< Jeremiasza 32 >

1 Słowo, które się stało do Jeremijasza od Pana roku dziesiątego Sedekijasza, króla Judzkiego, który jest rok ośmnasty Nabuchodonozora.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya mʼchaka chakhumi cha Zedekiya mfumu ya Yuda, chimene chinalinso chaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara.
2 (A wtenczas wojsko króla Babilońskiego obległo było Jeruzalem, a Jeremijasz prorok zamknięty był w sieni ciemnicy, która była w domu króla Judzkiego.
Pa nthawi imeneyi nʼkuti ankhondo a mfumu ya ku Babuloni atazinga Yerusalemu, ndipo mneneri Yeremiya ndiye anamutsekera mʼbwalo la alonda mʼnyumba yaufumu ya ku Yuda.
3 Bo go był dał wsadzić Sedekijasz, król Judzki, mówiąc: Czemu ty prorokujesz, mówiąc: Tak mówi Pan: Oto Ja to miasto podam w rękę króla Babiolońskiego, i weźmie je?
Tsono Zedekiya mfumu ya Yuda nʼkuti itamutsekera mʼmenemo, ndipo inati, “Nʼchifukwa chiyani ukulosera motero? Iwe ukunena kuti, ‘Yehova akuti: Ndidzapereka mzinda uno kwa mfumu ya ku Babuloni, ndipo idzawulanda.
4 Sedekijasz także król Judzki nie ujdzie ręki Chaldejczyków; ale zapewne wydany będzie w rękę króla Babilońskiego, i będą mówiły usta jego z usty jego, a oczy jego oczy jego ogladają.
Zedekiya mfumu ya Yuda sidzapulumuka mʼmanja mwa Ababuloni, koma idzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni. Adzayankhula naye ndi kuonana naye maso ndi maso.
5 I zawiedzie Sedekijasza do Babilonu, aby tam był, aż go nawiedzę, mówi Pan; ponieważ walczycie z Chaldejczykami, nie poszczęści się wam.)
Zedekiya adzatengedwa kupita naye ku Babuloni, kumene adzakhale mpaka nditamukhawulitsa, akutero Yehova. Ngakhale iye adzamenyane ndi Babuloni, koma sadzapambana.’”
6 Tedy rzekł Jeremijasz: Stało się słowo Pańskie do mnie, mówiąc:
Yeremiya anati, “Yehova wandiwuza kuti:
7 Oto Chanameel, syn Salluma, stryja twego, przyjdzie do ciebie, mówiąc: Kup sobie rolę moję, która jest w Anatot; bo tobie należy prawem bliskości, abyś ją kupił.
Taonani, Hanameli mwana wa Salumu, amalume ako akubwera ndipo adzakuwuza kuti, ‘Gula munda wanga wa ku Anatoti, chifukwa iwe ndiwe mʼbale wanga ndipo ndiwe woyenera kuwuwombola.’”
8 A gdy przyszedł do mnie Chanameel, syn stryja mego, według słowa Pańskiego do sieni ciemnicy, i rzekł do mnie: Proszę, kup rolę moję, która jest w Anatot, które jest w ziemi Benjaminowej, bo tobie należy prawem dziedzicznem, i bliskościąć przypada, kupże ją sobie: tedy zrozumiawszy, że to było słowo Pańskie,
Ndipo monga momwe Yehova ananenera, Hanameli, msuweni wanga anabweradi ku bwalo la alonda ndipo anati, “Gula munda wanga wa ku Anatoti mʼdziko la Benjamini. Popeza ndiwe woyenera kuwugula ndi kukhala wako, gula munda umenewu kuti ukhale wako.” “Ine ndinadziwa kuti amenewa anali mawu a Yehova aja;
9 Kupiłem od Chanameela, syna stryja swego onę rolę, która jest w Anatot, i odważyłem mu pieniędzy, siedmnaście syklów srebra;
choncho ndinagula munda wa ku Anatoti kwa Hanameli msuweni wanga, ndipo ndinamupatsa masekeli asiliva 17.
10 A uczyniwszy zapis zapieczętowałem i oświadczyłem świadkami, odważywszy pieniądze na wadze.
Ndinasayina panganolo ndikulimata pamaso pa mboni, kenaka ndinayeza ndalama zasilivazo pa sikelo.”
