< Amosa 7 >

1 To mi ukazał panujący Pan. Oto tworzył szarańczę, gdy najpierwej począł odrastać potraw, gdy oto potraw był po pokoszeniu królewskiem.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Yehova ankasonkhanitsa gulu la dzombe nthawi imene gawo la zokolola za mfumu linali litakololedwa kale ndipo mbewu zachiwiri zinali zitangoyamba kumera kumene.
2 A gdy zjadły trawę ziemi, rzekłem: Panujący Panie! sfolguj proszę; bo któż zostanie Jakóbowi, gdyż maluczki jest?
Dzombelo litadya zomera zonse za mʼdzikomo, Ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, khululukani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
3 I żałował Pan tego; a rzekł Pan: Nie stanie się.
Kotero Yehova anakhululuka. Yehovayo anati, “Izi sizidzachitika.”
4 Tedy mi ukazał panujący Pan, a oto panujący Pan wołał, że sprawę swoję powiedzie ogniem, a spaliwszy przepaść wielką, spalił i część królestwa Izraelskiego.
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: Ambuye Yehova ankayitana malawi a moto kuti alange anthu. Motowo unawumitsa nyanja yakuya ndi kupsereza dziko.
5 Tedym rzekł: Panujący Panie! przestań proszę; bo któż zostanie Jakóbowi, gdyż maluczki jest?
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Ambuye Yehova, chonde ndikukupemphani, lekani! Kodi Yakobo adzapulumuka bwanji? Iye ndi wofowoka kwambiri!”
6 I żałował Pan tego, a rzekł panujący Pan: I toć się nie stanie.
Kotero Yehova anakhululuka. Ambuye Yehova anati, “Izinso sizidzachitika.”
7 Potem ukazał mi, a oto Pan stał na murze według sznuru zbudowanym, w którego ręku było prawidło.
Zimene Iye anandionetsa ndi izi: Ambuye anayima pambali pa khoma lomangamanga, mʼmanja mwake muli chingwe chowongolera khoma.
8 I rzekł Pan do mnie: Cóż widzisz Amosie? I rzekłem: Prawidło. Tedy rzekł Pan: Oto Ja położę prawidło w pośrodku ludu mego Izraelskiego, a już mu więcej nie będę przeglądał.
Ndipo Ambuye anandifunsa kuti, “Amosi, nʼchiyani ukuonachi?” Ine ndinayankha kuti, “Chingwe chowongolera khoma.” Ndipo Yehova anati, “Taona, Ine ndikuyika chingwe chowongolerachi pakati pa anthu anga, Aisraeli; sindidzawalekereranso.
9 Bo wyżyny Izaakowe spustoszone będą, a świątnice Izraelskie zburzone będą, gdy powstanę przeciwko domowi Jeroboamowemu z mieczem.
“Malo achipembedzo a Isake adzawonongedwa ndipo malo opatulika a Israeli adzasanduka bwinja; ndidzagwetsa nyumba ya Yeroboamu ndi lupanga langa.”
10 Tedy posłał Amazyjasz, kapłan Betelski, do Jeroboama, króla Izraelskiego, mówiąc: Sprzysiągł się przeciwko tobie w pośrodku domu Izraelskiego, tak, iż ziemia nie może znieść wszystkich słów jego.
Pamenepo Amaziya wansembe wa ku Beteli anatumiza uthenga kwa Yeroboamu mfumu ya Israeli kuti, “Amosi akukuutsirani chiwembu pakati pa Aisraeli. Dziko silingalekerere zonena zake zonsezo.
11 Bo tak mówi Amos: Jeroboam od miecza umrze, a Izrael zapewne do więzienia z ziemi swojej zaprowadzony będzie.
Pakuti zimene Amosi akunena ndi izi: “‘Yeroboamu adzaphedwa ndi lupanga, ndipo Israeli adzapita ndithu ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”
12 Potem rzekł Amazyjasz do Amosa: O widzący! uchodź, uciekaj do ziemi Judzkiej, a jedz tam chleb, i tam prorokuj;
Ndipo Amaziya anawuza Amosi kuti, “Choka, mlosi iwe! Bwerera ku dziko la Yuda. Uzikalosera kumeneko ndipo anthu a kumeneko azikakudyetsa.
13 Ale w Betelu więcej nie prorokuj; bo to jest świątnica królewska, i dom królewski.
Usanenerenso ku Beteli, chifukwa kumeneko ndi malo opatulika a mfumu ndiponso ndi malo a nyumba yachipembedzo yaufumu.”
14 Tedy odpowiedział i rzekł do Amazyjasza: Nie byłem ja prorokiem, nawet ani synem prorockim; alem był skotarzem, a zbierałem figi leśne.
Amosi anayankha Amaziya kuti, “Ine sindine mneneri kapena mwana wa mneneri; koma ndine woweta ziweto, ndiponso mlimi wa nkhuyu.
15 Ale mię Pan wziął, gdym chodził za bydłem, i rzekł do mnie Pan: Idź, prorokuj ludowi memu Izraelskiemu.
Koma Yehova ananditenga ndikuweta nkhosa ndipo anati, ‘Pita ukanenere kwa anthu anga Aisraeli.’
16 Teraz tedy słuchaj słowa Pańskiego. Ty mówisz: Nie prorokuj w Izraelu, i nie każ w domu Izaakowym;
Tsono imva mawu a Yehova. Iwe ukunena kuti, “‘Usanenere zotsutsa Israeli, ndipo siya kulalikira motsutsa nyumba ya Isake.’”
17 Przetoż tak mówi Pan: Żona twoja w mieście nierząd płodzić będzie, a synowie twoi i córki twoje od miecza polegną, a ziemia twoja sznurem będzie podzielona, a ty w ziemi splugawionej umrzesz; lecz Izrael zapewne zaprowadzony będzie do więzienia z ziemi swojej.
“Tsono zimene akunena Yehova ndi izi: “‘Mkazi wako adzasanduka wachiwerewere mu mzindamu, ndipo ana ako aamuna ndi aakazi adzaphedwa ndi lupanga. Munda wako udzayezedwa ndi chingwe ndi kugawidwa, ndipo iwe mwini udzafera mʼdziko la anthu osapembedza Mulungu. Ndipo Israeli adzatengedwa ndithu kupita ku ukapolo, kutali ndi dziko lake.’”

< Amosa 7 >