< Izajasza 10 >

1 Biada tym, którzy stanowią prawa niesprawiedliwe! i pisarzom, którzy ucisk na innych spisują!
Tsoka kwa anthu amene amapanga malamulo opanda chilungamo, kwa iwo amene amalemba zongovutitsa anzawo,
2 Aby odpychali ubogiego od sądu, a wydzierali sprawiedliwość ubogich ludu mego; aby wdowy były korzyścią ich, a sierotki łupem ich.
kuwalanda anthu osauka ufulu wawo ndi kumana chilungamo osautsidwa pakati pa anthu anga, amalanda zinthu za akazi amasiye ndi kubera ana amasiye.
3 Cóż uczynicie w dzień nawiedzenia, i spustoszenia, które z daleka przyjdzie? do kogoż się ucieczecie o wspomożenie? a gdzie zostawicie sławę waszę?
Kodi mudzatani pa tsiku la chilango, pofika chiwonongeko chochokera kutali? Kodi mudzathawira kwa yani kuti akuthandizeni? Nanga chuma chanu mudzachisiya kuti?
4 Aby się nie miała między więźniami uniżyć, i między pobitymi upaść. A wszakże w tem wszystkiem nie odwróci się zapalczywość jego; ale jeszcze ręką jego będzie wyciągniona.
Kudzatsala nʼkungozolika mwamanyazi pakati pa anthu ogwidwa kapena kufa pamodzi ndi ophedwa. Komabe pa zonsezi mkwiyo wake sunawachokere, mkono wake uli chitambasulire.
5 Biada Assurowi, rózdze gniewu mego! chociaż kij rozgniewania mego jest w ręku jego.
“Tsoka kwa mfumu ya ku Asiriya, chikwapu cha mkwiyo wanga, iye ndiye ndodo ya mkwiyo wanga!
6 Na naród obłudny poślę go, a o ludu zapalczywości mojej przykażę mu, aby brał łup i wydzierał korzyści a położył go na podeptanie, jako błoto na ulicach.
Ndidzamutuma kukalimbana ndi mtundu wosapembedza Mulungu, ndidzamutumiza kukalimbana ndi anthu amene amandikwiyitsa Ine, kukafunkha ndi kulanda chuma, ndi kuwapondereza pansi ngati matope a mʼmisewu.
7 Lecz on nie tak będzie mniemał, i serce jego nie tak będzie myślało, ponieważ w sercu swem ułożył, aby wytracił i wykorzenił niemało narodów.
Koma izi si zimene akufuna kukachita, izi si zimene zili mʼmaganizo mwake; cholinga chake ndi kukawononga, kukapulula mitundu yambiri ya anthu.
8 Albowiem rzecze: Izali książęta moi nie są też i królmi?
Iye akuti, ‘Kodi atsogoleri anga ankhondo si mafumu okhaokha?’
9 Izali Chalmo nie jest jako Karchemis? Izali Arfat nie jest jako Emat? Izali Samaryja nie jest jako Damaszek?
‘Kodi Kalino sanagonjetsedwe monga Karikemesi? Kodi Hamati sali ngati Aripadi, nanga Samariya sali ngati Damasiko?
10 Jako ręka moja znalazła królestwa bałwańskie, chociaż bałwany ich większe były, niż w Jeruzalemie i w Samaryi.
Dzanja langa linakantha maufumu a anthu opembedza mafano, mafumu amene mafano awo ndi aakulu kupambana Yerusalemu ndi Samariya;
11 Izali Jeruzalemowi i bałwanom jego tak nie uczynię, jakom uczynił Samaryi i bałwanom jej?
nanga Ine nʼkulephera kodi kuwononga Yerusalemu pamodzi ndi mafano ake monga ndinakanthira Samariya pamodzi ndi mafano ake?’”
12 I stanie się, gdy Pan wykona wszystkę sprawę swoję na górze Syońskiej i w Jeruzalemie, że nawiedzę owoc wyniosłego serca króla Assyryjskiego, i pychę wysokich oczów jego;
Ambuye akadzamaliza ntchito yonse yolanga phiri la Ziyoni ndi Yerusalemu adzalanganso mfumu ya ku Asiriya chifukwa cha kudzitama ndi kunyada kwake.
