< Wyjścia 3 >

1 A Mojżesz pasł trzodę Jetra, świekra swego, kapłana Madyjańskiego; i zagnał trzodę na puszczą, a przyszedł do góry Bożej, do Horeb,
Tsono Mose amaweta ziweto za mpongozi wake Yetero, wansembe uja wa ku Midiyani. Tsiku lina iye anazitsogolera kupita ku chipululu ndipo anafika ku phiri la Mulungu lotchedwa Horebu.
2 I ukazał mu się Anioł Pański w płomieniu ognistym, z pośrodku krza; i widział, a oto, kierz gorzał ogniem, a on kierz nie zgorzał.
Kumeneko mngelo wa Yehova anaonekera kwa iye mʼmalawi amoto mʼchitsamba. Mose anaona kuti ngakhale chitsambacho chimayaka koma sichimanyeka.
3 Tedy rzekł Mojżesz: Pójdę teraz, a oglądam to widzenie wielkie, czemu nie zgore ten kierz.
Tsono Mose anati mu mtima mwake, “Ine ndipita komweko ndikaone zodabwitsazi, chitsamba sichikunyeka chifukwa chiyani?”
4 A widząc Pan, iż szedł patrzać, zawołał nań Bóg z pośrodku onego krza, mówiąc: Mojżeszu, Mojżeszu! A on odpowiedział: Otom ja.
Yehova ataona kuti Mose anapatuka kuti adzaonetsetse, Mulungu anamuyitana Mose kuchokera mʼchitsambamo nati, “Mose! Mose!” Ndipo anayankha, “Wawa.”
5 Tedy rzekł: Nie przystępuj sam; zzuj buty twe z nóg twoich: albowiem miejsce, na którem ty stoisz, ziemia święta jest.
Mulungu anati, “Usayandikire kuno. Vula nsapato zako, pakuti malo amene wayimapo ndi opatulika.”
6 Zatem rzekł: Jam jest Bóg ojca twego, Bóg Abrahamów, Bóg Izaaków, i Bóg Jakóbów; i zakrył Mojżesz oblicze swe, bo się bał patrzać na Boga.
Mulungu anati, “Ine ndine Mulungu wa makolo ako, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo.” Atamva zimenezi, Mose anaphimba nkhope yake chifukwa anaopa kuona Mulungu.
7 I rzekł Pan: Widząc widziałem utrapienie ludu mojego, który jest w Egipcie, a wołanie ich słyszałem przed przystawy ich; bom doznał boleści jego.
Yehova anati, “Ine ndaona ndithu mazunzo a anthu anga amene ali ku Igupto. Ndamva kulira kwawo chifukwa cha anthu amene akuwapsinja, ndipo ndakhudzidwa ndi masautso awo.
8 Przetoż zstąpiłem, abym go wybawił z ręki Egipskiej i wywiódł go z ziemi tej do ziemi dobrej i przestronnej, do ziemi opływającej mlekiem i miodem, na miejsce Chananejczyka, i Hetejczyka, i Amorejczyka, i Ferezejczyka, i Hewejczyka, i Jebuzejczyka.
Choncho ndabwera kuti ndiwapulumutse mʼdzanja la Aigupto, kuwatulutsa mʼdzikolo ndi kukawalowetsa mʼdziko labwino ndi lalikulu, dziko loyenda mkaka ndi uchi, kwawo kwa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
9 A teraz oto krzyk synów Izraelskich przyszedł przed mię: i widziałem też ich ucisk, którym je Egipczanie uciskają.
Ine ndamva ndithu kulira kwa Aisraeli, ndipo ndaona mmene Aigupto akuwazunzira.
10 Przetoż teraz, pójdź, a poślę cię do Faraona, abyś wywiódł lud mój, syny Izraelskie z Egiptu.
Kotero tsopano, pita. Ine ndikukutuma kwa Farao kuti ukatulutse anthu anga, Aisraeli mʼdziko la Igupto.”
11 I rzekł Mojżesz do Boga: Któżem ja, abym szedł do Faraona, a wywiódł syny Izraelskie z Egiptu?
Koma Mose anafunsa Mulungu, “Ine ndine yani kuti ndipite kwa Farao ndi kukatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto?”
12 I rzekł Bóg: Oto, będę z tobą, a to miej na znak, żem cię ja posłał: Gdy wywiedziesz ten lud z Egiptu, będziecie służyć Bogu na tej górze.
Ndipo Mulungu anati, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo ichi chidzakhala chizindikiro kwa iwe kuti ndine amene ndakutuma; Ukadzatulutsa anthu anga mʼdziko la Igupto, udzapembedza Mulungu pa phiri lino.”
13 I rzekł Mojżesz do Boga: Oto, ja pójdę do synów Izraelskich, i rzekę im: Bóg ojców waszych posłał mię do was: Jeźli mi rzeką: Które jest imię jego? Cóż im odpowiem?
