< Rodzaju 10 >

1 Teć są rodzaje synów Noego, Sema, Chama i Jafeta, którym się narodziło synów po potopie.
Nayi mbiri ya ana a Nowa, Semu, Hamu ndi Yafeti. Ana atatuwa anabereka ana awo chitatha chigumula.
2 Synowie Jafetowi Gomer, i Magog, i Madai, i Jawan, i Tubal, i Mesech, i Tyras.
Ana aamuna a Yafeti anali: Gomeri, Magogi, Madai, Yavani, Tubala, Mesaki ndi Tirasi.
3 A synowie Gomerowi: Aschenaz, i Ryfat, i Togorma.
Ana aamuna a Gomeri anali: Asikenazi, Rifati ndi Togarima.
4 A synowie Jawanowi: Elisa, i Tarsis, Cytym, i Dodanim.
Ana aamuna a Yavani anali: Elisa, Tarisisi, Kitimu ndi Rodanimu.
5 Od tych rozdzielone są wyspy narodów po swych ziemiach; każdy według języka swego, i według pokolenia swego, w narodziech swoich.
(Amenewa ndiwo makolo a anthu okhala mʼmphepete mwa nyanja. Awa ndi ana a Yafeti monga mwa mafuko a mu mitundu yawo, uliwonse ndi chiyankhulo chake).
6 A synowie Chamowi: Chus, i Micraim, i Put, i Chanaan.
Ana aamuna a Hamu anali: Kusi, Miziraimu, Puti ndi Kanaani.
7 Synowie zaś Chusowi: Seba, i Hewila, i Sabta, i Regma, i Sabtacha. A synowie Regmy: Seba i Dedan.
Ana aamuna a Kusi anali: Seba, Havila, Sabita, Raama ndi Sabiteka. Ana aamuna a Raama anali: Seba ndi Dedani.
8 A Chus spłodził Nemroda, który począł być możnym na ziemi.
Kusi anabereka Nimurodi amene anali wankhondo wamphamvu kwambiri pa dziko lapansi.
9 Ten był możnym myśliwcem przed obliczem Pańskiem; przetoż się mówi: Jako Nemrod możny myśliwiec przed Panem.
Iye anali mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova; nʼchifukwa chake anthu ali ndi chisudzo, chakuti, “Ndiwe mlenje wamphamvu kwambiri pamaso pa Yehova monga Nimurodi.”
10 A początek królestwa jego był Babel, i Erech, i Achad, i Chalne w ziemi Senaar.
Malo oyambirira a ufumu wake anali Babeli, Ereki, Akadi ndi Kaline. Malo onsewa anali mʼdziko la Sinara.
11 Z tej ziemi wyszedł Assur, i zbudował Niniwe, i Rechobot miasto, i Chale.
Atachoka mʼdziko limeneli anapita ku Asiriya kumene anakamanga Ninive, Rehoboti-Iri, Kala,
12 Także Resen, między Niniwe i między Chale; to miasto jest wielkie.
ndi Reseni, mzinda waukulu umene uli pakati pa Ninive ndi Kala.
13 Micraim też spłodził Ludyma, i Hananima, i Laubima, i Neftuhyma.
Igupto ndiye kholo la Aludi, Aanami, Alehabu, Anafutu,
14 I Patrusyma, i Chasluchyma, ( z których poszli Filistynowie, ) i Kaftoryma.
Apaturusi, Akasilu ndi Akafitori (kumene kunachokera Afilisti).
15 Chanaan też spłodził Sydona pierworodnego swego, i Heta.
Kanaani anabereka mwana wake wachisamba, Sidoni, ndipo anaberekanso Ahiti;
16 I Jebusa, i Amorra, i Gergesa.
Ayebusi, Aamori, Agirigasi;
17 I Hewa, i Archa, i Syma.
Ahivi, Aariki, Asini,
18 I Arada, i Samara, i Chamata, skąd się potem rozrodziły domy Chananejczyków.
Aaravadi, Azemari ndi Ahamati. Pambuyo pake, mafuko a Akanaani anafalikira ponseponse,
19 A granice Chananejskie były od Sydonu idąc do Gerary, aż do Gazy, aż wnijdziesz do Sodomy i Gomorry, i Adamy, i Seboima, aż do Lazy.
mpaka ku malire a Kanaani. Malirewo anachokera ku Sidoni kulowa cha ku Gerari mpaka ku Gaza, ndi kulowa ku Sodomu, Gomora, Adima ndi Zeboimu mpaka ku Lasa.
20 Ci są synowie Chamowi w familijach swych, w językach swych, w ziemiach swych, w narodziech swych.
Amenewa ndiwo ana aamuna a Hamu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe amakhala ndi mitundu yawo.
21 A Semowi, ojcu wszystkich synów Heberowych, bratu Jafeta starszego, urodzili się synowie.
Semu amene anali mkulu wake wa Yafeti nayenso anabereka nakhala kholo la Eberi.
22 Synowie Semowi: Elam i Assur, i Arfachsad, i Lud, i Aram.
Ana aamuna a Semu anali: Elamu, Asuri, Aripakisadi, Ludi ndi Aramu.
23 Synowie zaś Aramowi: Hus, i Hul, i Geter, i Mesech.
Ana aamuna a Aramu anali: Uzi, Huri, Geteri ndi Mesaki.
24 Arfachsad zaś spłodził Selecha, a Selech spłodził Hebera.
Aripakisadi anabereka Sela, ndipo Selayo anabereka Eberi.
25 A Heberowi urodzili się dwa synowie: imię jednemu Faleg, iż za dni jego rozdzielona jest ziemia; a imię brata jego Jektan.
A Eberi anabereka ana aamuna awiri: Wina anamutcha Pelegi chifukwa pa nthawiyo anthu a pa dziko lapansi anagawikana. Dzina la mʼbale wake linali Yokitani.
26 Jektan też spłodził Elmodada, i Salefa, i Hasarmota, i Jarecha.
Yokitani anabereka Alimodadi, Selefi, Hazari-Maveti, Yera,
27 I Adorama, i Uzala, i Dekla.
Hadoramu, Uzali, Dikila,
28 I Hebala, i Abymaela, i Sebaja.
Obali, Abimaeli, Seba,
29 I Ofira, i Hewila, i Jobaba: ci wszyscy są synowie Jektanowi.
Ofiri, Havila ndi Yobabu. Onsewa anali ana aamuna a Yokitani.
30 A było mieszkanie ich od Mescha idąc, do góry Sefar na wschód słońca.
Chigawo chimene ankakhala chinayambira ku Mesa mpaka ku Seferi, ku dera la mapiri chakummawa.
31 Cić są synowie Semowi w domach swych, w językach swych, w ziemiach swych, w narodziech swych.
Amenewa ndiwo ana a Semu monga mwa mafuko ndi ziyankhulo zawo, mʼmadera omwe ankakhala ndi mitundu yawo.
32 Teć są domy synów Noego, według pokolenia ich, i w narodziech ich, i od nich rozdzielone są narody na ziemi po potopie.
Amenewa ndiwo mafuko a ana aamuna a Nowa monga mwa mibado ya mitundu yawo. Mitundu yonse ya anthu inatuluka mwa iwowa ndi kufalikira pa dziko lonse lapansi chitatha chigumula chija.

< Rodzaju 10 >