< Izajasza 36 >

1 I stło się czternastego roku królowania Ezechyjasza, że przyciągnął Sennacheryb, król Assyryjski, przeciwko wszystkim miastom Judzkim obronnym, i pobrał je.
Chaka cha khumi ndi chinayi cha ulamuliro wa Mfumu Hezekiya, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anathira nkhondo mizinda yonse yotetezedwa ya ku Yuda, nayilanda.
2 I posłał król Assyryjski Rabsacesa z Lachys, do Jeruzalemu, do króla Ezechyjasza z wielkiem wojskiem, który stanął u rur sadzawki wyższej przy drodze pola blecharzowego.
Kenaka mfumu ya ku Asiriya inatuma kazembe wake wankhondo pamodzi ndi gulu lalikulu lankhondo kuchokera ku Lakisi kupita kwa mfumu Hezekiya ku Yerusalemu. Tsono kazembeyo anayima pafupi ndi ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe lakumtunda pa msewu wopita ku malo a munda wa mmisiri wochapa zovala.
3 Tedy wyszedł do niego Elijakim, syn Helkijaszowy, przełożony nad domem, i Sobna pisarz, i Joach, syn Asafowy, kanclerz.
Panali anthu atatu. Woyamba anali Eliyakimu mwana wa Hilikiya komanso ndiye woyangʼanira nyumba ya mfumu. Wachiwiri anali Sebina amene anali mlembi wa bwalo; ndipo wachitatu anali Yowa mwana wa Asafu komanso anali wolemba zochitika. Anthu awa anatuluka kukakumana ndi kazembe wa ankhondo uja.
4 I rzekł do nich Rabsaces: Proszę, powiedzcie Ezechyjaszowi: Tak mówi król wielki, król Assyryjski: Cóż to za ufność, którą ufasz?
Kazembe wa ankhondo anawawuza kuti, “Kamuwuzeni Hezekiya kuti, “Mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya ikunena kuti, Kodi chikukulimbitsa mtima ndi chiyani?
5 Rzekłbym: (Acz to rzecz daremna) Snać rady i mocy do wojny dosyć masz; ale w kimże ufasz, że mi się sprzeciwiasz?
Iwe ukuti uli ndi luso ndiponso mphamvu pa nkhondo, komatu ukuyankhula mawu opanda pake. Kodi tsono iwe ukudalira yani kuti undiwukire ine?
6 Otoś spoległ na lasce tej trzciny nałamanej, na Egipcie, którą jeźliby się kto podparł, wnijdzie w rękę jego, i przekole ją. Takić jest Farao, król Egipski, wszystkim, którzy w nim ufają.
Taona tsono, iwe ukudalira Igupto, bango lothyokalo, limene limalasa mʼmanja mwa munthu ngati waliyesa ndodo yoyendera! Umo ndi mmene Farao mfumu ya ku Igupto imachitira aliyense amene akuyidalira.
7 A jeźli mi rzeczesz: W Panu, Bogu naszym, ufamy; azaż nie ten jest, którego zniósł Ezechyjasz wyżyny i ołtarze, i przykazał Judzie i Jeruzalemowi mówiąc: Przed tym ołtarzem kłaniać się będziecie?
Ndipo ngati ukunena kwa ine kuti, ‘Ife tikudalira Yehova Mulungu wathu,’ kodi si Mulungu yemweyo amene nyumba zake ndi maguwa ake, Hezekiya anachotsa, nawuza anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe ili?’
8 Przetoż teraz proszę, zaręcz się Panu memu, królowi Assyryjskiemu, a ja tobie dam dwa tysiące koni, będzieszli je mógł osadzić jezdnymi.
“Ndipo tsopano bwera udzakambirane ndi mbuye wanga, mfumu ya ku Asiriya: Ine ndidzakupatsa akavalo 2,000 ngati ungathe kupeza okwerapo!
9 I jakoż się ty możesz oprzeć hetmanowi jednemu najmniejszemu z sług pana mego, choć ufasz w Egipcie dla wozów i jezdnych?
Iwe ungathe bwanji kugonjetsa ngakhale mmodzi mwa akazembe angʼonoangʼono a mbuye wanga, pamene ukudalira Igupto kuti akupatse magaleta ndi anthu okwera pa akavalo.
10 Nadto czy bez woli Pańskiej przyciągnąłem do tej ziemi, abym ją spustoszył? Pan rzekł do mnie: Ciągnij do tej ziemi, a spustosz ją.
Kuwonjezera pamenepa, kodi ine ndabwera kudzathira nkhondo ndi kuwononga dziko lino popanda chilolezo cha Yehova? Yehova mwini ndiye anandiwuza kuti ndidzathire nkhondo ndi kuwononga dziko lino.”
11 Tedy rzekł Elijakim, i Sobna, i Joach do Rabsacesa: Proszę, mów do sług twoich po syryjsku, wszak rozumiemy, a nie mów do nas po żydowsku przed tym ludem, który jest na murze.
