< Jozuego 13 >

1 I zstarzał się Jozue, a był zeszły w leciech. I rzekł Pan do niego: Tyś się zstarzał, a zszedłeś w leciech, a ziemi zostawa bardzo wiele ku posiadaniu.
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 Tać jest ziemia, która pozostawa: Wszystkie granice Filistynów, i wszyscy Gessurytowie,
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 Od Nilu, który oblewa Egipt, aż do granicy Akaronu na północy, przynależy Chananejczykowi, pięcioro księstw Filistyńskich; Asackie, i Asdodziejskie, Askalońskie, Getejskie, i Akaronicki, i Hawejczycy.
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 Od południa wszystka ziemia Chananejska, i Mara, które jest Sydończyków aż do Afeka, i aż do granicy Amorejczyka;
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 I ziemia Giblitów ze wszystkim Libanem na wschód słońca, od Baalgad pod górę Hermon, aż gdzie chodzą do Emat.
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 Wszystkie mieszkające na górach od Libanu aż do wód gorących, wszystkie Sydończyki Ja wypędzę przed syny Izraelskimi; tylko ją podziel Izraelitom w dziedzictwo, jakom ci rozkazał.
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 Przetoż teraz rozdziel tę ziemię w dziedzictwo, dziewięciorgu pokoleniu, i połowie pokolenia Manasesowego.
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 Gdyż z drugą połową Rubenitowie i Gadytowie wzięli dziedzictwo swoje, które im dał Mojżesz za Jordanem na wschód słońca, jako im dał Mojżesz, sługa Pański;
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 Od Aroer, które jest nad brzegiem potoku Arnon, i miasto, które jest w pośrodku potoku, i wszystkę równinę Medeba aż do Dybon;
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 I wszystkie miasta Sehona, króla Amorejskiego, który królował w Hesebon, aż do granicy synów Ammonowych;
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 Także Galaad, i granice Gessurytów, i Machatytów, i wszystkę górę Hermon, i wszystko Basan aż do Salecha;
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 Wszystko królestwo Oga w Basan, który królował w Astarot, i w Edrej; ten był pozostał z Refaimitów, a pobił je Mojżesz i wygładził je.
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 Ale nie wygnali synowie Izraelscy Gessurytów i Machatytów; przetoż mieszkał Gessur i Machat w pośród Izraelczyków aż do dnia tego.
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 Tylko pokoleniu Lewi nie dał dziedzictwa; ofiary ogniste Pana Boga Izraelskiego są dziedzictwem jego, jako mu powiedział Bóg.
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 A tak oddał Mojżesz pokoleniu synów Rubenowych dziedzictwo według familii ich.
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 I była granica ich od Aroer, które jest nad brzegiem potoku Arnon, i miasto, które jest w pośród potoku, i wszystka równina ku Medeba.
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 Hesebon, i wszystkie miasta jego, które były w równinie; Dybon i Bamot Baal, i Bet Baal Meon;
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
18 I Jassa, i Cedymot, i Mefaat;
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 I Karyjataim, i Sebama, i Saratasar na górze w dolinie;
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
20 I Betfegor, i Asdod, Fazga, i Betyjesymot.
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 Wszystkie też miasta w równinie, i wszystko królestwo Sehona, króla Amorejskiego, który królował w Hesebon, którego zabił Mojżesz, i książęta Madyjańskie Ewi, i Recem, i Sur, i Hur, i Reba; książęta Sehonowe, obywatele ziemi.
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 I Balaama, syna Boerowego, wieszczka, zabili synowie Izraelscy mieczem z innymi pobitymi.
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 Była tedy granica synów Rubenowych Jordan z granicami swemi. Toć jest dziedzictwo synów Rubenowych według domów ich, miast i wsi ich.
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 Dał też Mojżesz pokoleniu Gad, synom Gadowym, według domów ich dziedzictwo.
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 A były ich granice Jazer i wszystkie miasta Galaad, i połowa ziemi synów Ammonowych aż do Aroer, które jest przeciw Rabba;
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 I od Hesebon aż do Ramat Massa i Betonim, a od Mahanaim aż do granicy Dabir.
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 W dolinie też Beram, i Betnimra, i Sochot, i Safon, ostatek królestwa Sehona, króla Hesebońskiego, Jordan i pogranicze jego aż do końca morza Cynneret za Jordanem na wschód słońca.
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 Toć jest dziedzictwo synów Gad według domów ich, miast i wsi ich.
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 Nadto dał Mojżesz osiadłość połowie pokolenia Manasesowego, i była ta połowa pokolenia synów Manasesowych według domów ich.
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 Była granica ich od Machanaim wszystko Basan i wszystko królestwo Oga, króla Basańskiego, i wszystkie wsi Jairowe, które są w Basan, sześćdziesiąt miast.
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 I połowę Galaad, i Astarot, i Erdej, miasta królestwa Oga w Basan, dał synom Machyra, syna Manasesowego, połowie synów Machyrowych według domów ich.
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 Teć są osiadłości, które podzielił Mojżesz w polach Moabskich za Jordanem przeciw Jerychu na wschód słońca.
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 Ale pokoleniu Lewi nie dał Mojżesz dziedzictwa; bo Pan, Bóg Izraelski, sam jest dziedzictwem ich, jako im powiedział.
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

< Jozuego 13 >