Mose anati kwa Mulungu, “Ngati ndipita kwa Aisraeli ndi kukawawuza kuti, ‘Mulungu wa makolo anu wandituma kwa inu,’ ndipo iwo nʼkukandifunsa kuti ‘Dzina lake ndi ndani?’ Tsono ine ndikawawuze chiyani?”
14 Tedy rzekł Bóg do Mojżesza: Będę który Będę. I rzekł: Tak powiesz synom Izraelskim: Będę posłał mię do was.
Mulungu anati kwa Mose, “NDINE AMENE NDILI. Izi ndi zimene ukanene kwa Aisraeli: ‘NDINE wandituma kwa inu.’”
15 I mówił jeszcze Bóg do Mojżesza: Tak rzeczesz do synów Izraelskich: Pan, Bóg ojców waszych, Bóg Abrahamów, Bóg Izaaków, i Bóg Jakóbów posłał mię do was; toć imię moje na wieki, i to pamiętne moje od narodu do narodu;
Mulungu anatinso kwa Mose, “Ukanene kwa Aisraeli kuti ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake, ndi Mulungu wa Yakobo, wandituma kwa inu.’ Ili ndilo dzina langa mpaka muyaya, ndipo mibado ya mʼtsogolomo izidzanditchula ndi dzina limeneli.
16 Idźże, a zgromadź starsze Izraelskie, i mów do nich: Pan, Bóg ojców waszych, ukazał mi się, Bóg Abrahamów, Izaaków i Jakóbów, mówiąc: Wspominając wspomniałem na was, i widziałem, co się wam działo w Egipcie.
“Pita, ukawasonkhanitse akuluakulu a Israeli ndipo ukati kwa iwo, ‘Yehova, Mulungu wa makolo anu, Mulungu wa Abrahamu, Isake ndi Yakobo, anandionekera ndipo akuti Iye wadzakuyenderani ndipo waona mmene Aigupto akukuzunzirani.
17 I rzekłem: Wyprowadzę was z utrapienia Egipskiego do ziemi Chananejczyka, i Hetejczyka, i Amorejczyka, i Ferezejczyka, i Hewejczyka, i Jebuzejczyka, do ziemi opływającej mlekiem i miodem.
Choncho wanenetsa kuti adzakutulutsani mʼdziko la Igupto, dziko la masautsoli kupita ku dziko la Akanaani, Ahiti, Aamori Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi.’
18 Tedy usłuchają głosu twego, a pójdziesz ty i starsi Izraelscy do króla Egipskiego, i rzeczecie do niego: Pan, Bóg Hebrajczyków, zabieżał nam; przetoż teraz niech pójdziemy proszę w drogę trzech dni na puszczą, abyśmy ofiarowali Panu, Bogu naszemu.
“Akuluakulu a Israeli akakumvera. Kenaka iwe ndi akuluakuluwo mukapite kwa mfumu ya Igupto ndipo mukanene kuti, ‘Yehova, Mulungu wa Ahebri, wakumana nafe. Tsono tikukupemphani kuti mutilole tipite pa ulendo wa masiku atatu mʼchipululu kuti tikapereke nsembe kwa Yehova Mulungu wathu.’
19 Ale ja wiem, że wam nie pozwoli król Egipski odejść, jedno przez możną rękę.
Koma Ine ndikudziwa kuti mfumu ya Igupto sikakulolani kuti mupite pokhapokha Ine nditayikakamiza.
20 A tak wyciągnę rękę moję, i uderzę Egipt wszystkiemi cudami mojemi, które będę czynił w pośrodku jego: a potem wypuści was.
Tsono Ine ndidzatambasula dzanja langa ndi kukantha Aigupto ndi zodabwitsa zanga zimene ndidzazichita pakati pawo. Zikadzatha izi, Iye adzakulolani kuti mupite.
21 I dam łaskę ludowi temu w oczach Egipczanów: i stanie się, gdy wychodzić będziecie, że nie wynijdziecie próżni.
“Ndipo ine ndidzafewetsa mtima wa Aigupto pa anthu anga, kotero kuti mukadzatuluka simudzapita wopanda kanthu.
22 Ale wypożyczy niewiasta u sąsiadki swojej, i u gospodyni domu swego, naczynia srebrnego, i naczynia złotego, i szat; i włożycie je na syny wasze, i na córki wasze, i złupicie Egipt.
Mkazi aliyense adzapemphe Mwigupto woyandikana naye ndiponso mkazi amene akukhala mʼnyumba yake, kuti amupatse ziwiya za siliva ndi golide ndiponso zovala zimene mudzaveka ana anu aamuna ndi aakazi. Ndipo potero mudzawalanda zonse Aiguptowo.”

< Wyjścia 3 >