13 Bo rzecze: W mocy ręki mojej uczyniłem to, i w mądrości mojej; bom był mądry, i odjąłem granice narodów, a skarby ich zabrałem, i wytraciłem obywateli jako mocarz.
Pakuti mfumuyo ikuti, “‘Ndachita zimenezi ndi dzanja langa, ndiponso ndi nzeru zanga, chifukwa ndine wozindikira zinthu. Ndinachotsa malire a mitundu ya anthu, ndinafunkha chuma chawo; ndinagonjetsa mafumu awo monga munthu wamphamvu.
14 Owszem ręka moja znalazła majętność narodów jako gniazdo; a jako zbierają jajka, które są opuszczone, takiem ja wszystkę ziemię zebrał, a nie był ktoby skrzydłem ruszył, albo otworzył usta, i coby mruczał.
Dzanja langa lagwira chuma cha mitundu ya anthu ngati momwe munthu amagwirira chisa cha mbalame, ngati momwe anthu amatolera mazira osiyidwa, motero inenso ndinasonkhanitsa mayiko onse; palibe mbalame imene inakupiza mapiko ake, kapena kuyasama kukamwa kuti ilire.’”
15 Izali się będzie przechwalała siekiera przeciw temu, który nią rąbie? Izali się będzie wynosiła piła przeciw temu, który nią trze? jakożby się wynosiła rózga przeciw temu, który ją podniósł? jakożby się przechwalał kij, że nie jest drewnem?
Kodi nkhwangwa ingathe kudzikuza kupambana woyigwiritsa ntchito, kapena macheka angathe kudzikuza kupambana wowagwiritsa ntchito? Ndiye kukhala ngati kuti chikwapu chikuzunguza munthu amene wachinyamula, kapena ngati kuti ndodo ikuopseza amene wayinyamula!
16 Przetoż Pan, Pan zastępów, pośle na tłustych jego suchoty, a pod sławą jego z prędka się zapali, jako gwałtowny ogień;
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzatumiza matenda owondetsa kwa ankhondo amphamvu; kunyada kwa mfumuyo kudzapsa ndi moto wosazima.
17 Bo Światłość Izraelowa będzie ogniem, a Święty jego płomieniem, który spali i pożre ciernie jego i oset jego dnia jednego.
Mulungu, Kuwala kwa Israeli, adzakhala ngati moto, Woyera uja wa Israeli adzakhala ngati malawi a moto. Motowo udzawatentha ndi kuwapsereza ngati minga ndi mkandankhuku pa tsiku limodzi.
18 Także wspaniałość lasu jego i urodzajnych pól jego, od duszy aż do ciała zniszczy, i stanie się jako chorąży od strachu uciekający.
Ankhondo ake adzawonongedwa ngati nkhalango yayikulu ndi ngati nthaka yachonde.
19 A pozostałych drzew lasu jego mała liczba będzie, tak, że je i dziecię będzie popisać mogło.
Mitengo yotsalira ya mʼnkhalango zake idzakhala yochepa kwambiri, yoti ndi mwana yemwe ndi kuyiwerenga.
20 I stanie się dnia onego, że ostatki Izraelskie, i ci, którzy zostali z domu Jakóbowego, nie będą więcej spolegać na tym, co ich bije; ale prawdziwie spolegać będą na Panu, Świętym Izraelskim.
Tsiku limenelo otsalira a ku Israeli, opulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzadaliranso anthu amene anawakantha, koma adzadalira Yehova, Woyerayo wa Israeli.
21 Ostatek nawróci się, ostatek Jakóbowy do Boga mocnego.
Otsalira adzabwerera, otsalira a Yakobo adzabwerera kwa Mulungu Wamphamvu.
22 Bo choćby lud twój, o Izraelu! był jako piasek morski, ostatek tylko z niego nawróci się. Wytracenie naznaczone sprawi, że ziemia będzie opływała sprawiedliwością.
