< Jeremiasza 30 >

1 Słowo, które się stało do Jeremijasza od Pana, mówiąc:
Yehova anawuza Yeremiya kuti,
2 Tak powiada Pan, Bóg Izraelski, mówiąc: Napisz sobie wszystkie słowa, którem mówił do ciebie, na księgach.
“Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza.
3 Albowiem oto dni idą, mówi Pan, a przywrócę więźniów ludu swego Izraelskiego i Judzkiego, mówi Pan, i przyprowadzę ich do ziemi, którąm był dał ojcom ich, i posiędą ją.
Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”
4 A teć są słowa, które mówił Pan o Izraelu i o Judzie;
Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda:
5 Tak zaiste mówi Pan: Słyszeliśmy głos strachu i lękania, i że niemasz pokoju.
“Yehova akuti: “Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa, ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.
6 Pytajcież się teraz, a obaczcie, jeźli rodzi mężczyzna; przeczże tedy widzę, że każdy mąż rękami swemi trzyma się za biodra swe jako rodząca, i że się obróciły wszystkich oblicza w bladość?
Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti: Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira? Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?
7 Biada! bo wielki jest ten dzień, tak, że mu nie było podobnego; ale jakiżkolwiek jest czas utrapienia Jakóbowego, przecie z niego wybawiony będzie.
Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri! Sipadzakhala lina lofanana nalo. Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo, koma adzapulumuka ku masautsowo.”
8 Stanie się bowiem dnia onego, mówi Pan zastępów, iż skruszę jarzmo jego z szyi twojej, a związki twoje potargam, i nie będą go więcej cudzoziemcy w niewolę podbijać;
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo, ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo ndipo ndidzadula zingwe zowamanga; Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.
9 Ale służyć będą Panu, Bogu swemu, i Dawidowi, królowi swemu, którego im wzbudzę.
Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo ndiponso Davide mfumu yawo, amene ndidzawasankhira.
10 Przetoż nie bój się ty, sługo mój Jakóbie! mówi Pan, ani się strachaj o Izraelu! bo oto Ja cię wybawię z daleka, i nasienie twoje z ziemi pojmania ich. I wróci się Jakób, aby odpoczywał i pokój miał, a nie będzie, ktoby go ustraszył;
“‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo; usade nkhawa, iwe Israeli,’ akutero Yehova. ‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali, zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere, ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.
11 Bom Ja z tobą, mówi Pan, abym cię wybawił. Ponieważ uczynię koniec wszystkim narodom, między które cię rozproszę, wszakże tobie nie uczynię końca, ale cię miernie karać będę, a cale cię bez karania nie zaniecham.
Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’ akutero Yehova. ‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu kumene ndinakubalalitsirani, koma inu sindidzakuwonongani kotheratu. Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa. Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’”
12 Tak zaiste mówi Pan: Ciężkie bardzo będzie skruszenie twoje, nader bolesna rana twoja.
Yehova akuti, “Chilonda chanu nʼchosachizika, bala lanu ndi lonyeka.
13 Nie będzie, ktoby sądził sprawę twoję ku uleczeniu; lekarstwa ku uleczeniu mieć nie będziesz.
Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu, palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira, palibe mankhwala ochiritsa inu.
14 Wszyscy miłośnicy twoi zapomną cię, ani cię nawiedzą, gdy cię zranię raną nieprzyjacielską, i okrutnem karaniem, dla wielkości nieprawości twojej i niezliczonych grzechów twoich.
Abwenzi anu onse akuyiwalani; sasamalanso za inu. Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira. Ndipo ndakulangani mwa nkhanza, chifukwa machimo anu ndi ambiri, ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.
15 Przeczże wołasz nad skruszeniem swem i ciężką boleścią swoją? Dla wielkości nieprawości twojej, i dla niezliczonych grzechów twoich uczyniłem ci to.
Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu? Bala lanu silingapole ayi. Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.
16 A wszakże wszyscy, którzy cię pożerają, pożarci będą; a wszyscy, którzy cię ciemiężą, wszyscy, mówię, w niewolę pójdą; a którzy cię plundrują, splundrowani będą; a wszystkich, którzy cię łupią, podam na łup.
“Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa; adani anu onse adzapita ku ukapolo. Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso; onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.
17 Tedyć zdrowie przywrócę, i od ran twoich uleczę cię, mówi Pan, przeto, że wygnaną nazwali cię (mówiąc: ) Tać jest Syon, niemasz nikogo, ktoby ją nawiedził.
Ndidzachiza matenda anu ndi kupoletsa zilonda zanu, akutero Yehova, ‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika. Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’”
18 Tak mówi Pan: Oto Ja przywrócę pojmanych z namiotów Jakóbowych, a nad przybytkami jego zmiłuję się; i będzie zaś zbudowane miasto na pagórku swoim, a pałac według porządku swego wystawiony będzie.
Yehova akuti, “Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo; mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake, nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.
19 I wynijdzie od nich dziękczynienie, i głos weselących się; bo ich rozmnożę, a nie ubędzie ich, i uwielbię ich, a nie będą poniżeni.
Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo. Ndidzawachulukitsa, ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika; ndidzawapatsa ulemerero, ndipo sadzanyozedwanso.
20 I będą synowie jego, jako i przedtem, a zgromadzenie jego przedemną utwierdzone będzie; ale nawiedzę wszystkich, którzy ich trapią.
Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale, ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga; ndidzalanga onse owazunza.
21 I powstanie z niego najzacniejszy jego, a panujący nad nim z pośrodku jego wynijdzie, któremu się rozkażę przybliżyć, aby przystąpił przed mię; bo któż jest ten, coby ręczył za się, że przystąpi przed mię? mówi Pan.
Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo. Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo. Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira. Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane popanda kuyitanidwa?” akutero Yehova.
22 I będziecie ludem moim, a Ja będę Bogiem waszym.
“Choncho inu mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”
23 Oto wicher Pański z popędliwością wynijdzie, wicher trwający nad głową niezbożników zostanie.
Taonani ukali wa Yehova wowomba ngati mphepo ya mkuntho. Mphepo ya namondwe ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.
24 Nie odwróci się zapalczywość gniewu Pańskiego, póki nie uczyni tego, a póki nie wykona umysłu serca swego; w ostatnie dni zrozumiecie to.
Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka mpaka atakwaniritsa zolinga za mu mtima mwake. Mudzamvetsa zimenezi masiku akubwerawo.

< Jeremiasza 30 >