< Izajasza 42 >

1 Oto sługa mój, spolegać będę na nim, wybrany mój, którego sobie upodobała dusza moja. Dam mu Ducha swego, on sąd narodom wyda.
“Nayu mtumiki wanga, amene ndimamuchirikiza, amene ndamusankha, amenenso ndimakondwera naye. Ndayika Mzimu wanga mwa Iyeyo, ndipo adzaweruza anthu a mitundu yonse mwachilungamo.
2 Nie będzie wołał, ani się będzie wywyższał, ani będzie słyszany na ulicy głos jego.
Iye sadzafuwula, sadzamveka mawu, kapena mawu ake kumveka mʼmisewu.
3 Trzciny nałamanej nie dołamie, a lnu kurzącego się nie dogasi; ale sąd wyda według prawdy.
Bango lophwanyika sadzalithyola, ndipo moto wozilala sadzawuzimitsa. Motero adzaonetsa kuti chilungamo ndicho choonadi;
4 Nie zamroczy się, ani ustanie, dokąd nie wykona sądu na ziemi, a nauki jego wyspy oczekiwać będą.
sadzafowoka kapena kukhumudwa mpaka atakhazikitsa chilungamo pa dziko lapansi, ndi mpaka mayiko a mʼmbali mwa nyanja atafika poyembekezera malangizo ake.”
5 Tak mówi Bóg, Pan, który stworzył niebiosa i rozpostarł je; który rozszerzył ziemię, i co się rodzi z niej; który daje tchnienie ludowi mieszkającemu na niej, a ducha tym, co chodzą po niej.
Yehova Mulungu amene analenga zamlengalenga ndi kuziyalika, amene analenga dziko lapansi ndi zonse zimene zimabereka, amenenso amapereka mpweya kwa anthu ake okhala mʼdzikomo, ndi moyo kwa onse oyendamo, akuti,
6 Ja Pan wezwałem cię w sprawiedliwości, i ująłem cię za rękę twą; przetoż strzedz cię będę, i dam cię za przymierze ludowi, i za światłość narodom.
“Ine Yehova, ndakuyitana chifukwa Ine ndine wolungama; ndikugwira dzanja ndipo ndidzakuteteza. Ndakupereka kukhala pangano langa kwa anthu ndi kuwunika kwa anthu a mitundu ina.
7 Aby otwierał oczy ślepych, a wywodził więźniów z ciemnicy, i z domu więzienia siedzących w ciemnościach.
Udzatsekula maso a anthu osaona, udzamasula anthu a mʼndende ndi kutulutsa mʼndende anthu okhala mu mdima.
8 Ja Pan, toć jest imię moje, a chwały mojej nie dam innemu, ani sławy mojej bałwanom rytym.
“Ine ndine Yehova: dzina langa ndi limenelo! Sindidzapereka ulemerero wanga kwa wina aliyense kapena matamando anga kwa mafano.
9 Oto pierwsze rzeczy przyszły, Ja też nowe opowiadam, pierwej, niż się zaczną, dam wam o nich słyszeć.
Taonani, zinthu zimene ndinalosera kale zachitikadi, ndipo ndikuwuzani zinthu zatsopano; zinthuzo zisanaonekere Ine ndakudziwitsani.”
10 Śpiewajcie Panu pieśń nową, chwała jego jest od kończyn ziemi, którzy się pławicie po morzu, i wszystko, co w niem jest, wyspy i obywatele ich.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, mutamandeni inu okhala mʼdziko lonse lapansi, inu amene mumayenda pa nyanja, nyanja ikokome ndi zonse zili mʼmenemo. Inu okhala pa zilumba tamandani Yehova.
11 Podnieście głos pustynie, i miasta jej, i wsi, w których mieszka Kedar; wykrzykajcie obywatele skał, z wierzchu gór wołajcie.
Chipululu ndi mizinda yake zikweze mawu awo; midzi ya Akedara ikondwere. Anthu a ku Sela ayimbe mwachimwemwe; afuwule kuchokera pamwamba pa mapiri.
12 Oddajcie cześć Panu, a chwałę jego na wyspach opowiadajcie.
Atamande Yehova ndipo alalike matamando ake kwa anthu apazilumba zonse.
13 Pan wynijdzie jako mocarz, jako mąż waleczny wzruszy się gorliwością; trąbić, owszem krzyczeć będzie, a przeciw nieprzyjaciołom swoim mężnie sobie pocznie,
Yehova adzapita ku nkhondo ngati munthu wamphamvu, adzawutsa ukali wake ngati munthu wankhondo; akukuwa ndiponso akufuwula mfuwu wankhondo ndipo adzagonjetsa adani ake.