11 Potemem wziął według przykazania i prawa zapis kupna zapieczętowany i otwarty;
Pambuyo pake ndinatenga makalata anga a pangano, imodzi yomatidwa mʼmene munali malamulo onse a panganolo ndi ina yosamatidwa.
12 I oddałem on zapis kupna Baruchowi, synowi Neryjasza, syna Maasejaszowego, przed oczyma Chanameela, stryja swego, i przed oczyma świadków, którzy się podpisali w onym zapisie kupna, przed oczyma wszystkich Żydów, którzy byli usiedli w sieni ciemnicy;
Ndinapereka makalatawo kwa Baruki mwana wa Neriya, mdzukulu wa Maseya pamaso pa Hanameli msuweni wanga, pamaso pa mboni zimene zinasayina panganoli ndiponso pamaso pa Ayuda onse okhala mʼbwalo la alonda.
13 I rozkazałem Baruchowi przed oczyma ich, mówiąc:
“Ndinamulangiza Baruki pamaso pa onsewo kuti,
14 Tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski: Weźmij te zapisy, ten zapis tego kupna, jako zapieczętowany, tak i ten zapis otworzony, a włóż je w naczynie gliniane, aby trwały przez wiele lat;
‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Tenga makalata awa a umboni wapangano, iyi yokhala ndi chizindikiro ndi yopanda chizindikiro, uwasunge mʼmbiya kuti akhale nthawi yayitali.
15 Bo tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski: Jeszcze będą kupowane domy, i role, i winnice w tej ziemi.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Anthu adzagulanso nyumba, minda ndi mitengo yamphesa mʼdziko lino.’”
16 Potem modliłem się Panu, kiedym oddał on zapis kupna Baruchowi, synowi Neryjaszowemu, mówiąc:
Nditamupatsa makalata a panganowa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova:
17 Ach panujący Panie! otoś ty uczynił niebo i ziemię mocą swoją wielką i ramianiem twoim wyciągnionem, nie jestci skryta przed tobą żadna rzecz;
“Aa, inu Ambuye Yehova, munalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Munazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo palibe chokulakani.
18 Czynisz miłosierdzie nad tysiącami, i oddajesz nieprawość ojcowską do łona synów ich po nich; Bóg wielki mocny, Pan zastępów imię twoje;
Mumaonetsa chikondi chanu kwa anthu osawerengeka koma mumalanga ana chifukwa cha machimo a makolo awo. Inu ndinu Mulungu Wamkulu ndi Wamphamvu. Dzina lanu ndinu Yehova Wamphamvuzonse.
19 Wielki w radzie i możny w sprawie, ponieważ oczy twoje otworzone są na wszystkie drogi synów ludzkich, abyś oddał każdemu według dróg jego, i według owoców spraw jego;
Zolinga zanu ndi zazikulu ndipo zochita zanu ndi zamphamvu. Maso anu amaona zonse zimene anthu amachita. Mumapereka mphotho kwa munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndi ntchito zake.
20 Któryś uczynił znaki i cuda na ziemi Egipskiej aż do dnia tego, i w Izraelu, i między innymi ludźmi, i uczyniłeś sobie imię, jako się to dziś okazuje.
Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ku Igupto, ndipo mwakhala mukuzichita mpaka lero, pakati pa Aisraeli ndiponso pakati pa anthu onse. Choncho mwadzitchukitsa mpaka lero lino.
21 Boś wywiódł lud twój Izraeski z ziemi Egipskiej w znakach i w cudach, i w ręce mocnej, i w ramieniu wyciągnionem i w strachu wielkim;
Munatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu pochita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene zinaopseza adani anu.
22 A podałeś im tę ziemię, o którąś przysiągł ojcom ich, żeś im miał dać ziemię opływającą mlekiem i miodem.
Munawapatsa dziko lino limene munalonjeza mwalumbiro kulipereka kwa makolo awo, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
23 Ale że wszedłszy do niej, a posiadłszy ją, nie usłuchali głosu twojego, i w zakonie twoim nie chodzili, wszystkiego, coś im rozkazał czynić, nie czynili; przetoż sprawiłeś to, aby nań przyszło to wszystko złe.
