< Izajasza 4 >

1 A w on dzień uchwyci się siedm niewiast męża jednego, mówiąc: Chleb swój jeść będziemy, i odzieniem swem przyodziewać się będziemy; tylko niech nas zowią od imienia twego, a odejmij pohańbienie nasze.
Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi, nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu, ndi kuvala zovala zathu; inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu. Tichotseni manyazi aumbeta!”
2 W on dzień latorośl Pańska zacna i sławna będzie, a owoc ziemi bujny i pozorny tym, którzy zachowani będą z Izraela.
Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli.
3 I stanie się, że kto zostanie na Syonie, i który zostawiony będzie w Jeruzalemie, świętym słynąć będzie, każdy, który jest napisany do żywota w Jeruzalemie.
Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu.
4 Gdy omyje Pan plugastwo córek Syońskich, a krew Jeruzalemską opłócze z niego w duchu sądu, i w duchu zapalenia.
Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto.
5 I stworzy Pan nad każdem miejscem góry Syońskiej, i nad każdem zgromadzeniem jej obłok we dnie, a dym i jasność pałającego ognia w nocy: bo nad wszystką sławą będzie ochrona.
Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova.
6 A będzie namiotem na zasłonę we dnie od gorąca, a na ucieczkę i ukrycie przede dżdżem i powodzią.
Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.

< Izajasza 4 >