Iwe Israeli, ngakhale anthu ako achuluke ngati mchenga wa ku nyanja, otsala okha ndiwo adzabwerere. Chiwonongeko chalamulidwa, chidzaonetsa chilungamo chosefukira.
23 Wytracenie mówię naznaczone uczyni Pan, Pan zastępów, w pośrodku tej wszystkiej ziemi.
Ambuye Yehova Wamphamvuzonse adzawononga ndithu dziko lonse monga momwe analamulira.
24 Przetoż tak mówi Pan, Pan zastępów: Nie bój się Assyryjczyka, ludu mój! który mieszkasz w Syonie; rózgą ubije cię, a laskę swą podniesie na cię, jako na drodze Egipskiej.
Nʼchifukwa chake, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, “Inu anthu anga okhala mu Ziyoni, musawaope Asiriya, amene amakukanthani ndi ndodo nakumenyani ndi zibonga monga mmene Igupto anachitira.
25 Albowiem po maluczkim czasie skończy się gniew mój przeciwko tobie, a na wygładzenie ich zapalczywość moja powstanie.
Patsala pangʼonongʼono kuti mkwiyo wanga uchoke pa inu ndipo ndidzaonetsa ukali wanga pa iwo mpaka kuwawononga.”
26 Gdyż bicz nań wzbudzi Pan zastępów, jako porażkę Madyjańczyków na skale Horeb; a jako podniósł rózgę swoję na morze na drodze Egipskiej tak ją nań podniesie.
Yehova Wamphamvuzonse adzawakwapula ndi chikwapu, monga momwe anakwapulira Amidiyani ku thanthwe la Orebu; ndipo adzatukula ndodo yake pa madzi ndikuwalanga monga analangira Igupto pa nyanja.
27 A dnia onego zdjęte będzie brzemię jego z ramienia twego, i jarzmo jego z szyi twojej; owszem, skażone będzie jarzmo od przytomności pomazanego.
Tsiku limenelo katundu wawo adzachotsedwa pa mapewa anu, goli lawo lidzachoka mʼkhosi mwanu; golilo lidzathyoka chifukwa cha kunenepa kwambiri.
28 Przyciągnie do Ajat, przejdzie przez Migron, w Machmas złoży oręż swój.
Adani alowa mu Ayati apyola ku Migironi; asunga katundu wawo ku Mikimasi.
29 Przejdą bród, w Gieba jako w gospodzie nocować będą; ulęknie się Rama, Gabaa Saulowe uciecze.
Adutsa pa mpata uja, ndipo akuti, “Tikagona ku Geba” Rama akunjenjemera; Gibeya, mzinda wa Saulo ukuthawa.
30 Podnieś głos twój, córko Gallim! niech słyszą w Lais, o ubogie Anatot!
Lilani mokweza, inu anthu a ku Galimu! Tchera khutu, iwe Laisa! Iwe Anatoti wosauka!
31 Ustąpi Madmena; obywatele Gabim zbiorą się do uciekania.
Anthu a ku Madimena akuthawa; anthu a ku Gebimu bisalani.
32 Jeszcze przez dzień zastanowiwszy się w Nobie, pogrozi ręką swą górze córki Syońskiej, i pagórkowi Jeruzalemskiemu.
Lero lomwe lino adaniwo adzayima ku Nobu; adzagwedeza mikono yawo, kuopseza anthu a ku Ziyoni, pa phiri la Yerusalemu.
33 Oto Pan, Pan zastępów, okrzesze wszystkę siłę latorośli, a te, którzy są wysokiego wzrostu, podetnie; i będą wysocy poniżeni.
Taonani, Ambuye Yehova Wamphamvuzonse, adzadula mwamphamvu nthambi za mitengo, mitengo yodzikweza idzadulidwa, mitengo yayitali idzagwetsedwa.
34 Gęstwiny także lasów siekiera wytnie, a Liban od wielmożnego upadnie.
Yehova adzadula ndi nkhwangwa mitengo ya mʼnkhalango yowirira; Lebanoni adzagwa pamaso pa Wamphamvu.

< Izajasza 10 >