Iwo analowa nʼkulitenga kukhala lawo, koma sanamvere Inu kapena kutsatira lamulo lanu; ndipo sanachite zomwe munawalamula. Choncho inu mwawagwetsera masautso onsewa.”
24 Oto strzelbę zatoczono przeciwko miastu, aby je wzięto, a miasto podane jest w ręce Chaldejczyków walczących przeciw niemu przez miecz, i głód, o mór; a tak cośkolwiek rzekł, dzieje się, to sam widzisz.
“Onani momwe adani azingira ndi mitumbira yankhondo mzindawu kuti awulande ndipo akuwuthira nkhondo. Chifukwa cha lupanga, njala ndi mliri. Mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni anthu atafowoka ndi nkhondo, njala ndi mliri. Zimene munkanena zija zachitikadi monga mukuzionera tsopano.
25 A ty przecie mówisz do mnie, panujący Panie: Kup sobie tę rolę za pieniądze, a oświadcz to świadkami, choć już to miasto podane jest w ręcę Chaldejczyków.
Ngakhale mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni, komabe Inu Ambuye Yehova, munandiwuza kuti, ‘Gula munda ndi siliva ndipo upereke ndalamazo pali mboni.’”
26 I stało się słowo Pańskie do Jeremijasza, mówiąc:
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti,
27 Otom Ja Pan, Bóg wszelkiego ciała; izaliż przedemną może być skryta która rzecz?
“Taonani, Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse. Kodi chilipo chinthu choti Ine nʼkundikanika?
28 Przetoż tak mówi Pan: Oto Ja daję to miasto w rękę Chaldejczyków, i w rękę Nabuchodonozora, króla Babilońskiego, i weźmie je.
Nʼchifukwa chake ine Yehova ndikuti: Ndidzawupereka mzinda uno kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulanda.
29 A wszedłszy Chaldejczycy, którzy walczą przeciwko temu miastu, zapalą to miasto ogniem, i spalą je i te domy, na których dachach kadzili Baalowi, a sprawowali ofiary mokre bogom cudzym, aby mię wzruszali do gniewu.
Ndipo Ababuloni amene akuwuthira nkhondo mzinda uno adzalowa ndi kuwutentha; adzatentha ndi kugwetsa nyumba zimene pa denga pake anthu ankandipsetsa mtima pofukiza lubani kwa Baala ndi popereka chopereka cha chakumwa kwa milungu ina.
30 Bo synowie Izraelscy i synowie Judzcy od dzieciństwa swego to tylko czynią, co jest złego przed oczyma mojemi; synowie, mówię, Izraelscy tylko mię draźnili sprawą rąk swoich, mówi Pan.
“Aisraeli ndi Ayuda akhala akuchita zoyipa zokhazokha pamaso panga kuyambira ubwana wawo. Kunena zoona Aisraeli akumandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa, akutero Yehova.
31 Zaiste na zapalczywość moję, i na gniew mój robi sobie to miasto ode dnia, którego je zbudowali, aż do dnia tego, tak, że mi przyjdzie oddalić od oblicza mego;
Kuyambira tsiku limene mzindawu unamangidwa mpaka lero, wakhala ukuwutsa mkwiyo wanga ndi ukali wanga. Nʼchifukwa chake ndiyenera kuwuchotsa pamaso panga.
32 A to dla wszelkiej złości synów Izraelskich i synów Judzkich, którą popełniali, pobudzając mię do gniewu, sami, królowie ich, książęta ich, kapłani ich i prorocy ich, jako mężowie Judzcy, tak obywatele Jeruzalemscy.
Aisraeli ndi Ayuda, anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, mafumu awo, nduna zawo, ansembe ndi aneneri awo anandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa.
33 Obracając się do mnie tyłem a nie twarzą; a gdy ich nauczam rano wstawając i nauczając, wszakże nie słuchają, aby przyjęli naukę.
Anandifulatira ndipo ngakhale ndinakhala ndikuwaphunzitsa kawirikawiri, sanamve kapena kuphunzirapo kanthu.
34 Nadto nastawiali obrzydliwości swych w tym domu, który nazwany jest od imienia mego, aby go splugawili.
Iwo anayika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi dzina langa ndipo anayipitsa.