14 Mówiąc: Milczałem dość długo, jakobym nie słyszał, wstrzymywałem się; ale już jako rodząca krzyczeć będę, spustoszę, i wszystkich oraz połknę.
Yehova akuti, “Ndakhala ndili chete kwa nthawi yayitali, ndakhala ndili phee osachita kanthu. Koma tsopano, ngati mayi pa nthawi yochira, ndi kubuwula ndi kupuma modukizadukiza ndipo ndili wefuwefu.
15 W pustynie góry i pagórki obrócę, i wszystkie zioła ich posuszę; obrócę i rzeki w wyspy, a jeziora wysuszę.
Ndidzawononga mapiri ndi zitunda ndipo ndidzawumitsa zomera zawo zonse; ndidzasandutsa mitsinje kukhala zilumba ndipo ndidzawumitsa maiwe.
16 I powiodę ślepych drogą, której nie znali, a ścieszkami, o których nie wiedzieli, poprowadzę ich; obrócę przed nimi ciemności w światłość, a co nierównego, w równinę. Toć jest, co im uczynię, a nie opuszczę ich.
Ndidzatsogolera anthu osaona mʼmisewu imene sanayidziwe, ndidzawatsogolera mʼnjira zimene sanayendepo; ndidzasandutsa mdima wa kutsogolo kwawo kuti ukhale kuwala ndipo ndidzasalaza malo osalala. Zimenezi ndizo ndidzachite; sindidzawataya.
17 Cofną się nazad, i zawstydzą się bardzo, którzy ufają w bałwanach rytych, którzy mówią obrazom litym: Wyście bogowie nasi.
Koma onse amene amadalira mafano amene amanena kwa mafanowo kuti, ‘ndinu milungu yathu,’ ndidzawachititsa manyazi kotheratu.
18 O głusi! słuchajcie; a wy ślepi! przejrzyjcie, abyście widzieli.
“Imvani, agonthi inu; yangʼanani osaona inu, kuti muone!
19 Któż ślepy, jedno sługa mój? a kto głuchy, jedno poseł mój, którego posyłam? Któż tak ślepy jako doskonały, ślepy, mówię, jako sługa Pański?
Ali wosaona ndani, si mtumiki wanga kodi? Ndipo ndani ali wosamva ngati mthenga amene ndamutuma? Kodi ndani ali wosaona ngati uja ndinachita naye pangano, kapena wosaona ndani ngati mtumiki wa Yehova?
20 Widzi wiele rzeczy, a wszakże nie zrozumiewa; otworzone ma uszy, wszakże nie słyszy.
Iwe waona zinthu zambiri, koma sunazisamale; makutu ako ndi otsekuka koma sumva kanthu.”
21 Pan go sobie upodobał dla sprawiedliwości swojej; uwielbił go zakonem, i sławnym go uczynił.
Chinamukomera Yehova chifukwa cha chilungamo chake, kapena lamulo lake kukhala lalikulu ndi lopambana.
22 Ale ten lud jest złupiony i rozszarpany, którego młodzieńców ile ich kolwiek jest, imają, i do ciemnic podawają; podani są na łup, a niemasz ktoby ich wybawił; podani są na rozchwycenie, ani jest, ktoby rzekł: Wróć ich zaś.
Koma awa ndi anthu amene afunkhidwa ndi kuwalanda zinthu zawo, onsewa anawakola mʼmaenje kapena akuwabisa mʼndende. Tsono asanduka chofunkha popanda wina wowapulumutsa kapena kunena kuti, “Abwezeni kwawo.”
23 Któż to z was w uszy przyjmuje? kto zrozumiewa, aby czulszym był napotem?
Kodi ndani wa inu amene adzamvetsera zimenezi kapena kutchera khutu ndi kumva za mʼtsogolomo?
24 Kto podał na rozszarpanie Jakóba, a Izraela łupieżcom? Izali nie Pan, przeciwko któremuśmy zgrzeszyli? Bo nie chcieli drogami jego chodzić, ani słuchać zakonu jego.
Ndani anapereka Yakobo kwa ofunkha, ndi Israeli kwa anthu akuba? Kodi si Yehova, amene ife tamuchimwirayu? Pakuti sanathe kutsatira njira zake; ndipo sanamvere malangizo ake.
25 Dlatego nań Pan wylał popędliwość gniewu swego, i gwałtowną wojnę, a zapalił go w około, a wszakże nie poznał tego; zapalił go, mówię, a wszakże tego do serca nie przypuścił.
Motero anawakwiyira kwambiri, nawavutitsa ndi nkhondo. Anayatsa moto ponseponse mowazungulira komabe iwo sanamvetse; motowo unawapsereza, koma iwo sanatengepo phunziro ayi.

< Izajasza 42 >