Pamenepo Eliyakimu, Sebina ndi Yowa anawuza kazembeyo kuti, “Chonde yankhulani kwa atumiki anufe mʼChiaramu, popeza timachimva. Musayankhule nafe mu Chihebri kuopa kuti anthu onse amene ali pa khomapa angamve.”
12 I odpowiedział Rabsaces: Azaż mię do Pana twego albo do ciebie posłał Pan mój, abym te słowa mówił? Posłał mię raczej do mężów, którzy siedzą na murze, aby jedli łajna swoje, a mocz swój pospołu z wami pili.
Koma kazembeyo anayankha kuti, “Kodi mbuye wanga wandituma kuti ndidzanene zinthu izi kwa mbuye wanu yekha ndi inu nokha basi? Ayi, komanso kwa anthu amene akhala pa khomawa. Iwowa adzadya chimbudzi chawo chomwe ndi kumwa mkodzo wawo womwe monga momwe mudzachitire inuyonso.”
13 A tak stanął Rabsaces i wołał głosem wielkim po żydowsku, mówiąc: Słuchajcie słów króla wielkiego, króla Assyryjskiego.
Tsono kazembeyo anayimirira nafuwula mu Chihebri kuti, “Imvani mawu a mfumu yayikulu, mfumu ya ku Asiriya!
14 Tak mówi król: Niech was nie zwodzi Ezechyjasz: bo was nie będzie mógł wybawić.
Zimene mfumu ikunena ndi izi: Musalole kuti Hezekiya akunamizeni. Iye sangakupulumutseni!
15 A niech wam nie rozkazuje Ezechyjasz ufać w Panu, mówiąc: Zapewne nas Pan wybawi, a nie będzie to miasto podane w rękę króla Assyryjskiego.
Hezekiya asakukakamizeni kudalira Yehova ndi mawu akuti, ‘Ndithu, Yehova adzatipulumutsa; ndipo sadzapereka mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya.’
16 Nie słuchajcież Ezechyjasza; albowiem tak powiedział król Assyryjski: Uczyńcie zemną przymierze, a wynijdźcie do mnie, a jedz każdy z was z winnicy swojej, i każdy z figowego drzewa swego, a pij każdy z was wodę z studni swojej;
“Musamumvere Hezekiya. Zimene mfumu ya ku Asiriya ikunena ndi izi: Pangani mtendere ndi ine ndipo mutuluke mu mzinda. Mukatero aliyense wa inu adzadya mphesa ndi nkhuyu za mʼmunda mwake ndiponso adzamwa madzi a mʼchitsime chake,
17 Aż przyjdę a pobiorę was do ziemi podobnej ziemi waszej, do ziemi zboża i wina, do ziemi chleba i winnic.
mpaka mfumuyo itabwera kudzakutengani kupita ku dziko lofanana ndi lanulo, dziko limene lili ndi tirigu ndi vinyo watsopano, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
18 Niech was nie zwodzi Ezechyjasz, mówiąc: Pan nas wybawi. Izaż mogli bogowie narodów wybawić każdy ziemię swoję z ręki króla Assyryjskiego?
“Inu musalole kuti Hezekiya akusocheretseni pamene iye akuti, ‘Yehova adzatipulumutsa.’ Kodi alipo mulungu wa anthu a mtundu wina amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya?
19 Gdzież są bogowie Emat i Arfad? Gdzie są bogowie Sefarwaim? Azaż wybawił Samaryję z ręki mojej?
Kodi ili kuti milungu ya Hamati ndi Aripadi? Ili kuti milungu ya Sefaravaimu? Kodi inapulumutsa Samariya mʼdzanja langa?
20 Którzyż są między wszystkimi bogami tych ziem, którzyby wydarli ziemię swoję z ręki mojej? A miałby Pan wybawić Jeruzalem z ręki mojej?
Kodi ndi milungu iti mwa milungu yonse ya mayiko awa amene anapulumutsa dziko lake mʼdzanja? Nanga tsono Yehova adzapulumutsa Yerusalemu mʼdzanja langa motani?”
21 Ale oni milczeli, i nie odpowiedzieli mu i słowa; bo takie było rozkazanie królewskie, mówiąc: Nie odpowiadajcie mu.
Koma anthu anakhala chete ndipo sanayankhepo kanthu, chifukwa mfumu inawalamula kuti, “Musayankhe.”
22 I przyszedł Elijakim, syn Helkijaszowy, przełożony domu, i Sobna pisarz, i Joach, syn Asafowy, kanclerz, do Ezechyjasza, rozdarłszy szaty swe, i oznajmili mu słowa Rabsacesowe.
Pamenepo anthu atatu aja Eliyakimu, mwana wa Hilikiya amene ankayangʼanira nyumba ya mfumu; Sebina mlembi wa bwalo; ndi Yowa, mwana wa Asafu mlembi wa zochitika anapita kwa Hezekiya atangʼamba zovala zawo ndipo anamuwuza zonse zimene anayankhula kazembe uja.

< Izajasza 36 >