35 Nabudowali, mówię, wyżyn Baalowi, które są w dolinie Ben Hennon, aby przenaszali przez ognień synów swoich i córki swoje Molochowi, chociażem im tego nie rozkazał, ani to wstąpiło na serce moje, aby kiedy czynić mieli tę obrzydliwość, a do grzech u Judą przywodzić.
Anamanga malo opembedzerapo Baala mʼChigwa cha Hinomu kuti aziperekapo ana awo aamuna ndi aakazi ngati nsembe kwa Moleki. Ine sindinawalamulire kutero, ndipo sindinaganizepo nʼkomwe kuti iwo angachite chinthu chonyansa chotero, ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda.
36 A teraz dlatego tak mówi Pan, Bóg Izraelski, o tem mieście, o którem wy powiadacie: Podane jest w rękę króla Babilońskiego przez miecz, i głód, i mór:
“Anthu ponena za mzindawu akuti udzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni mwa nkhondo, njala ndi mliri, koma Yehova Mulungu wa Israeli akuti,
37 Oto Ja zgromadzę ich ze wszystkich ziem, do którychem ich wygnał w popędliwości mojej i w gniewie moim, i w zapalczywości wielkiej, i przywiodę ich zaś na to miejsce, i uczynie, aby bezpiecznie mieszkali;
Ine ndidzawasonkhanitsadi anthuwa kuchokera ku mayiko onse kumene ndinawapirikitsira ndili wokwiya ndi waukali kwambiri. Ndidzabwera nawo ku malo ano ndipo ndidzawalola kukhala mwamtendere.
38 I będą ludem moim, a Ja będę Bogiem ich.
Iwo adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
39 I dam im serce jedno, i drogę jednę, aby się mnie bali po wszystkie dni, tak, aby się im dobrze działo, i synom ich po nich;
Ndidzawapatsa mtima umodzi ndi khalidwe limodzi kotero kuti azidzandiopa nthawi zonse ndipo iwo pamodzi ndi zidzukulu zawo zinthu zidzawayendera bwino.
40 I uczynię z nimi przymierze wieczne, że się nie odwrócę od nich, abym im nie miał dobrze czynić; nadto bojaźń moję dam do serca ich, aby nie odstępowali odemnie.
Ndidzachita nawo pangano losatha: sindidzaleka kuwachitira zabwino, ndipo ndidzawapatsa mtima woti azidzandiopa, kuti asadzandisiyenso.
41 I będę się weselił z nich, dobrze im czyniąc, gdyż ich wszczepię w tej ziemi warownie, ze wszystkiego serca mego i ze wszystkiej duszy mojej.
Ndidzakondwera powachitira zabwino, ndipo ndidzawakhazikitsa ndithu mʼdziko lino ndi mtima wanga wonse ndi moyo wanga wonse.
42 Bo tak mówi Pan: Jakom przywiódł na ten lud to wszystko wielkie złe, tak przywiodę na nich to wszystko dobre, o któremem z nimi mówił.
“Yehova akuti: Monga momwe ndinagwetsera masautso aakulu onsewa pa anthuwa, momwemonso ndidzawapatsa zinthu zonse zabwino zimene ndinawalonjeza.
43 Tedy będą kupować rolę w tej ziemi, o której wy powiadacie: Spustoszona jest tak, że w niej niemasz ani człowieka ani bydlęcia, podana jest w rękę Chaldejczyków.
Adzagulanso minda mʼdziko muno, limene inu mukuti, ‘Ndi dziko losiyidwa, lopanda anthu kapena nyama, pakuti linaperekedwa kwa Ababuloni.’
44 Rolę za pieniądze kupować będą, i zapisem warować, i pieczętować, i świadkami oświadczać w ziemi Benjaminowej, i około Jeruzalemu, i w miastach Judzkich, jako w miastach na górach tak w miastach na równinach, i w miastach na południe, gdy zaś przywrócę pojmanych ich, mówi Pan.
Adzagula minda ndi ndalama zasiliva, ndipo achita pangano, ndi kumata pamaso pa mboni. Izi zidzachitika mʼdziko la Benjamini, ku malo ozungulira Yerusalemu, mʼmizinda ya Yuda, mʼmizinda ya ku mapiri, mʼmizinda ya kuchigwa ndi yakummwera ku Negevi. Zoona, ndidzabwezera ufulu wawo, akutero Yehova.”

< Jeremiasza 32 >