< Jozuego 7 >

1 Ale zgrzeszyli synowie Izraelscy przestępstwem przy rzeczach przeklętych; albowiem Achan, syn Charmiego, syna Zabdy, syna Zare, z pokolenia Juda, wziął nieco z rzeczy przeklętych; zaczem zapalił się gniew Pański przeciw synom Izraelskim.
Koma Aisraeli anachita zachinyengo ndi lamulo lija loti asatenge kalikonse koyenera kuwonongedwa. Akani mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera, wa fuko la Yuda anatengako zinthu zina. Choncho Yehova anakwiyira Israeli kwambiri.
2 Bo gdy posłał Jozue kilka mężów z Jerycha do Haj, które było blisko Betawen na wschód słońca od Betel, i rzekł do nich, mówiąc: Idźcie, a wyszpiegujcie ziemię; tedy szedłszy oni mężowie, wyszpiegowali Haj.
Tsono Yoswa anatuma anthu kuchokera ku Yeriko kukazonda ku mzinda wa Ai umene uli pafupi ndi mzinda wa Beti-Aveni kummawa kwa Beteli, ndipo anawawuza kuti, “Pitani mukazonde chigawochi.” Anthuwo anapitadi kukazonda Ai.
3 A wróciwszy się do Jozuego, rzekli mu: Niech nie ciągnie wszystek lud; około dwóch tysięcy mężów, albo około trzech tysięcy mężów niech idą, a zburzą Haj; nie trudź tam wszystkiego ludu, bo ich tam trocha.
Atabwera kwa Yoswa, anamuwuza kuti, “Sikofunika kuti apite anthu onse kukathira nkhondo mzinda wa Ai. Mutumizeko anthu 2,000 kapena 3,000 kuti akatenge mzindawo. Musawatume anthu onse kumeneko popeza kuli anthu ochepa.”
4 Poszło tedy około trzech tysięcy mężów z ludu, i uciekli przed mężami z Haj.
Choncho kunapita anthu 3,000. Koma iwo anathamangitsidwa ndi anthu a ku Ai.
5 A porazili z nich mężowie z Haj około trzydziestu i sześciu mężów, goniąc je od bramy aż do Sabarym, a porazili je, gdy uciekali z góry, i dla tego rozpłynęło się serce ludu, i było jako woda.
Anthu a ku Ai anathamangitsa Aisraeli kuchokera pa chipata cha mzindawo mpaka ku ngwenya ndipo anapha anthu 36. Iwowa anawapha pamene ankatsika phiri. Choncho mitima ya anthu inasweka ndipo analibenso mphamvu.
6 Tedy rozdarłszy Jozue odzienie swoje, upadł twarzą swoją na ziemię przed skrzynią Pańską, a leżał aż do wieczora, on i starsi Izraelscy, posypawszy prochem głowy swoje.
Tsono Yoswa anangʼamba zovala zake nagwada nʼkuweramitsa mutu wake pansi patsogolo pa Bokosi la Yehova. Akuluakulu a Israeli nawonso anadzigwetsa pansi ndipo anakhala pomwepo mpaka madzulo atadziwaza fumbi kumutu kwawo.
7 Zatem rzekł Jozue: Ach! Panie Panujący, przeczżeś przeprowadził lud ten za Jordan, abyś nas podał w rękę Amorejczyka na wytracenie? O byśmy byli raczej mieszkali za Jordanem!
Ndipo Yoswa anati, “Kalanga ine, Ambuye Wamphamvuzonse chifukwa chiyani munatiwolotsa Yorodani? Kodi mumalinga zotipereka mʼmanja mwa Aamori kuti atiwononge chotere? Kukanakhala kwabwino ife tikanakhala tsidya linalo la Yorodani!
8 O Panie, cóż rzekę, ponieważ podawa Izrael tył nieprzyjaciołom swoim?
Tsono Ambuye, ine ndinene chiyani, pakuti tsopano Israeli anathamangitsidwa ndi adani ake?
9 Bo usłyszawszy Chananejczycy, i wszyscy obywatele tej ziemi, obtoczą nas zewsząd, a wytracą imię nasze z ziemi. I cóż to uczynisz imieniowi twemu wielkiemu?
