< Jeremiasza 48 >

1 Przeciwko Moabowi. Tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski: Biada miastu Nebo, bo spustoszone będzie; pohańbione i wzięte będzie Karyjataim; zawstydzone będzie miasto na miejscu wysokiem, i bać się będzie.
Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
2 Nie będzie się więcej chlubił Moab z Hesebonu; myślą złe przeciwko niemu, mówiąc: Pójdźcie, a wytraćmy ich z narodu. I ty, Madmenie! wykorzeniony będziesz, miecz pójdzie za tobą.
Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
3 Głos krzyku z Choronaim: O spustoszenie i zburzenie wielkie!
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
4 Starty będzie Moab, słyszany będzie krzyk maluczkich jego,
Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
5 Przeto, że na drodze Luchytskiej będzie ustawiczny płacz, a którędy zstępują do Choronaim, nieprzyjaciele krzyk zburzenia słyszeć będą,
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
6 Mówiących: Uciekajcie, wybawcie duszę swoję, a stańcie się jako wrzos na puszczy.
Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
7 Bo dlatego, że masz nadzieję w dostatku twoim, i w skarbach twoich, będziesz też wzięte, i Chamos pójdzie w pojmanie, kapłani jego, także i książęta jego.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
8 Bo burzyciel przyjdzie na każde miasto, a żadne miasto nie ujdzie; zginie i dolina, i równiny spustoszone będą, jako mówi Pan.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
9 Dajcie skrzydła Moabowi, niech prędko uleci; bo miasta jego przyjdą w spustoszenie, tak, że nie będzie w nich obywatela.
Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
10 Przeklęty, kto zdradliwie czyni sprawę Pańską; przeklęty także, kto hamuje miecz swój ode krwi.
“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
11 Miałci Moab pokój od dzieciństwa swego, i usadził się na drożdżach swoich, ani był przelewany z naczynia w naczynie, to jest, w pojmanie nie chodził, dla czego został w nim smak jego, a woń jego nie zmieniła się.
“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
12 Przetoż oto dni idą, mówi Pan, że poślę nań tych, którzy wtargnienia czynią, a pojmają go, i naczynia jego wypróżnią, a łagwie jego potłuką.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 I zawstydzony będzie Moab od Chamosa, jako zawstydzony jest dom Izraelski od Betel, nadziei swojej.
Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
14 Jakoż mówicie: Mocniśmy, a mężowie duży do boju?
“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Zburzony będzie Moab, i z miast swoich wynijdzie, a wyborni młodzieńcy jego pójdą na zabicie, mówi król, Pan zastępów imię jego.
Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Blisko jest zginienie Moabowe, i przyjdzie; a nieszczęście jego prędko się pospieszy.
Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
17 Użalcie się go wszyscy, którzy mieszkacie około niego, i wszyscy, którzy znacie imię jego, mówcie: Jakoż się złamała laska mocy, i kij ozdobny?
Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
18 Zstąp z sławy, a siądź w pragnieniu, obywatelko, córko Dybońska! bo zburzyciel Moabu przyciągnie przeciwko tobie, rozrzuci twierdze twoje.
“Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Stań na drodze a przypatrz się pilnie, obywatelko Aroer! pytaj tego, który ucieka, i tej, która uchodzi, mówiąc: Co się dzieje?
Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
20 Zawstydzony jest Moab, bo jest potarty; narzekajcie a wołajcie, opowiadajcie w Arnon, że pustoszą Moaba.
Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
21 Bo sąd przyszedł na ziemię tej równiny, na Holon, i na Jassa, i na Mefaat,
Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22 I na Dybon, i na Nebo, i na Bet Dyblataim,
Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23 I na Kiryjataim, i na Betgamul, i Betmehon.
Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24 I na Karyjot, i na Bocrę, i na wszystkie miasta ziemi Moabskiej, dalekie i bliskie.
Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 Odcięty będzie róg Moabski, i ramię jego będzie starte, mówi Pan.
Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
26 Opójcie go, ponieważ się przeciw Panu podniósł; niech się wala Moab w blwocinach swoich, niech będzie i on na pośmiech.
“Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 Bo azaż w pośmiewisku nie był u ciebie Izrael? Izali go między złodziejami zastano? że, ilekroć mówisz o nim, wyskakujesz.
Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 Opuszczajcie miasta a mieszkajcie na skale, obywatele Moabscy! a bądźcie jako gołębica, która ściele gniazdo swoje na kraju dziury.
Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
29 Słyszeliśmy o pysze Moabowej, że jest bardzo pyszny; o wysokomyślności jego, i o hardości jego, i o nadętości jego, i o wyniosłości serca jego.
“Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
30 Znamci Ja, mówi Pan, zagniewanie jego; lecz nie ma siły; kłamstwa jego nie dowiodą tego.
Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 Dlatego nad Moabczykami narzekam, a nade wszystkim Moabem wołam, a dla obywateli Kircheres wzdycha serce moje.
Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 Bardziej niż płakano Jazerczyków, płaczę nad tobą, o winna macico Sabama! Latorośli twoje dostaną się za morze, aż do morza Jazer dosięgną; na letnie owoce twoje, i na zbieranie wina twego burzyciel przypadnie.
Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 I ustanie wesele i radość nad polem urodzajnem w ziemi Moabskiej, a winu z prasy wstręt uczynię; nie będą go tłoczyć z wykrzykaniem, a wykrzykanie nie będzie wykrzykaniem.
Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
34 Bardziej krzyczeć będą niż Hesebończycy; aż do Eleale, aż do Jazy wydadzą głos swój, od Zoar aż do Choronaim, jako jałowica trzecioletnia; bo też i wody Nimrym zniszczeją.
“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 I uczynię, mówi Pan, że ustanie w Moabie ofiarujący na wyżynach, i kadzący bogom swoim.
Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
36 Przetoż serce moje nad Moabem jako piszczałki piszczeć będzie; także nad obywatelami w Kircheres serce moje jako piszczałki piszczeć będzie, i dlatego, że i zboże zgromadzone wniwecz się obróci.
“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 Bo na każdej głowie będzie łysina, i każda broda ogolona będzie; na wszystkich rękach będą szramy, a na biodrach wór.
Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 Po wszystkich dachach Moabskich i po ulicach jego, wszędy nic nie będzie, tylko narzekanie; bom skruszył Moaba jako naczynie nieużyteczne, mówi Pan.
Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
39 Narzekać będą, mówiąc: Jakoć jest starty! Jako tył podał Moab z hańbą! i jest Moab pośmiewiskiem, i postrachem wszystkim, którzy są około niego.
“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
40 Bo tak mówi Pan: Oto nieprzyjaciel jako orzeł przyleci, a rozciągnie skrzydła swe na Moaba.
Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 Karyjot wzięte będzie, i zamki wzięte będą, a serce mocarzów Moabskich dnia onego będzie jako serce niewiasty bolejącej.
Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 I wygładzony będzie Moab z ludu; bo się przeciwko Panu podnosił.
Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Strach i dół, i sidło nad tobą, o obywatelu Moabski! mówi Pan.
Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
44 Kto uciecze przed strachem, wpadnie w dół; a kto wynijdzie z dołu, sidłem ułapiony będzie; bo przywiodę nań, to jest na Moaba, rok nawiedzienia jego, mówi Pan.
“Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
45 W cieniu Hesebon stawali ci, którzy uciekali przed gwałtem; ale ogień wynijdzie z Hesebonu, i płomień z pośrodku Sehonu, i pożre kąt Moabski, i wierzch głowy tych, którzy go burzą.
“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
46 Biada tobie, Moabie! zaginieć lud Chamosowy; bo synowie twoi zabrani będą w niewolę, i córki twoje do więzienia.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
47 Wszakże zasię przywrócę więźniów Moabskich w ostateczne dni, mówi Pan. Aż dotąd sąd o Moabie.
“Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

< Jeremiasza 48 >