< Jeremiasza 19 >

1 Tak mówi Pan: Idź, a kup dzban gliniany od garncarza, a wziąwszy niektórych z starszych ludu i z starszych kapłanów;
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukagule mʼphika wadothi kwa munthu wowumba. Utenge akuluakulu ena a anthuwa ndi ansembe
2 Wnijdź do doliny syna Hennomowego, która jest u wrót bramy wschodniej, a tam opowiadaj słowa, które do ciebie mówić będę.
ndipo mupite ku Chigwa cha Hinomu chimene chili pafupi ndi pa chipata cha mapale. Pamenepo ukalengeze mawu amene ndikakuwuze.
3 A rzecz: Słuchajcie słowa Pańskiego, królowie Judzcy i obywatele Jeruzalemscy! Tak mówi pan zastępów, Bóg Izraelski: Oto Ja przywiodę złe na to miejsce, o którem ktokolwiek usłyszy, zabrzmi mu w uszach jego.
Ukanene kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu a ku Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti: Tamverani! Ine ndibweretsa mavuto pa malo pano mwakuti aliyense amene adzamve adzadzidzimuka.
4 Przeto, że mię opuścili, a splugawili to miejsce, kadząc na niem bogom cudzym, których nie znali oni i ojcowie ich, i królowie Judzcy, i napełnili to miejsce krwią niewinnych;
Pakuti anthu andikana Ine ndipo ayipitsa malo ano. Afukiza lubani pa malo ano kwa milungu imene iwo ngakhale makolo awo ngakhalenso mafumu a ku Yuda sanayidziwe. Iwo adzaza malowa ndi magazi a anthu osalakwa.
5 I pobudowali wyżyny Baalowi, aby palili synów swych ogniem na całopalenie Baalowi, czegom nie rozkazał, anim oto mówił, ani to wstąpiło na serce moje:
Amanga nsanja zopembedzerapo Baala, kuperekapo ana awo kuti akhale nsembe zopsereza kwa Baala, chinthu chimene Ine sindinalamule kapena kuchiyankhula, ngakhalenso kuchiganizira.
6 Dlatego oto dni idą, mówi Pan, w których nie będzie nazywane więcej to miejsce Tofet, ani doliną syna Hennomowego, ale doliną mordu.
Nʼchifukwa chake taonani, masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzatchulanso malo ano kuti Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma Chophera anthu.
7 Bo wniwecz obrócę radę Judzką i Jeruzalemską na tem miejscu, a sprawię, że oni upadną od miecza przed twarzą nieprzyjaciół swoich, i od ręki szukających duszy ich; i dam trupy ich na pokarm ptastwu niebieskiemu, i zwierzowi ziemskiemu;
“‘Pamalo pano ndidzasokoneza maganizo a anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Ndidzachititsa kuti adani awo awaphe ku nkhondo. Ndidzawakanthitsa kwa anthu amene akuwazonda. Mitembo yawo ndidzayipereka kwa mbalame za mlengalenga ndi zirombo za kutchire kuti ikhale chakudya chawo.
8 Podam także to miasto na spustoszenie i na świstanie; każdy idący mimo nie zdumieje się, a świstać będzie nad wszystkiemi plagami jego.
Mzinda uno ndidzawusakaza ndi kuwusandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyansa. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
9 I sprawię to, że będą jeść ciała synów swoich, i ciała córek swoich, a każdy z nich ciało bliźniego swego jeść będzie w oblężeniu i w uciśnieniu, którem ich ucisną nieprzyjaciele ich, i ci, którzy szukają duszy ich.
Adani awo adzawuzinga mzindawo kufuna kuwapha motero kuti anthu a mʼkatimo adzafika pomadyana wina ndi mnzake. Adzadya ana awo aamuna ndi ana awo aakazi.’
10 Potem stłucz ten dzban przed oczyma mężów, którzy pójdą z tobą,
“Tsono iwe udzaphwanye mtsukowo anthu amene udzapite nawowo akuona,
11 A rzecz do nich: Tak mówi Pan zastępów: Tak stłukę ten lud, i to miasto, jako gdy kto tłucze naczynie garncarskie, które więcej naprawione być nie może: a w Tofet pogrzebywać będą, iż miejsca inszego nie będzie ku pogrzebowi.
ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika.
12 Tak uczynię temu miejscu, mówi Pan, i obywatelom jego, i postąpię sobie z tem miastem, tak jako z Tofet.
Umu ndi mmene ndidzachitire ndi malo ano pamodzi ndi anthu okhalamo, akutero Yehova. Ndidzasandutsa mzindawu kukhala ngati Tofeti.
13 Bo będą domy Jeruzalemskie i domy królów Judzkich, jako to miejsce Tofet, nieczyste ze wszystkiemi domami temi, na których dachach kadzili wszystkiemu wojsku niebieskiemu, i sprawowali ofiary mokre bogom cudzym.
Nyumba za mu Yerusalemu ndi za mafumu a ku Yuda ndidzazisandutsa ngati za ku Tofeti chifukwa ndi nyumba zimene pa madenga ake ankafukiza lubani kwa zolengedwa zamlengalenga ndi kuthira nsembe zachakumwa kwa milungu ina.’”
14 Tedy wróciwszy się Jeremijasz z Tofet, gdzie go był Pan posłał, aby tam prorokował, stanął w sieni domu Pańskiego, i rzekł do wszystkiego ludu:
Kenaka Yeremiya anabwerako ku Tofeti, kumene Yehova anamutuma kuti akanenere, nakayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Yehova ndi kuwawuza anthu kuti,
15 Tak mówi Pan zastępów, Bóg Izraelski: Oto Ja przywiodę na to miasto i na wszystkie miasto jego wszystko to złe, którem wyrzekł przeciw niemu; bo zatwardzili kark swój, aby nie słuchali słów moich.
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Tamverani! Ine ndidzabweretsa masautso amene ndinanena aja pa mzinda uno ndi pa mizinda yozungulira, chifukwa anthu ake ndi nkhutukumve ndipo sanamvere mawu anga.’”

< Jeremiasza 19 >