Akanaani ndi anthu ena a dziko lino adzamva zimenezi ndipo adzatizinga ndi kutiwonongeratu. Nanga inu mudzatani ndi dzina lanu lamphamvulo?”
10 Tedy rzekł Pan do Jozuego: Wstań; przeczżeś upadł na oblicze twoje?
Koma Yehova anati kwa Yoswa, “Imirira! Chifukwa chiyani wagwada pansi chotere?
11 Zgrzeszył Izrael, i przestąpili przymierze moje, którem im przykazał; albowiem wzięli z rzeczy przeklętych, a ukradli je, i skłamali, i schowali je między naczynie swoje.
Aisraeli achimwa. Iwo aphwanya pangano limene ndinawalamula kuti asunge. Anatengako zinthu zina zofunika kuwonongedwa. Choncho anabako, ananena bodza ndi kuyika zinthu zakubazo pamodzi ndi katundu wawo.
12 A dla tegoć synowie Izraelscy nie będą się mogli ostać przed nieprzyjacioły swymi, tył będą podawali nieprzyjaciołom swym, bo się zmazali rzeczą przeklętą; nie będę więcej z wami, jeźli nie wykorzenicie przeklęstwa tego z pośrodku was.
Nʼchifukwa chake Aisraeli sangathe kulimbana ndi adani awo. Iwo anathawa pamaso pa adani awo chifukwa ndiwo oyenera kuwonongedwa. Ine sindikhalanso ndi inu pokhapokha mutawononga chilichonse choyenera kuwonongedwa pakati panu.
13 Wstań, poświęć lud i rzeczy: Poświęćcie się na jutro; bo tak mówi Pan, Bóg Izraelski: Przeklęstwo jest w pośrodku ciebie, Izraelu; nie ostoisz się przed nieprzyjacioły twymi, aż odejmiecie przeklęstwo z pośrodku siebie.
“Nyamuka, ukawawuze anthu kuti, ‘Mudzipatule nokha kukonzekera kuonana nane mawa; pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti choyenera kuwonongedwa chija chili pakati panu, inu Aisraeli. Simungathe kulimbana ndi adani anu mpaka mutachichotsa.’
14 A tak przystąpcie rano według pokoleń waszych; a pokolenie, które okaże Pan, przystąpi według familii; a familija, którą okaże Pan, przystąpi według domów; a dom, który okaże Pan, przystąpi według osób.
“Mawa mmamawa adzabwere pamaso pa Yehova fuko limodzilimodzi. Fuko limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo mbumba imodziimodzi. Tsono mbumba imene Yehova adzayiloze idzabwere patsogolo banja limodzilimodzi. Banja limene Yehova adzaliloze lidzabwere patsogolo munthu mmodzimmodzi.
15 A kto będzie znaleziony w przeklęstwie, będzie spalony ogniem, on, i wszystko, co jego jest, dla tego że przestąpił przymierze Pańskie, a dopuścił się niegodnej rzeczy w Izraelu.
Iye amene adzagwidwe ndi zinthu zoyenera kuwonongedwazo adzawotchedwa ndi moto, pamodzi ndi banja lake lonse ndi zinthu zake zonse. Iyeyutu wachita chinthu chonyansa pakati pa Aisraeli ndi kuphwanya pangano limene anthu anga anachita ndi Ine!”
16 Przetoż wstawszy Jozue rano, rozkazał przystępować Izraelowi według pokoleń ich; i znalazło się pokolenie Juda.
Mmawa mwake Yoswa anabweretsa Israeli fuko limodzilimodzi ndipo fuko la Yuda linalozedwa.
17 I kazał przystąpić familii Juda, i znalazła się familija Zare, i kazał przystąpić familii Zarego według osób, i znalazł się dom Zabdy.
Anabweretsa poyera mbumba zonse za fuko la Yuda, ndipo mbumba ya Zera inagwidwa. Kenaka anatulutsa poyera mabanja onse a mbumba ya Zera ndipo banja la Zabidi linagwidwa.
18 I kazał przystąpić domowi jego według osób, i znalazł się Achan, syn Charmiego, syna Zabdy, syna Zare, z pokolenia Juda.
