpiemy, pracujemy, a nie dadzą nam odpocząć.
Otilondola atigwira pakhosi; tafowoka ndipo sakutilola kupumula.
6 Egipczykom podajemy rękę i Assyryjczykom, żebyśmy się nasycili chleba.
Tinadzipereka kwa Aigupto ndi kwa Asiriya kuti tipeze chakudya.
7 Ojcowie nasi zgrzeszyli, niemasz ich, a my nieprawość ich ponosimy.
Makolo athu anachimwa ndipo anafa kale, koma chilango chawo chili pa ife.
8 Niewolnicy panują nad nami, niemasz, ktoby nas wybawił z ręki ich.
Akapolo akutilamulira, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe angatimasule mʼdzanja lawo.
9 Z odwagą duszy naszej szukamy chleba swego dla strachu miecza i na puszczy.
Timapeza chakudya chathu poyika miyoyo yathu pa chiswe chifukwa cha lupanga mʼchipululu.
10 Skóra nasza jako piec zczerniała od srogości głodu.
Khungu lathu latentha ngati uvuni mʼngʼanjo, chifukwa cha kuwawa kwa njala.
11 Niewiasty w Syonie pogwałcono; i panny w miastach Judzkich.
Amayi agwiriridwa mu Ziyoni, ndi anamwali mʼmizinda ya Yuda.
12 Książęta ręką ich powieszeni są, a osoby starszych nie mają w uczciwości.
Akalonga athu akuwapachika pomangirira manja awo, akuluakulu sakuwalemekeza.
13 Młodzięców do żarn biorą, a młodzieniaszkowie po drwami padają.
Achinyamata akukakamizidwa kupera tirigu; anyamata akudzandira ndi mitolo ya nkhuni.
14 Starcy w bramach więcej nie siadają, a młodzieńcy przestali pieśni swoje.
Akuluakulu anachokapo pa chipata cha mzinda; achinyamata aleka nyimbo zawo.
15 Ustało wesele serca naszego, pląsanie nasze w kwilenie się obróciło.
Chimwemwe chachoka mʼmitima yathu; kuvina kwathu kwasanduka maliro.
16 Spadła korona z głowy naszej; biada nam, żeśmy zgrzeszyli!
Chipewa chathu chaufumu chagwa pamutu pathu. Tsoka kwa ife, chifukwa tachimwa!
17 Dlategoż mdłe jest serce nasze, dlatego zaćmione są oczy nasze;
Mitima yathu yakomoka chifukwa cha zimenezi, chifukwa cha zinthu zimenezi maso athu sakuona bwino,
18 Dla góry Syońskiej, że jest spustoszona, liszki chodzą po niej.
pakuti phiri la Ziyoni, limene lasanduka bwinja, nkhandwe zikungoyendayendapo.
19 Ty, Panie! trwasz na wieki, a stolica twoja od narodu do narodu.
Inu Yehova, lamulirani kwamuyaya; mpando wanu waufumu udzakhalabe ku mibadomibado.
20 Przeczże nas na wieki zapominasz, a opuszczasz nas przez tak długi czas?
Chifukwa chiyani mumatiyiwala nthawi zonse? Chifukwa chiyani mwatitaya nthawi yayitali chotere?
21 Nawróć nas do siebie, o Panie! a nawróceni będziemy; odnów dni nasze, jako z dawna były.
Yehova mutitembenuzire kwa Inu, kuti tibwerere; mukonzenso masiku athu akhale monga akale,
22 Bo izali nas cale odrzucisz, a gniewać się będziesz na nas tak bardzo?
pokhapokha ngati mwatitaya kotheratu, ndi kuti mwatikwiyira kobzola muyeso.

< Lamentacje 5 >