< Izajasza 41 >

1 Umilknijcie przedemną, wyspy! a narody niech się posilą. Niech przystąpią a niech mówią: Przystąpmy społem do sądu
“Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja! Alekeni ayandikire ndi kuyankhula; tiyeni tikhale pamodzi kuti atiweruze.
2 Któż wzbudził od wschodu słońca sprawiedliwego, i wezwał go, aby go naśladował? Któż mu podbił narody, aby nad królami panował, podawszy je jako proch pod miecz jego, a jako plewy rozproszone pod łuk jego?
“Ndani anadzutsa wochokera kummawa uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita? Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
3 Uganiał się z nimi, przeszedł spokojnie ścieszkę, po której nogami swemi nie chadzał.
Amawalondola namayenda mosavutika, mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
4 Któż to sprawił i uczynił? któż wzywał rodzaje od początku? Ja Pan, pierwszy i ostatni, Ja sam.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza, si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu? Ine Yehova, ndine chiyambi ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”
5 Widziały wyspy, i ulękły się; kończyny ziemi zdumiały się; zgromadziły się, i zeszły się.
Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa; anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera. Akuyandikira pafupi, akubwera;
6 Jeden drugiemu pomagał, a bratu swemu mówił: Zmacniaj się!
aliyense akuthandiza mnzake ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
7 A tak zmacniał teszarz złotnika, blachę młotem gładzącego, kującego na kowadle, mówiąc: Do lutowania to dobre. Potem to stwierdził gwoździami, aby się nie ruszyło.
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide, ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala. Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.” Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.
8 Ale ty, Izraelu, sługo mój! ty Jakóbie, któregom obrał, nasienie Abrahama, przyjaciela mego!
“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga, Yakobo amene ndakusankha, Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
9 Ty, któregom pochwycił od kończyn ziemi, owszem, pominąwszy przedniejszych ich, powołałem cię mówiąc do ciebie: Sługaś ty mój, obrałem cię, a nie odrzuciłem cię.
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi, ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi. Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’ Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Nie bój się! bom Ja z tobą. Nie lękaj się! bom Ja Bogiem twoim. Zmocnię cię, a dam ci pomoc, i podeprę cię prawicą sprawiedliwości swojej.
Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe; usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako. Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza, ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.
11 Oto zawstydzą się, a będą pohańbieni wszyscy gniewem pałający przeciwko tobie: staną się jako nic, i zginą ci, którzy się tobie sprzeciwiają.
“Onse amene akupsera mtima adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa; onse amene akukangana nawe sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Szukałlibyś ich, nie znajdziesz ich; ci, którzy się sprzeciwiają tobie, będą jako nic, a ci, którzy walczą z tobą, w niwecz obróceni będą.
Udzafunafuna adani ako, koma sadzapezeka. Iwo amene akuchita nawe nkhondo sadzakhalanso kanthu.
13 Bom ja Pan, Bóg twój, trzymam cię za prawicę twoję, a mówięć: Nie bój się! Ja cię wspomogę.
Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako, amene ndikukugwira dzanja lako lamanja ndipo ndikuti, usaope; ndidzakuthandiza.
14 Nie bój się, robaczku Jakóbie, garstko ludu Izraelskiego! Jać będę na pomocy, mówi Pan a odkupiciel twój, Święty Izraelski.
Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi, iwe wochepa mphamvu Israeli, chifukwa Ine ndidzakuthandiza,” akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 Otom cię uczynił jako wóz z zębami nowemi po obu stronach; i pomłócisz góry, a potrzesz je, a pagórki jako plewę położysz.
“Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri. Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya, ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Przewiejesz je, wtem je wiatr porwie, a wicher rozproszy je; ale się ty rozradujesz w Panu, w Świętym Izraelskim będziesz się chlubił.
Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso adzamwazika ndi kamvuluvulu. Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako, ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:
17 Ubogich i nędznych, którzy szukają wody, a niemasz jej, których język usechł od pragnienia, Ja Pan wysłucham ich; Ja, Bóg Izraelski, nie opuszczę ich.
“Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi, koma sakuwapeza; ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu. Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo; Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Otworzę rzeki na miejscach wysokich, a źródła w pośród równin; obrócę pustynie w jeziora wód, a ziemię suchą w strumienie wód.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma, ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa. Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 Nasadzę na puszczy cedrów, wybornych cedrów, sosien, i oliwnych drzew; nasadzę pustynię jedliną, wiązem, i bukszpanem;
Mʼchipululu ndidzameretsa mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi. Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 Aby widzieli, i poznali, i uważali, i zrozumieli, że to ręka Pańska uczyniła, i że to Święty Izraelski stworzył.
kuti anthu aone ndi kudziwa; inde, alingalire ndi kumvetsa, kuti Yehova ndiye wachita zimenezi; kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.
21 Przedłóżcie sprawę waszę, mówi Pan; ukażcie mocne dowody swoje, mówi król Jakóbowy.
“Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’ Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Niech przystąpi, a niech nam oznajmi to, co się ma stać; rzeczy pierwsze, które były, powiedzcie, abyśmy uważyli w sercu swem, a poznali cel ich; albo przynajmniej nam przyszłe rzeczy oznajmijcie.
Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze zomwe zidzachitike mʼtsogolo. Tifotokozereni zinthu zamakedzana tiziganizire ndi kudziwa zotsatira zake. Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23 Oznajmijcie, co ma przyjść napotem, a poznamy, żeście bogowie; albo uczyńcie co dobrego lub złego, abyśmy się zdumiewali, gdybyśmy to społem widzieli.
tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani, ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu. Chitani chinthu chabwino kapena choyipa, ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Otoście wy zgoła na nic, a sprawa wasza także na nic nie jest; przetoż obrzydły jest ten, co was sobie obiera.
Koma inu sindinu kanthu ndipo zochita zanu nʼzopandapake; amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.
25 Wzbudzę od północy lud, ten przyciągnie; i od wschodu słońca, ten wzywać będzie imienia mego; oborzy się na książąt jako na błoto, a podepcze ich, jako garncarz glinę.
“Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera, munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana. Amapondaponda olamulira ngati matope, ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Kto oznajmi od początku? tedy będziemy wiedzieli; albo co było od dawnych czasów? tedy rzeczemi: Tyś jest sprawiedliwy? Niemasz zgoła nikogo, coby oznajmił, ani jest, ktoby się dał słyszeć, albo ktoby słyszał mowy wasze.
Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe, kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’ Palibe amene ananena, palibe analengeza zimenezi, palibe anamva mawu anu.
27 Jam pierwszy, który Syonowi opowiadam: Oto, oto są; a Jeruzalemowi dam opowiadaczy rzeczy pociesznych.
Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’ Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 Bo widzę, że niemasz nikogo, niemasz nikogo między nimi, coby dał radę; acz się ich pytają, wszakże nie odpowiadają i słowa.
Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe, palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu, palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Oto ci wszyscy są marnością, za nic nie stoją uczynki ich; wiatrem i próżnością są odlewane bałwany ich.
Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo! Zochita zawo si kanthu konse; mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.

< Izajasza 41 >