Potsiriza anatulutsa anthu onse a banja la Zabidi ndipo Akani anagwidwa. Iyeyu anali mwana wa Karimi, mwana wa Zabidi, mwana wa Zera wa fuko la Yuda.
19 I rzekł Jozue do Achana: Synu mój, daj proszę chwałę Panu, Bogu Izraelskiemu, i wyznaj przed nim, a oznajmij mi proszę, coś uczynił, nie taj przede mną.
Ndipo Yoswa anati kwa Akani, “Mwana wanga pereka ulemerero kwa Yehova Mulungu wa Israeli ndipo umuyamike Iye. Ndiwuze zimene wachita, ndipo usandibisire.”
20 Tedy odpowiedział Achan Jozuemu, mówiąc: Zaprawdę, jam zgrzeszył Panu, Bogu Izraelskiemu, tak a tak uczyniłem.
Akani anayankha kuti, “Zoona! Ine ndachimwira Yehova Mulungu wa Israeli. Chimene ndachita ine ndi ichi:
21 Widziałem między łupy płaszcz babiloński jeden, piękny, i dwieście syklów srebra, i pręt złoty jeden, pięćdziesiąt syklów ważący, i pożądałem tego, i wziąłem to, a oto, te rzeczy są zakopane w ziemi, w pośród namiotu mego, a srebro pod niemi.
Ndinaona mwa zinthu zolanda ku nkhondo zija, mkanjo wokongola wa ku Babuloni, makilogalamu awiri a siliva ndiponso golide wolemera theka la kilogalamu. Zimenezi ndinazikhumba ndipo ndinazitenga. Ndazibisa mʼkati mwa tenti yanga, ndipo siliva ali pansi pake.”
22 Tedy posłał Jozue posły, którzy bieżeli do namiotu, a oto te rzeczy były skryte w namiocie jego, a srebro pod niemi.
Motero Yoswa anatuma anthu, ndipo anathamanga kupita ku tenti. Anthuwo anakapeza kuti zinthuzo zinabisidwadi mʼtenti yake, ndipo siliva analidi pansi pake.
23 A wziąwszy je z namiotu przynieśli je do Jozuego, i do wszystkich synów Izraelskich, a położyli je przed obliczem Pańskiem.
Iwo anazichotsa zinthuzo mu tenti yake nabwera nazo kwa Yoswa ndi kwa Aisraeli onse ndipo anaziyika pamaso pa Yehova.
24 A tak wziąwszy Jozue, i wszystek Izrael z nim, Achana, syna Zarego, i srebro, i płaszcz, i pręt złoty, i syny jego, i córki jego, i woły jego, i osły jego, i owce jego, i namiot jego, i wszystko co miał, wywiedli je na dolinę Achor.
Kenaka Yoswa pamodzi ndi Aisraeli onse anatenga Akani mwana wa Zera pamodzi ndi siliva, mkanjo, golide zimene anapezeka nazo zija. Anatenganso ana ake aamuna ndi aakazi, ngʼombe zake, abulu ndi nkhosa, tenti yake ndi zonse anali nazo, kupita nazo ku chigwa cha Akori.
25 I rzekł Jozue: Przeczżeś nas potrwożył? niechże cię też Pan zatrwoży dnia tego. I ukamionował go wszystek Izrael, i spalili je ogniem, ukamionowawszy je kamieńmi;
Yoswa anati “Chifukwa chiyani wabweretsa mavuto awa pa ife? Yehova ndiye abweretse mavuto pa iwe lero.” Kenaka Aisraeli onse anaponya miyala Akani, namupha. Anaponyanso miyala banja lake lonse, nʼkulipha. Pambuyo pake anatentha Akani uja, banja lake ndi zonse zimene anali nazo.
26 Potem wystawili na nim wielką kupę kamieni, która trwa aż do dnia tego. I odwrócił się Pan od gniewu zapalczywości swojej; przetoż nazwane jest imię miejsca onego, dolina Achor, aż do dnia dzisiejszego.
Anawunjika mulu waukulu wa miyala pa Akani, imene ilipobe mpaka lero. Nʼchifukwa chake malowa amatchedwa chigwa cha Akori mpaka lero. Ndipo Yehova anachotsa mkwiyo wake.

< Jozuego 7 >