< Hioba 9 >

1 I odpowiedział Ijob, a rzekł:
Ndipo Yobu anayankha kuti,
2 Prawdziwieć wiem, że tak jest; bo jakożby miał być usprawiedliwiony człowiek przed Bogiem?
“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona. Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?
3 Jeźliby się z nim chciał spierać, nie odpowie mu z tysiąca na jednę rzecz.
Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye, Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.
4 Mądry jest sercem, i mocny siłą; któż użył pokoju, stawiwszy się mu upornie?
Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka. Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?
5 On przenosi góry, a nie wiedzą ludzie, kto je podwraca w gniewie swym.
Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa, ndipo amawagubuduza ali wokwiya.
6 On wzrusza ziemię z miejsca swego, a słupy jej trzęsą się.
Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.
7 Gdy on zakaże słońcu, nie wschodzi; i gwiazdy pieczętuje.
Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala; Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.
8 On sam rozpościera niebiosa, i depcze po wałach morskich.
Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.
9 On sprawił wóz niebieski z gwiazd, Oryjona i Hyjady, i inne gwiazdy skryte na południe.
Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana, nsangwe ndi kumpotosimpita.
10 On czyni rzeczy wielkie, a niewybadane i dziwne, którym niemasz liczby.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka, zodabwitsa zimene sizingawerengeke.
11 Oto, idzieli mimo mię, nie widzę go; a przychodzili, nie baczę go.
Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona; akadutsa, sindingathe kumuzindikira.
12 Oto gdy co porwie, któż go przymusi, aby przywrócił? Albo któż mu rzecze: Cóż czynisz?
Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa? Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’
13 Gdyby Bóg nie odwrócił gniewu swego, upadliby przed nim pomocnicy hardzi.
Mulungu sabweza mkwiyo wake; ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.
14 Jakoż mu ja tedy odpowiem? Jakie słowa obiorę przeciwko niemu?
“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji? Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?
15 Któremu, chociażbym był sprawiedliwym, nie odpowiem; owszem się sędziemu memu upokorzę.
Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe; ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.
16 Choćbym go wzywał, a onby mi się ozwał, przecię nie wierzę, aby przypuścił do uszów głos mój:
Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera, sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.
17 Bo mię starł w wichrze, i rozmnożył rany moje bez przyczyny;
Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho, ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.
18 Nie dopuszcza mi odetchnąć, owszem mię nasyca gorzkościami.
Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso koma akanandichulukitsira zowawa.
19 Jeźli się udam do mocy, oto on najmocniejszy; a jeźli do sądu, któż mię z nim sprowadzi?
Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi! Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?
20 Jeźlibym się usprawiedliwiał, usta moje potępią mię; jeźlibym się doskonałym czynił, tedy mię przewrotnym być pokaże.
Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa; ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.
21 Chociażbym był doskonały, przecież ja tego do siebie znać nie będę; ale dam naganę żywotowi memu.
“Ngakhale ine ndili wosalakwa, sindidziyenereza ndekha; moyo wanga ndimawupeputsa.
22 Jedno jest, dla czegom to mówił: że tak doskonałego, jako i niezbożnego on niszczy;
Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’
23 Jeźli biczem nagle zabija, z pokuszenia niewinnych naśmiewa się;
Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi, Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.
24 Ziemia podana bywa w ręce niezbożnika, oblicze sędziów jej zakrywa. A jeźliż nie on, któż tedy inny jest, co to czyni?
Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo. Ngati si Iyeyo, nanga ndani?
25 Ale dni moje prędsze były niż poseł; uciekły, a nie widziały nic dobrego.
“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro; masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.
26 Przeminęły jako prędkie łodzie, jako orzeł lecący do żeru.
Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja, ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.
27 Jeźli rzekę: Zapomnę narzekania mego, zaniecham gniewu swego, a posilę się:
Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga, ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’
28 Tedy się lękam wszystkich boleści moich, widząc, że mię z nich nie wypuścisz.
ndikuopabe mavuto anga onse, popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.
29 Jeźlim ja niezbożny, przeczże próżno pracuję?
Popeza ndapezeka kale wolakwa ndivutikirenji popanda phindu?
30 A choćbym się umywał wodami śnieżnemi, i oczyściłbym mydłem ręce moje:
Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,
31 Wszakże w dole zanurzysz mię, i brzydzić się mną będą szaty moje.
mutha kundiponyabe pa dzala, kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.
32 Albowiem on nie jest człowiekiem jako ja, abym mu śmiał odpowiedzieć, albo żebym z nim miał iść w prawo.
“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha, sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.
33 Bo nie masz między nami rozjemcy, któryby mógł rozwieść sprawę naszę.
Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu, kuti atibweretse ife tonse pamodzi,
34 Niech tylko zdejmie zemnie rózgę swoję, a strach jego niech mię nie straszy;
munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!
35 Tedy będę mówił, a nie będę się go bał; bom ja nie jest taki sam u siebie.
Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo, koma monga zililimu, sindingathe.

< Hioba 9 >