< Hioba 8 >

1 I odpowiedział Bildad Suhytczyk, a rzekł:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Pokądże rzeczy takowe mówić będziesz? a pokąd będą słowa ust twoich jako wiatr gwałtowny?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Izażby miał Bóg sąd podwrócić? a Wszechmocny miałby sprawiedliwość wynicować?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Że synowie twoi zgrzeszyli przeciw niemu, przetoż ich puścił w rękę nieprawości ich.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Jeźli się ty wczas nawrócisz do Boga, a będziesz się modlił Wszechmocnemu;
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 Jeźli będziesz czystym i szczerym; tedyć pewnie ocuci dla ciebie, i spokojne uczyni mieszkanie sprawiedliwości twojej.
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 A choć początek twój mały będzie, jednak ostatek twój bardzo się rozmnoży.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 Bo spytaj się proszę wieku starego, a nagotuj się ku wyszpiegowaniu ojców ich.
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 (Gdyż wczorajszymi jesteśmy, a nic nie wiemy, ponieważ jako cień są dni nasze na ziemi.)
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 Oni cię nauczą i powiedząć, i z serca swego wypuszczą słowa.
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Azaż urośnie sitowie bez wilgotności? Izali urośnie rogoża bez wody?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Owszem jeszcze w zieloności swojej, niż bywa podcięta, prędzej niż inna trawa usycha.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Takieć są drogi wszystkich, którzy zapominają Boga; i tak nadzieja obłudnika zginie.
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 Podcięta bywa nadzieja jego, a jako dom pająka ufanie jego.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Spolężeli na domu swoim, nie ostoi się; wesprzeli się na nim, nie zadzierzy się.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Zieleni się na słońcu, i w ogrodzie jego świeża latorośl jego wyrasta.
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 Nad ródłem splątają się korzenie jego, i na miejscu kamienistem rozkłada się.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Ale gdy go wytną z miejsca jego, tedy się go miejsce zaprze, mówiąc: Niewidziałem cię.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Toć to jest wesele drogi jego, a inny z ziemi wyrośnie.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Oto Bóg nie odrzuci człowieka szczerego, ale złośnikom nie poda ręki.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Aż się napełnią śmiechem usta twe, a wargi twoje wykrzykaniem.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 Gdyż, którzy cię mają w nienawiści, obleczeni będą wstydem, a przybytku niepobożnych nie będzie.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Hioba 8 >